Wednesday, January 20, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Kachali asayang’anire Bungwe la zisankho’

by Johnny Kasalika
22/12/2012
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bungwe lounikira za ufulu wa Amalawi komanso mgwirizano wa mabungwe pa zisankho adzudzula mtsogoleri wa dziko lino posankha wachiwiri wake Khumbo Kachali kukhala mkulu yoyang’anira bungwe la zisankho la Electoral Commission (EC).

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Mabungwe a Malawi Watch ndi Malawi Electoral Support Network (Mesn) ati uku n’kuika khoswe pamkhate chifukwa Kachali ndi chipani chake cha PP adzapikisana nawo pachisankho cha 2014 chomwe a EC akuyendetsa.

Mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wachibadwidwe la Malawi Watch, Billy Banda, kudzanso mneneri wa bungwe lowona za zisankho la Malawi Electoral Support Network (Mesn), Steven Duwa, ati ngati Banda sasintha ganizoli ndiye kuti iwo sadzapita kuchisankho cha 2014 chifukwa izi ndi zokonza kale.

Zitangodziwika kuti Pulezidenti Joyce Banda wasankha wachiwiri wake kuti asenze udindo woyang’anira bungweli, bungwe la European Union (EU) lidachititsa mtsutso pankhani ya ufulu wachibadwidwe ndipo pamtsutsowo mkulu wa EC, Maxon Mbendera, adadabwanso ndi ganizo la boma kotero wafunsa mlangizi wa mtsogoleri wa dziko lino pa malamulo, Anthony Kamanga, kuti awafotokozere momwe agwirire ntchito ndi Kachali.

Ndime 76 (4) ya malamulo oyendetsera dziko lino imati: “Pogwira ntchito kapena kuyendetsa udindo wawo malinga ndi ndime ino bungwe loyendetsa chisankho silizikakamizidwa kapena kuopsezedwa ndi munthu aliyense.”

Apa Billy Banda adati zomwe wachita mtsogoleriyu poswa malamulo a dziko lino atha kutengeredwa kubwalo la milandu chifukwa malamulowo si a munthu mmodzi. “Zachitikazi ndi zosakomera Amalawi ndipo Amalawi salola zimenezi. Akumbukire bwino kuti m’boma la DPP Amalawi adakwiya pomwe Bingu wa Mutharika adatseka bungwelo.

“Zikuonetseratu kuti mtsogoleriyu ali ndi zolinga zolakwika chifukwa sakutsatsa malamulo. Khumbo Kachali, yemwe amusankhayo, akufunanso atadzaimira nawo m’masankho ndiye zingatheke kuti nayenso akhale pamphika?” akufunsa Banda.

Iye wati ngati izi sizisinthidwa, bungwelo limema Amalawi kuti achite zionetsero posonyeza kukwiya kwawo komanso kuti asadzavote.

Mogwirizana ndi Banda, Duwa wati wakwiya ndi ganizoli chifukwa bungwelo limayenera ligwire ntchito modziimira palokha.

Iye wati bungwe lawo lalembera kalata mtsogoleriyu kuti asinthe ganizo lake.

“Timenya nkhondo mpaka izi zisinthidwe. Ngati sabweza ganizo lawo ndiye sitidzavota,” adatero Duwa.

Koma mneneri wa boma, Moses Kunkuyu, yemwenso ndi nduna yofalitsa nkhani, wati palibe chachinyengo chilichonse chomwe chingachitike chifukwa Kachali sagwira ntchito ku EC.

“Udindo umene wachiwiri kwa Pulezidenti wapatsidwa sikukhudzana ndi chilichonse cha chisankho. Iwo ali pakhomo poti ngati a EC akufuna thandizo ndi zina zoyendetsera zisankho azikapeza wachiwiri kwa Pulezidenti.

“Udindowu udali m’manja mwa a Pulezidenti ndiye iwo awupereka kwa wachiwiri wawo. Amabungwe ngati sakumvetsa afunse, si bwino kumangolankhula kuti achoke pampando chikhalirecho sadamvetse chomwe chachitika,” adatero Kunkuyu.

Kachali wakhala akudzudzulidwa ndi amabungwe komanso Amalawi kuti samalankhula bwino ndipo akuyenera kuchotsedwa pa mpando wa wachiwiri kwa pulezidenti.

Potsegulira chipatala ku Lupaso m’boma la Karonga, iye adadzudzula anthu omwe amadzudzula iye ndi Pulezidenti Banda kuti akuyendayenda kwambiri ponena kuti ‘samayenda m’makomo mwa amanu kapena abambo anu.’

Kachali adakhudzidwanso ndi nkhani yosowetsedwa kwa mabedi 13 omwe adatengedwa pachipatala cha Mponera ndi kuwapititsa ku Mzimba komwe panthawiyo kumachitika zisankho zapadera za aphungu a ku Nyumba ya Malamulo.

Kaamba zimenezi, Amalawi ambiri akukaika ngati Kachali ndi munthu woti angamudalire kuti akhoza kuyendetsa zinthu mokomera Amalawi onse mosakondera.

Malinga ndi Billy Banda, kaamba ka zomwe Kachali adachita, sikungakhale kulondola kumupatsa udindo ngati umenewu chifukwa Amalawi sangamukhulupirirenso.

Previous Post

JB achotsa Kachali ku EC

Next Post

Yaya is 2012 African Player of the Year

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post

Yaya is 2012 African Player of the Year

Trending Stories

  • Kenani: We cannot just watch the house burning

    Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Fake injury claims soar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Doctors sound SOS on health workers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Csec, Isama want clarity on schools’ closure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
Political Uncensored

Maddening chaotic virus

January 17, 2021
Emily Mkamanga

Chakwera has to instill unity

January 17, 2021
People’s Tribunal

Perilous times and the need for accountability

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.