Sunday, July 3, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Kusowa kwa mpikisano n’kwachabe’

by Johnny Kasalika
01/09/2012
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pali mantha kuti zipani za m’dziko muno zingayoyoke ngati makatani ngati mipando yonona yachipani monga wa pulezidenti ndi wachiwiri wake ipitirire kukhala yongotola popanda wopikisana naye ku misonkhano yaikulu ya zipani.

Izi zaunikidwa ndi otsogolera zitukuko kumidzi ena ndi katswiri pandale potsatira zochitika kumsonkhano waukulu wa chipani cha People’s Party (PP) komwe mpando wa pulezidenti ndi wachiwiri wake kuchigawo cha kumpoto padalibe kupikisana.

Kusapezeka opikisana m’mipandoyo kudapereka danga kuti mwini chipanichi, yemwenso ndi mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda adutse popanda omugwedeza.

Naye wachiwiri kwa Banda, Khumbo Kachali adadutsa moyera.

M’boma lomwe langopita kumene la DPP, mwini chipanicho komanso yemwe adaali pulezidenti, Bingu wa Mutharika samachititsa msonkhano waukuluwu n’komwe, m’malo mwake iye amangoloza anthu m’maudindo a m’chipanicho.

Chitsanzo, Mutharika adaloza Hetherwick Ntaba kukhala mneneri wachipani.

Mtsogoleri wakale yemwenso adali pulezidenti m’chipani cha UDF, Bakili Muluzi atangotula udindo kwa Friday Jumbe kudali kukokanakokana mpaka pano pomwe chipanichi chagawikana.

Zitadziwika kuti kukhala msonkhano waukulu kuchipani cha PP, anthu ena monga mkulu wina wa bizinesi, Caesar Fatch, adabwera poyera kuti adzapikisana ndi Banda.

Koma poyandikira chisankhocho, Fatch adalengeza kuti wazisiya, ati adzayeseranso kutsogoloku.

Malinga ndi operekera ndemangawa, izi ndizo zikuchititsa kuti zipani za m’dziko muno zizisokonekera pomwe pulezidenti wachipanicho wachoka paudindo chifukwa ofuna mpandowo amakhala akukokana, ena n’kumathiothoka m’chipani.

Katswiri wa pa zandale, Blessings Chinsinga wati zipanizi zitamakhala ndi msonkhanowu n’kupezekanso olimbirana nawo m’maudindo onse, achipani si bwezi mavuto omwe adachitika ku UDF ndi DPP atachitika.

“Izi si zachilendo m’dziko; ngakhale m’maiko akunja mavutowa alipo. Koma mathero a zonse, chipani chimatha chifukwa anthu amayamba kukokana pomwe pulezidentiyo wachoka pampando.

“Ndibwino mipandoyi idziphangiridwa chifukwa pomwe pulezidenti wachoka, amene adayamba kupikisana naye ndiwo amakhala patsogolo,” adatero Chinsinga.

Makiyi Matukuta, mkulu wa bungwe la Malawi Carer ku Mayani m’boma la Dedza, wati anthu kumeneko adali odabwa kumva kuti Banda wadutsa pampando wa pulezidenti popanda opikisana naye.

“Padzikhala kupikisana; anthu amakhala ndi chidwi kumva zomwe opikisanawo akonza. Zateremu ndiye kuti ufune usafune mtsogoleri wanu amakhala yemwe wadutsayo.

“Izi zimapha chidwi cha anthu ena omwe amafuna adzasankhe mtsogoleri yemwe amukonda,” adatero Matukuta.

Previous Post

JB rebuffs MPs on salary hike

Next Post

Start a mastermind group

Related Posts

Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Next Post

Start a mastermind group

Opinions and Columns

Editor's Note

MPs’ houses to cost taxpayers K60bn

July 3, 2022
My Thought

Women underutilise digital platforms

July 3, 2022
Big Man Wamkulu

Her body count is too high, should I dump her?

July 3, 2022
Search Within

We should start discussing ideas

July 3, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Alliance partners talk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MP Chihana flops at Sadc elections

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima opens pandora’s box

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Her body count is too high, should I dump her?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCP, UTM opt for peaceful discussions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.