Monday, March 1, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

A maufulu ayamikira MCP

by Bobby Kabango
11/09/2015
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akatswiri andale kudzanso mabungwe oimira ufulu wa anthu mdziko muno ayamikila chipani chachikulu chotsutsa boma cha Malawi Congress Party (MCP) powonetsa chitsanzo chabwino kwambiri potsata ndale za demokalase posankha anthu m’maudindo kupyolera mnjira yovomelezeka ya chisankho.

Chakwera (wachiwiri kuchokera ku manja) limodzi ndi mkazi wake Monica komanso akuluakulu ena kumsonkhanowo
Chakwera (wachiwiri kuchokera ku manja) limodzi ndi mkazi wake Monica komanso akuluakulu ena kumsonkhanowo

M’miyezi iwiri yotsana ya July kudzanso August chaka chino, MCP   yachititsa zisankho mu zigawo za kumwera ndi pakati. Ndipo m’menemo chaika anthu atsopano m’mipando yosiyasiyana oyendetsa chipanichi mzigawozo.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Katswiri wa ndale ku sukulu ya ukachenjede ya University of Malawi chigawo cha Chancellor College a Mustapha Husseni, ati zomwe ikuchita MCP ndiye zoyenera komanso zofunika kwambiri pa ulamuliro wa demokalase mchipani.

“Chipanichi mpofunika kuchiyamikira pazomwe chikuchitazi. Chikuchita ndale zololerana za-’intraparty democracy’, ndipo ife tingoti asaleke zimenezi chifukwa kumeneku ndiye kulimbitsa chipani mnjira yoyenera,” atero a Husseni.

Malinga ndi mneneli wa MCP a Jessie Kabwira,  chipanichi chichititsanso chisankho chonga chomwechi ku chigawo cha kumpoto. Iwo ati akuchita zimenezi kuti chipanichi chikhale cholimba, ndicholinga chakuti pomadzafika nthawi ya chisankho chachikuru chosankha prezidenti wadziko, aphungu, kudzanso makhansala mu 2019, chidzakhale cha mphamvu kwambiri m’madera onse adziko lino.

Mkulu wa Centre for the Deveopment of People (Cedep) , a Gift Trapence,  sadabise mau kukhosi ponena kuti zimenezi sizachilendo ai, kaamba kakuti ndikofunikiradi  kutero, maka poyang’anila kuti eni ake a zipani za ndale ndi anthu wamba omwe ndiwochuruka.MCP_women_dancing

“Zotsatira zake nzakuti zinthu zikamayenda motero, anthu ambiri amakhala nacho chikhulupiliro chipani choterocho. Iwo amadziwa kuti pakutero icho  chikutsatsa njira zabwino za democracy. Ndiponso izi sizifunika mchipani mokhamo ai, komanso ngakhale dziko lonse,” adatero a Trapence.

Nawonso a Timothy Mtambo, a Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR), potsilira ndemanga afotokoza kuti MCP yawonetsa kukhwima nzeru mu ndale za demokalase poika anthu m’maudindo mchipanichi kudzera mnjira yovomelezeka yachisankho.

“Zoonadi iyi ndi njira yabwino kwambiri, kusiyana ndikungoloza ndi chala kapena kumangosankhana ndi pakamwa pokha.  Kuwonjezera pamenepa, ife tikupempha kuti zisathere pa maudindo ang’onoang’ono okhawa  ai,  komanso ngakhale wa pulezident ndi ena otere, zidzikhalanso chimodzimodzi. Pamenepa sitikunena MCP yokha ai, komanso zipani zonse za ndale mdziko muno,” atero a Mtambo.

A Mtambo anatinso ndizodabwitsa kuti MCP yomwe inkakanitsitsa kubweretsa ndale za demokalse mu ulamuliro wake wa  chipani chimodzi,  lero lino ikuposa zipani zina, pokhala patsogolo kuwonetsa chitsanzo chabwino pa ndale za zipani zambiri mdziko muno.

A Mtambo anadzudzulanso mchitidwe omwe akuti zikuchita zipani zina mdziko muno, posankha mwana kaya mchimwene wake wa pulezident wa chipanicho kukhala mulowa malo, pomwe mtsogoleriyo akutula pansi udindo.

“Ngakhale kuti mdziko muno muli ufulu wakuti wina aliyense akhoza kupikisana nawo pa udindo wina uliwonse, komabe, mchitidwe okhala ngati waufumu, osiilana udindo muzipani za ndale ukukhumudwitsa anthu, komanso kuwopseza chitetezo cha ndale za democray.”

“Zoterezi sizabwino nkamodzi komwe. Ndipo zitheretu. Apatu  sitikunena muchipani cha ndale chokha ai, komanso ngakhale dziko lonse la Malawi. Tisawumilize anthu kuchita zomwe mwina iwo sakufuna. Alekeni otsatila chipani  asankhe okha munthu yemwe akumufuna kuwatsogolera mchipanimo.  Ndiye tikawonetsetsa, komanso kunena mwa chilungamo poyelekeza ndi zipani zina,  zimenezo sitinaziwone pakali pano mu MCP. Pachifukwachi ndithu tikuwayamikira komanso kuwalimbikitsa kuti zimenezi apitilize,” adatero Mtambo.

Previous Post

‘Zilango zophweka zivulaza maalubino’

Next Post

Panazale samakololapo!

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Flames (in red) in action against Zimbabwe in a 2017 Afcon qualifier last month

Panazale samakololapo!

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021
People’s Tribunal

When blood of citizens is on head of leaders

February 28, 2021

Trending Stories

  • chisale1 | The Nation Online

    Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MIN coy on K18bn MZ youth centre

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • TUM insists strike continues

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.