Sunday, February 28, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Achitira zadama mu basi

by Martha Chirambo
04/06/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Anthu ena okhala mumzinda wa Mzuzu akhala akuchitira za dama m’mabasi omwe adaimikidwa kumsika wa Zigwagwa pafupifupi miyezi inayi yapitayi.

Mabasiwa, salinso m’manja mwa kampani ya Axa chifukwa banki ya FDH idawagulitsa kwa mkulu wina wa bizinesi yemwe adawaimika ku Zigwagwako poyembekezera kuwagulitsa ndi kuwaphwasula ena mwa iwo.

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

basi | The Nation Online
Imodzi mwa basi amachitiramo zadamayo

Komatu anthu ena apezerapo mwayi wochitiramo za chiwerewere maka yomwe idali ndi magalasi osaonekera mkati, tintedi.

Msangulutso udatsinidwa khutu kuti izi zakhala zikuchitika madzulo komanso usiku ndipo kuti anthuwa amalipira kangachepe kuti apeze mwayi wodzithandiza m’basimo.

Komatu si anthu a zadama okhawa omwe amapumira m’mabasiwo, ngakhalenso ena osowa kogona, adatenga mabasiwo ngati nyumba zogona alendo.

Pomwe Msangulutso udakazungulira pamalopo udapeza mlonda Chimwemwe Kachali yemwe adavomereza kuti wakhala akupezerera anthu akuchita chiwerewere mu imodzi mwa mabasiwo makamaka usiku.

“Anthu amatengerapo mwayi chifukwa ndi yosaonekera mkati ndiye zomwe amachitazo sizimaoneka kunja. Chifukwa choti chitseko chake sichitsekeka, anthu ankangolowamo,” adatero Kachali.

Iye adakanitsitsa zoti adalandirapo ndalama kuchokera kwa anthuwa.

“Mwina popeza miyezi yapitayo tidalipo awiri ndi mnzanga, ndiye kuti mwina ndi yemwe amalandira ndalama;  koma ine sindidalandireko kanthu chifukwa ambiri mwa anthu omwe amachitira zadama mmenemo adali anthu woti timawadziwa ndithu,” adatero Kachali.

Iye adaonjezera kuti zikuoneka kuti ngakhale komwe mabasiwo adali asadagulidwe ndi bwana wake mchitidwewu umachitika chifukwa adabwera ali ndi makondomu ogwiritsidwa ntchito mwa zina.

Apa adatinso masiku ena amapezanso makondomu ogwiritsidwa kale ntchito omwe anthuwo amawataya akamaliza zadamazo.

“Idafika nthawi yoti anthu amakuwa akamadutsa pano kuti m’mabasimu mutuluka mwana ndipo ena amati aphwasulidwe kapena kugulitsidwa mwachangu,” adalongosola Kachali.

Iye adati zitafikapo abwana ake adayesa kuitseka ndi mawaya kuti anthu asamalowe koma sizidathandize chifukwa anthuwo adadula mawayawo.

“Nthawi zina ndikati ndikayendere basi pakati pausiku ndimapeza mwagona anyamata achilendo. Zikatero ndimawathamangitsa. Ambiri mwa iwo amakhala oti athamangitsidwa m’nkhalango ndipo alibe kolowera,” adatero Kachali.

Pocheza ndi tsamba lino, mwini ma basiwo George Biyeni adati adagula mabasi asanu omwe adali a kampani ya Axa kuchokera kubanki ya FDH ndipo adalemba alonda ake awiri oyang’anira mabasiwo koma mmodzi adasiya ntchito.

Biyeni adati mphekesera yoti m’mabasiwo makamaka ya tintediyo mumachitika za dama idamupeza ndipo adangoganiza zoyitseka ndi mawaya kuti anthuwo asamalowemo.

“Ndimati ndikalowa m’basimo, mumaoneka kuti anthu amachitamo zawo ndithu, koma ndikafunsa sindimayankhidwa bwinobwino,” adatero Biyeni.

Iye adati basi yomwe izi zimachitika kwambiriyo waiphwasula tsopano ndipo yomwe yatsala pamalopo ndi yoti omwe adawagulitsawo aikhonza kukonzekera kupita nayo ku Blantyre.

Biyeni adaonjezera kuti n’zovuta anthu a zadamawa kugwiritsa ntchito basi inayo chifukwa mwini wake adaikamo anthu ake angapo omwe akugona momwemo poilondera kwinaku akuikhonza.

Ndipo polankhulapo mneneri wa polisi mchigawo cha ku mpoto Peter Kalaya adati ofesi yake sidalandirepo dandaulo pa nkhaniyi.

“Tikadauzidwa tikadafufuza ndipo ochita zadamawo akadaimbidwa mlandu wa idle and disorderly—kuchita zadama malo osayenera,” Kalaya adatero. 

Previous Post

Sweet revenge: Silver are Airtel Top 8 champs

Next Post

Teresa Ndanga triumphs in Misa-Malawi polls

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
Ndanga being interviewed by members of the media

Teresa Ndanga triumphs in Misa-Malawi polls

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Court has declared Escom a private firm

    Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K1.7bn Chisale assets seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What the hell is APM doing with BJ?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC alleges threats, intimidation from investor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.