Sunday, March 7, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Adona Hilida akadangobwera

by Tadeyo
27/12/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Ngakhale pa Wenela padali zovuta, malo aja timakonda padali kuphulika nyimbo.

Ine nilibe pulobulemu

RelatedHeadlines

Akana ndalama za Covid-19

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

Nilibe pulobulemu….

Chifukwatu timayembekezera kuti wotisiyayo mtembo wake ufika masana a tsiku limenelo.

Titakhala pamalopo, adabwera mkulu wina akuthamanga.

tadeyo

“Akuluakulu,tiyeni mukandithandize kukhazikitsa mtima pansi bambo a malemu, akufika kumene kuchokera kwawo kwa Govala,” adatero mkulu uja, thukuta lochita kusamba.

Tidakhamukira komweko! Koma mkulu adavuta.

“Mwana wanga Boyisi waferanji? Boyisi anditumizira bulangete kuchoka ku Joni ndani? Ndikuti osandigwira!” adali kulira mkuluyo.

“Pepani, pepani,” wina ankayesera kumutonthoza.

Mkulu adali ndi mavuvu! “Osandigwira! Boyisi waferanji mwana wanga? Bwanji sunandifonere kuti unditsanzike? Osandigwira ineeeeee!”

Anthu okwana 10 adakwanitsa kumukhazika pansi. Adali kufwenthera ndipo ine ndidakhala moyandikana naye.

“Mwamwa kale tiyi?” adandinong’oneza mkuluyo.

Abale anzanga, matchona amayenera kubwera kumudzi akakhalakhala kunjako.

Nkhani idayala nthenje pa Wenela usiku umenewo kusiwa idali ya matchona.

“Koma mtchona wamkulu ndi Adona Hilida! Makhrisimasi awiri ndithu ali mliyenda! Ndalama ali nazo,” adatero Gervazzio.

“Ali ku exile! Anyamata ambiri amakhala ku exile asanalande ulamuliro koma Adona Hilida adathawira kunja ulamuliro utawasempha, ntchito za manja awo poboola mipopi ya chuma zitawachitira umboni,” adatero Abiti Patuma.

“Muli ndi umboni wanji kuti zikuwakhudza? Mudaliko?” adafunsa mkulu amene adali naye tsiku limenelo.

“Mufunanso umboni wotani kuposa zomwe zikuonekeratuzi? Adathawiranji? Nanga anthu onse akuwatchula Adona Hilidawa angakhale kuti akulota?” adayankha Abiti Patuma.

Abale anzanga, inetu zimandisempha.

“Ndipo akadangobwera nthawi ya Khrisimasiyi chifukwatu ndiye chochita sangachisowe. Akhoza kumagulitsa nawo mabaluni ngakhalenso makombola awandawa. Chochita sichingasowe,” adatero Gervazzio.

“Komanso anthu onsewa akuti ndalamazo zidali zakuti Polisi Palibe idzaluzire mpando wonona. Onsewa ngamisala? Akuopa chiyani Adona Hilida? Akadangobwera kuti mlandu wa munda tidzaukambire pamunda pawo pomwepo,” adatero Abiti Patuma.

Kwa ine, ndingothokoza kuti sindili mtchona ngati Adona Hilida. Ndimapuma mpweya mopanda kucheuka! Kusankha n’kwanga kuti ndisangalale Khrisimasi kapena ayi. Pajatu kwathu kwa Kanduku timakhulupirira kuti chisangalalo cha Khrisimasi chidalipo kuyambira kale, Yesu asadabadwe.

Koma izotu sindizitengera kwenikweni pozindikira kuti uzimu ndiwo ufunika.

Sindikulalikira, koma ndi bwino kuthokoza kuti taonanso Khrisimasi ina! Ndi bwino kumayamika Mulungu chifukwa mwamwayi n’kutsetserekera mu 2016. Zaka ndiye zikukhamukira ku 2019 kuti tidzaone Adona Hilida ndi Polisi Palibe akuthotha Moya Pete ndi Dizilo Petulo Palibe.

Gwira bango upita ndi madzi! n

Previous Post

Chaos in Thyolo, Mulanje land dispute

Next Post

Manet+ cautions govt on proposed hospital fees

Related Posts

covid relief | The Nation Online
Nkhani

Akana ndalama za Covid-19

March 6, 2021
Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
Next Post
Chiradzulu District Hospital: Manet+ fears users fees would prevent others from acessing services at a hospital such as this

Manet+ cautions govt on proposed hospital fees

Opinions and Columns

My Diary

Musowa voice missing yet needed

March 6, 2021
Off the Shelf

Off the Shelf 5 years on

March 6, 2021
Back Bencher

Let the teachers have their Covid-19 risk allowances

March 6, 2021
Guest Spot

Ensuring quality education for Malawian girls

March 6, 2021

Trending Stories

  • Lowe: We are trying to find potential markets

    Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SKC ‘intervenes’ on youths’ demos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt, TUM gloves off

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Let the teachers have their Covid-19 risk allowances

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.