Tuesday, March 2, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Afuna kudzikhweza nsanje itakula

by Steven Pembamoyo
10/06/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Apolisi ya Mponela ku Dowa amanga mayi wa zaka 24 Ketrina Paulo pomuganizira kuti amafuna kudzikhweza ponyansidwa ndi mwamuna wake yemwe adafuna kudya ndalama za utenanti ndi mkazi amene adalekana naye.

Mneneri wapolisiyo, Kondwani Kandiado, watsimikiza izi ponena kuti adamanga mayiyo pamlandu wofuna kudzipha zomwe zimatsutsana ndi ndime 229 ya malamulo a dziko lino koma koma amutulutsa pa belo chifukwa ali ndi ana amapasa ofunika chisamaliro koma  akaonekera kukhothi posachedwa.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

suicide ILLUSTRATION 10 JUNE | The Nation Online
Wojambula wathu kuyerekeza momwe zidalili

“Tidamanga mayiyo titalandira uthenga kuchoka kuchipatala komwe amati akalandire thandizo mwamuna wake atamupulumutsa. Akuti nkhani zake n’zabanja ndiye tamupatsa belo uku tikufufuza kuti tikhale ndi umboni wodzapita nawo kukhothi,” adatero Kandiado.

Malinga ndi mmodzi mwa anthu a m’mudzi mwa Msakambewa, Emmanuel Mazaza, banja loyamba la Skalioti Dzakande wa zaka 34 lidatha zitamveka kuti bamboyo adali ndi chibwenzi ndipo amafuna kutenga chiwiri.

Iye adati ngakhale zidali choncho, bamboyo sadasunthike ndipo mkazi woyambayo, Angela Kefa yemwe ali naye ana atatu atapita kwawo, iye adakatenga mkazi wachiwiriyo n’kulowana naye.

Dzinja lapitalo, bamboyo adakafuna ntchito ya utenanti ndipo adayipeza paesiteti ina yapafupi ndi kwawoko kenako adatenga mkazi wakeyo n’kupita naye kuntchitoko.

Monga mwa ndondomeko ya ntchito ya utenanti, banjalo lidagwirizana ndi mwini esiteti ndalama zomwe adzalipatse ntchito ikadzatha ndipo pomwe msika wa fodya uli mkati, bwanayo adalipira antchito ake kuphatikizapo banjalo.

Banjalo litalandira chachikulu cha Dedza komwe akulandira chithandizo cha mankhwala.

“Chomwe chidachitika n’choti mayiyo adapita kwa mnzake kukacheza ndipo pochoka kumeneko adazindikira kuti macheso palibe pakhomopo. Mayiyu adapita kunyumba yoyandikana nayo komwe adakabwereka machesowo kuti ayatsire moto.

“Nthawi yomwe adali kunyumba inayo kukabwereka macheso, mwamuna wakeyo adamutsatira kunyumba inayo kukamuuza kuti apite kunyumba kuti akakambirane nkhani ina,” adatero Manda.

Iye adati mayiyo adabwerera kunyumbako koma atangofika, bamboyo adatenga mpeni wakuthwa ndi kucheka nawo pakhosi pamkazi wakeyo ndipo zitatero bamboyo adathawa.

“Chifukwa chomwe adapangira izi sichikudziwa ndipo panopa kafukufuku wathu alimkati kuti tigwire bambo ameneyu ndipo tikamugwira akayankha mulandu ovulaza munthu,”  adafotokoza Manda. n

Previous Post

Gaba is Hope for Cancer ambassador

Next Post

Margaret Ali: Upholding children and women’s rights

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Ali in line of her duty to protect women and children

Margaret Ali: Upholding children and women’s rights

Opinions and Columns

My Turn

Tackling global slowdowns

March 1, 2021
People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021

Trending Stories

  • Olela: We are excited

    K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • We won’t give Up—Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Lhomwe chiefs divided on paramount chief

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.