Saturday, July 2, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

by Martha Chirambo
04/06/2022
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mayi wina yemwe ndi mlembi kunthambi yoyang’anira za umoyo pakhonsolo ya mzinda wa Mzuzu, anadabwitsa anthu masiku apitawa pomwe anasamukira paofesi ya bwanamkubwa wa khonsoloyo chifukwa wakhala osalandira malipiro ake kwa miyezi iwiri. 

Ndinawe Mtambo wa zaka 28 anagona panja pa maofesi a khonsoloyo kwa masiku awiri.

Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo

Pakhondepo, mayiyo anaika firiji, bedi loyala bwino komanso akatundu ena pokakamiza kuti khonsoloyo ikonze mavuto a za chuma omwe yakhala ikukumana nawo kuchoka m’chaka cha 2017.

“Ndikudandaula chifukwa anandichotsapo msanga. Ndimafuna ndizikhala pompo mpaka unduna wa maboma aang’ono komanso mtsogoleri wa dziko lino alowererepo,” anatero a Mtambo.

Polankhula ndi Msangulutso, iwo adati a khonsoloyo anakawatenga mayi awo ndi omwe anadzachotsa katunduyo.

A Mtambo adaonjezeranso kuti akhonsoloyo adatuma munthu wawo kuti amutengere kuchipatala cha amisala kuti akamuyeze.

“Akuofesi anapitanso kwa mayi anga kukawapempha kuti awapatse chilolezo chonditengera kuchipatala cha amisala koma ndinawakanira chifukwa kuchipatala sakakamizana,” adatero iwo.

Iwo adati a khonsoloyo adawapatsa malipiro awo a miyezi iwiri atatha masiku awiri akugona panjapo.

“Nditangoyamba kugona panja anthu ena amandinena kuti ndili ndi mavuto pomwe ena anandisilira ndipo ankafuna kuchita ngati ine koma ndidawakaniza chifukwa zomwe ndinachitazo zinali za ukadziotche,” analongosola motero a Mtambo.

Iwo adati panthawiyo ankalawilira m’mawa n’kukasamba paseli pa maofesiwo pomwe chakudya amaphikanso pomwe panali katundu wawo.

Apa anaonjezera kuti ngati zinthu sizisintha pakhonsoloyo adzachitanso za mtunduwo koma zagulu lalikulu osati zayekha.

“Ndikukhulupilira kuti uthenga wa mavuto omwe tikukumana nawo wafika tsopano ndipo papezeka njira zowathetsera,” anatero a Mtambo.

Iwo anati chodandaulitsa kwambiri n’choti ngakhale mabungwe okongoza anthu ndalama akumawasala akangomva kuti amagwira ntchito kukhonsolo ya mzinda wa Mzuzu ndipo sakumawapatsa ngongole.

Mavuto a zachuma afika posauzana pa khonsoloyo chifukwa pomwe Msangulutso umacheza ndi a Mtambo muofesi yake, kunafikanso amayi ena wogwira ntchito pamalopo omwe anadandaulanso kuti alibe kalikonse.

Ogwira ntchito ena pa khonsoloyo ati akhala miyezi isanu osalandira malipiro awo.

Mneneri wa khonsolo ya Mzuzu a Macdonald Gondwe anatsimikiza kuti a Mtambo anayamba kugona panja Loweruka ndipo akhonsolo anampatsa malipiro ake a miyezi iwiri Lamulungu.

“Anayamba kugona kuno Loweruka, tinampatsa malipiro ake m’mawa wa Lamulungu, koma chodabwitsa n’choti madzulo a tsiku lomwelo anapitanso kwawo kukatenga katundu woonjezera monga firiji ndi zofunda komanso zofunda,” analongosola a Gondwe.

Malinga ndi a Gondwe aliyense ndi wodabwa paofesipo chifukwa Mtambo sanachiteko zimenezi. A Gondwe anatsimikizanso kuti ngakhale a khonsolo anapempha kwa mayi ake kuti a Mtambo apite kuchipatala, izi sizinachitike.

Previous Post

Mr. President, talk is cheap

Next Post

Tadala Chinkwezule: One of 2022 Top 100 Female Lawyers in Africa

Related Posts

Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Nkhani

Woimba abedwa mumzinda wa mzuzu

May 28, 2022
Next Post

Tadala Chinkwezule: One of 2022 Top 100 Female Lawyers in Africa

Discussion about this post

Opinions and Columns

My Diary

God-fearing nation, my foot!

July 2, 2022
Off the Shelf

APM digging a hole for DPP

July 2, 2022
Guest Spot

‘Fighting corruption is not the easiest task of any govt’

July 2, 2022
My Turn

Following spouse is no crime

July 1, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Alliance partners talk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • New VP houses draw criticism

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Malawi credit Status at risk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Britain squeezes Zuneth Sattar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima opens pandora’s box

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.