Saturday, March 6, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Agwidwa ‘ukapolo’ ku Ntchisi

by Danwood Chirwa
26/12/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Madzi achita katondo kwa T/A Malenga m’boma la Ntchisi komwe Gulupu Malenga, Peku Wakuda ndi Munkana aletsa anthu a m’mudzi mwa Peku Woyera kukhala nawo pa zochitika zilizonse m’derali kuphatikizapo maliro, ukwati komanso kupita kumsika wawo waukulu potsatira mkangano wa malo.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Nkhaniyi ikuti mfumu yaing’ono Peku Woyera idawina mlandu wa malo womwe udaweruzidwa ndi magulupu atatuwa.

Malinga ndi Peku Woyera, magulupuwa ataona kuti zake zayera pamlanduwu, adanenetsa kuti amkhaulitsa.

Akuti asayende: Peku Woyera
Akuti asayende: Peku Woyera

“Chilango chake anthuwa adagwirizana kuti ine ndi anthu a m’mudzi mwanga tisiye kukhala nawo pazochitika mpaka kutiletsa kupita kukagula zinthu kumsika wathu waukulu ati kaamba koti ndidawina mlanduwo,” idatero mfumuyo, yomwe dzina lake la pamsonkho ndi Tisiyenji Daniyele.

Mfumuyo idati anthuwa adaletsedwanso kukhala nawo pamisonkhano ya chitukuko.

“Ngakhale ana awaletsa kutenga nawo mbali pazamasewero, pomwe amayi awathamangitsa kumabanki a m’mudzi ndi makalabu a ulimi. Moti ndikulankhula pano mayi wina adamulanda katundu wosiyanasiyana pakhomo yemwe adagula patauni yathu yaing’ono,” Peku Woyera adatero.

Iye adati pano anthuwa akudalira msika waukulu wa Ng’ombe womwe uli pamtunda wa pafupifupi makilomita asanu.

Peku Woyera adati ngakhale nkhaniyi idatengeredwa kubwalo la milandu komwe adalamulidwa kuti azisonkhana nawo ndi anzawo, magulupuwo akanitsitsa kuchotsa chiletsocho.

“Ndife akapolo m’mudzi mwathu momwe,” adatero Peku Woyera.

Polankhulapo, gulupu Malenga adavomereza za nkhaniyi ndipo adati chidatsitsa dzaye kuti magulupu atatuwo apereke chiletso chokhwimachi ndi mwano womwe Peku Woyera adachita ponyozera zisamani zomwe amalandira.

Malenga adati mwachikhalidwe chawo, zilango monga izi zimaperekedwa kwa anthu amwano ndi cholinga choti aphunzire mwambo.

Iye adati mudzi wonse walandira chilangochi chifukwa udakhudzidwa pamkangano wa malowo.

“Ife tikufuna kuti mfumuyi ndi anthu ake azibwera kubwalo akalandira chisamani, koma akapitiriza mwano sitingachitire mwina koma kuwalanga powasala,” Malenga adatero.

Koma Clement Zindondo, mmodzi wa akuluakulu a bungwe lomwe si laboma lomwe likutengapo gawo pa achinyamata ndi chitukuko la Ntchisi Organisation for Youth and Development (NOYD), adati anthuwa akusowekera thandizo kaamba koti magulupawa awaphwanyira ufulu wawo wosonkhana ndi anzawo.

“Ife tikudabwa kuti bwanji magulupuwa sakulemekeza chigamulo cha bwalo la milandu? Apatu sakusamala za malamulo oyendetsera dziko lino ndipo ndikhulupirira kuti akhoti achitapo kanthu nkaniyi ikawapezanso,” Zindondo adatero.

Chilangochi nchotchuka zedi m’boma la Ntchisi ndipo mafumu ambiri atengeredwako kubwalo la milandu la majisitireti la Ntchisi chifukwa chophwanyira anthu ufulu wosonkhana ndi anzawo.n

Previous Post

TCC unpacks tobacco contract farming

Next Post

When Christmas spending finishes you off

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post

When Christmas spending finishes you off

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Chilima: There will be a Bill

    Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 vaccine in today

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • 2 testify in Itaye case

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.