Monday, March 8, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Agwira ‘onyoza’ mtsogoleri wa dziko lino

by Johnny Kasalika
24/11/2012
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

JB oct27 | The Nation Online Amayi awiri ati apolisi adawamanga sabata ikuthayi powaganizira kuti adanyoza mtsogoleri wadziko lino, Joyce Banda ndi chipani chake cha People’s Party (PP) ati atakana kulandira chovala chamakaka achipanichi kuti avinire mtsogoleriyu.

RelatedHeadlines

Akana ndalama za Covid-19

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

Amayiwa ati adakananso kulowa m’gulu la amayi anzawo omwe amavinira mtsogoleriyu pomwe adakayendera dera lawo.

Oganiziridwawa, Eliza Kusheni wazaka 26 ndi Dorothy Ng’onga wazaka 24 adatulutsidwa pabelo la bwalo lamilandu la Mwanza Magistrate Lolemba atakhala masiku asanu m’chitokolosi cha apolisi.

Wapolisi wamkulu ku Mwanza, Ellobiam Banda, adatsimikizira zakunjatidwa kwa awiriwo koma iye adati amayiwo sadamangidwe pochitira mtudzu mtsogoleri wadziko lino monga akunenera.

Iye adati kumangidwa kwa awiriwo kudadza malinga ndi kusagwirizana pakati pa iwo ndi amayi am’deralo.

“Amayi awiriwa agamulidwa pogwiritsa ntchito mawu onyoza.

Zikuganiziridwa kuti amayi awiriwa adanyoza mayi wina, Martha Mazinzi potsatira nsanje yomwe idakula,” adatero wapolisiyu.

Iye adati atangonjata amayiwo Lachinayi, oganiziradwawo adatulutsidwa pabelo Lolemba chifukwa apolisiwo adali otangwanidwa ndi mtsogoleri wa dziko lino pomwe amakayendera kumeneko.

Zotolera za apolisi zikutsutsana ndi zimene oganiziridwawo komanso mkhalakale wachipani cha DPP, Bright Kachingwe kumeneko akunena.

Ng’onga wati iye ndi mayi mnzakeyo adazizwa ndikumangidwa kwawo chifukwa patsikulo sadachitire mtudzu aliyense.

“Patsikulo timachokera kundende ya Mwanza pomwe tidakumana ndi amayi 6, mmodzi mwa iwo adavala chovala cha makaka achipani cha PP, ndipo ndidathirira ndemanga kuti chovalacho chidali chabwino,” adatero mayiyo.

Ng’onga adati atazindikira kuti zinthu zidayamba kutentha, iye ndi mnzake adachoka pamalopo pomwe adabisala m’golosale yomwe awiriwo amagwira ntchito.

Iye adati apolisi adabwera pamalopo kudzawanjata popanda zifukwa zokwanira.

Awiriwo adatulutsidwa pabelo posapereka chikole chilichonse. Bwalo lidalamula kuti awiriwo adzikawonekera kupolisi Lolemba lililonse.

Kachingwe adati chipani ndichokhudzidwa ndi kunjatindwa kwa awiriwo.

Previous Post

College of Medicine doctor gets AU Young Scientist Award

Next Post

Anti-piracy war rages on

Related Posts

covid relief | The Nation Online
Nkhani

Akana ndalama za Covid-19

March 6, 2021
Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
Next Post
The Nation Online Anti-piracy war rages on

Anti-piracy war rages on

Opinions and Columns

Search Within

Cut out the religious dogma from Covid-19 vaccines

March 7, 2021
Big Man Wamkulu

Won’t libido-boosting pills kill him?

March 7, 2021
Political Uncensored

Pulling rank…

March 7, 2021
People’s Tribunal

Ombudsman has challenged us all

March 7, 2021

Trending Stories

  • Protesting pay cut: Mathanga

    Court blocks RBM deputy governor salary cut

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • RBM sues Mulli, 4 others

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Police, DPP, ‘ignore’ court order

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.