Friday, May 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Akana ndalama za Covid-19

by Martha Chirambo
06/03/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Anthu ayera m’manja. Ndalama za Covid zatuluka. Komatu mayi wina mumzinda wa Mzuzu wakana kulandira ndalamazi akuti nzasataniki.

Mayiyo akuti ndalamayi ikatuluka aipereka kwa mnzake.

Malinga ndiGertrude Moses, mnzakeyo adamuuza kuti sangatenge ndalama zomwe a boma akupereka kuthandiza anthu pa chuma m’nyengo ino ya matenda a Covid 19 pa zifukwa zitatu.

“Anati ndalamazi ndi za sataniki komanso za kumidima chifukwa zangobwera osakhetsera thukuta,” adalongosola Moses.

Iye adatinso akuopa kulandira ndalamazi chifukwa mwina ndi nyambo ndipo mtsogolo muno aboma adzalengeza kuti  aliyense yemwe adalandira azikasamalira odwala matendawa.

Komatu si mayi yekhayu yemwe ali ndi maganizo achoncho chifukwa nawo omwe ankachita kalemberayu mumzinda wa Mzuzu adakumana nazo zambiri.

Malinga ndi mmodzi mwa omwe ankachita nawo kalemberayu, Mirriam Masangano makomo ambiri amabwenzedwa kuti ndondomekoyi ndi ya sataniki.

“Anthu ena ambiri adakananso kulembetsa maina awo chifukwa amati ali kale ndi ndalama ndipo ena olo mpanda sankatitsekulira,” adalongosola Masangano.

Iye adati mnzawo wina mpaka adalumitsidwa galu pogwira ntchitoyi.

Pomwe mnzake wina  Kiloshina Kampani adati m’makomo ena amalandiridwa ndi agalu omwe amawathamangitsa mpaka kugwa  ndi kuvulala.

“Tikukhulupilira kuti izi zidachitika chifukwa anthuwa adalibe uthenga wokwanira wokhudza ntchitoyi,” adalongosola Kampani.

Mneneri wa khonsolo ya mzinda wa Mzuzu, MacDonald Gondwe adati ngakhale khonsoloyo idayesetsa kulengeza pa mkuzamawu za kalemberayu, ambiri sadamvetsetse.

“Ndi zoona kuti ntchitoyi idakumana ndi zokhoma zambiri ndipo madandaulo ngosayamba kuchokera kwa omwe amagwira ntchitoyi komanso olandira,” adalongosola Gondwe.

Iye adati ena mwa omwe adakana kulandira ndalamazo, pakadalipano akuvutanso kuti alowe nawo mkaundula wa opindura nawo pa ndalamazi.

Pomwe Gilbert Kaponda yemwe amagwira ntchito ndi anthuwa mzinda wa Mzuzu  kuchokera ku unduna woona kuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo adatsimikiza kuti anthu awo adakumana ndi mavutowa.

Mmodzi mwa ogwira ntchito athu ankafuna kumenyedwa, bambo wa panyumbapo atamupezelera akumufunsa mafunso mkazi wake. Bamboyu amayesa kuti mkazi wake amafunsiridwa,” adalongosola Kaponda.

Anthu papafupifupi 199 000 m’dziko muno apindula nawo pa ndondomeko ya boma yomwe ikupereka ndalama zokwana K19.5 billion zothandizira anthu omwe kapezedwe kawo ka chuma kakhudzidwa kwambiri ndi matenda a Covid 19.

Ndalamazi ziperekedwa kwa miyezi itatu kwa anthu okhala madera a Zomba, Mzuzu , Blantyre ndi Lilongwe. Ndipo azilandira K35 000 pa mwezi.

Pomwe anthu a ku Lilongwe ndi Blantyre ayamba kale kulandira zawo, ku Mzuzu ndi Zomba sizidayambe.

Previous Post

Police, DPP, ‘ignore’ court order

Next Post

Bullets fine Kajoke over Flames camp

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Kajoke: It was irresponsible for me to break the Covid-19 protocols

Bullets fine Kajoke over Flames camp

Opinions and Columns

Business Unpacked

Fixing economy needs action, not rhetoric

May 19, 2022
Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022

Trending Stories

  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCTU pushes for 75% minimum wage hikeof

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Road traffic spot fines on way out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mayors may face ballots

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.