Friday, July 1, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Akhazikitsa lamulo Logonjetsera covid

by Steven Pembamoyo
15/08/2020
in Chichewa
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Boma lakhazikitsa lamulo lothandiza kulimbana ndi mlili wa Covid-19 loti akadaulo azaumoyo akuti ndi chida champhamvu pa nkhondo yolimbana ndi matendawa.

Lamulolo lakhazikitsidwa nyengo yomwe chiwerengero cha anthu opezeka ndi Covid-19 m’dziko muno chikuthamangira 5 000 ndipo ndichimodzi mwa ziwerengero zomwe zikuthamanga mu Africa.

Chiwerengero cha anthu opezeka ndi Covid-19 m’dziko muno chasuntha mwachangu kuchoka pa 1 038 ndi omwalira 13 malingana ndi zomwe udatulutsa unduna wazaumoyo pa June 27 2020 kufika 4 714 ndi omwalira 152 pa August 11 2020.

Izi zikutanthauza kuti pa mwezi umodzi ndi theka, chiwerengero cha opezeka ndi Covid-19 chaonjezekera ndi anthu 3 676 komanso omwalira 139.

Chiponda: Tikufuna kugonjeza Covid-19

 Malingana ndi nduna ya zaumoyo Khumbize Kandodo Chiponda, boma lidaona kuti n’chanzeru kuti likhazikitse lamulo lomwe lithandize polimbana ndi kukwera kwa chiwerengero cha anthu opezeka ndi matendawa.

“Sikuti lamuloli langobwera ayi, zidatengera kugundana mitu pakati pa unduna ndi nthambi zosiyanasiyana ndipo titakhutira kuti lamuloli likugwirizana ndi zolinga za dziko lino poteteza anthu ake ndipo tidalikhazikitsa pa August 8 2020,” adatero Chiponda.

Woimira boma pa milandu Chikosa Silungwe adati momwe zililimu chilichonse chatheka ndipo lamuloli lidayamba kale kugwira ntchito.

“Chomwe ndingapemphe n’choti anthu akhale ndi luntha lotsatira lamuloli chifukwa muli zilango zomwe opanga zosemphana nalo azilandira,” adatero Silungwe.

Zina zomwe lamulolo likunena n’zoti munthu akapezeka pagulu osavala masiki, azilipira ndalama zosachepera K10 000 kapena kukagwira ndende ya miyezi itatu.

Gawo lina likuti anthu sakuloledwa kukhala m’magulu a anthu oposa 10 ndipo misonkhano yonse yaletsedwa kupatula misonkhano yokhudza za Covid-19 basi.

 Milandu ina monga ya eni galimoto zonyamula anthu omwe akweza munthu wopanda masiki, eni malo ololeza anthu kuchitirako m’sonkhano woletsedwa, eni malo omwera mowa, komanso ophikira zakudya osatsata malamulo azilipira ndalama zosaposa K100 000 kapena kugwira ndende ya miyezi itatu.

Eni malo omwera mowa akuloledwa kutsegula kuyambira 2 koloko masana mpaka 8 koloko madzulo ndipo onse ofuna mowa azingogula n’kukamwera kwawo pamene amene ali ndi malo odyerapo azionetsetsa kuti anthu akukhala motalikirana pakudya kapena azingogula n’kukadyera kwina.

Gawo lina la lamuloli likupereka mphamvu kwa nthambi ya zachitetezo malingana ndi khumbo la nduna kugwiritsa ntchito mphamvu zilizonse zofuna kuti anthu atsatire lamuloli.

Pazamaliro, lamulolo likulola anthu osaposa 50 okha omwenso azidziteteza moyenera popita kumaliroko, koma pa za nyumba zopemphereramo Silungwe adangoti anthu asamaposemo 10.

Mneneri wapolisi James Kadadzera adati apolisi amasowa lamulo lowamasula manja kuti azigwira ntchito yawo yoonetsetsa kuti anthu akutsatira ndondomeko zopewera Covid-19.

“Apapa zakhala bwino chifukwa tsopano tili ndi lamulo lomwe tizigwiritsa ntchito.

“Tionetsetsa kuti anthu akutsatira lamuloli. Popanda lamulo ntchito yathu imavuta kagwiridwe kake,” adatero Kadadzera.

M’mwezi wa April 2020, boma lakale lidayesa kukhazikitsa ndondomeko zopewera Covid-19 zomwe ina idali ya m’bindikiro (lockdown) koma chifukwa padalibe lamulo lililonse, mabungwe ndi anthu ena adakatenga ziletso ndipo ndondomekozo sizidagwire ntchito.

Kadaulo pa zaumoyo Maziko Matemba wayamikira lamulo latsopanoli ponena kuti lipatsa mphamvu apolisi ndi asirikali ankhondo kugwiritsa ntchito mphamvu zomwe amalephera kutulutsa pankhondo yolimbana ndi Covid-19.

“Iyiyi si nkhondo ya masewera ayi ndi nkhondo yaikulu. Mungokumbukira momwe zidayendera m’maiko ena, tsono pamafunika kachikwapu kuti anthu azindikile kukula kwa nkhondoyi,” adatero Matemba.

Naye George Jobe wa bungwe la Malawi Health Equity Network (Mhen) adati kupatula kuphunzitsa anthu za Covid-19, lamuloli ligwira ntchito yaikulu bola anthu alimvetsetse.

Mafumu monga Maseya ya ku Chikwawa, Mponela ya ku Dowa, komanso Chikulamayembe ya ku Rumphi adati lamulolo lafika kale m’midzi ndipo mafumu ali kalikiliki kufotokozera anthu awo.

Maseya adati poti n’kumayambiriro anthu akumvetsetsa pang’onopang’ono za lamuloli moti ena akulephera kumvetsetsa chosiyira kupita kutchalitchi pamene ena akadali kumwera mowa m’malo ogulitsira momwe mukukhala khamu la anthu.

“Ukayenda m’ziphikomu, kukuoneka kuti anthu sadafike povomereza zomwe lamulo likunena pa zakamwedwe, koma poti mwina lamulo silidakhazikitse tiona,” adatero Maseya.

Mponela adati nkhani yayikulu yomwe ikuvuta ndi yamaliro chifukwa anthu adakhazikitsa mwambo wamaliro ngati chikhalidwe ndipo amalingalira za ulemu omwe maliro amayenera kulandira.

Previous Post

Non-league basketball team’s project charms sports minister

Next Post

Sugar factory operational delay hits farmers

Related Posts

Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Nkhani

Woimba abedwa mumzinda wa mzuzu

May 28, 2022
Next Post

Sugar factory operational delay hits farmers

Opinions and Columns

Rise and Shine

Create your personal brand

June 30, 2022
Business Unpacked

We can do without some levies in fuel price

June 29, 2022
My Turn

US court threatens women’s rights

June 29, 2022
People’s Tribunal

Two years later and we are still singing same song

June 26, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Sattar: I have nothing to hide

    Britain squeezes Zuneth Sattar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Malawi credit Status at risk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nam cheated on SA trip

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ex-MPC boss sues for unfair dismissal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DPP disorder upsets speaker

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.