Saturday, May 28, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Akhoti anyanyala ntchito

by Staff Writer
14/01/2012
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mavenda 40 omwe adamangidwa mu mzinda wa Lilongwe sabata yathayi ali m’gulu la anthu zikwizikwi za anthu amene akhudzidwa ndi kunyanyala ntchito kwa anthu ogwira ntchito m’mabwalo amilandu m’dziko muno komwe kunayambika Lolemba lapitali.

Chifukwa chakusayenda kwa zinthu m’mabwalo amilanduwa iwowa alephera kupeza belo kapena chithandizo china chilichonse ndipo afinyikabe mpaka kunyanyala ntchitoku kutatha.

Onyanyala ntchitowa ati akuchita izi pofuna kukakamiza boma kuti liyambe kupereka malipiro omwe adagwirizana m’chaka cha 2006.

Apa akatswiri pa ndale, amabungwe komanso anthu otumikiridwa ndi mabwalowa ati boma likuyenera kulongosola izi madzi asadafike m’khosi.

Kuyambira Lolemba mabwalo amilandu adali otseka, ndipo pofika Lachitatu pomwe timasindikiza Tamvani, mabwalowo adali asadawatsegule.

Malinga ndi mkulu wa bungwe loona zaufulu wa anthu la Malawi Watch Billy Banda wati kunyanyala ntchitoko kwasonyeza kuti boma silikulabadira miyoyo ya anthu.

Banda wati ngati kunyanyalaku kungapitirire, Amalawi ambiri avutika chifukwa pali ena omwe sakuyenera kukhala kundende koma ali kumeneko chifukwa cha kunyanyala ntchitoku.

Mavenda 40 omwe adamangidwa ku Lilongwe pazipolowe amayenera kukaonekera kubwalo lamilandu Lolemba koma sizidatheke chifukwa cha sitalakayo.

Mneneri wa polisi m’chigawo chapakati, John Namalenga, Lachiwiri adavomereza kuti anthuwa adalephera kukaonekera kubwalo lamilandu chifukwa choti kumabwaloko kudali kotseka.

Iye adati kunyanyalaku kukapitirira ndiye kuti zitokosi zam’dziko muno zikhala zodzadza.

“Ngati anthu achuluka m’chitolokosi timakawasunga ku polisi za Kawale ndi Lingadzi. Koma ngati kunyanyalaku kungapitirire tisowa pogwira.

‘Kudzadzaku kungachitike ngati titamanga anthu ambiri pakamodzi chifukwa zimatheka kumanga anthu oposa 100 patsiku,” adatero Namalenga.

Mphunzitsi wa zandale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Joseph Chunga, wati uku ndikupha ufulu wachibadwidwe makamaka kwa anthu omwe ali m’manja mwa apolisi chifukwa amayenera kukaonekera kubwalo lamilandu kuti akapatsidwe belo kapena kuti akadziwike ngati ndi wolakwa pa mlandu omwe amangidwira.

“Monga mwa malamulo, pamayenera pasadutse maola 48 omangidwa asadakaonekere kubwalo lamilandu. Ngati izi sizidatsatidwe, ndiye kuti ufulu wako waphwanyidwa.”

Iye adati kunyanyalako kukapitirira pali chiopsezo kuti boma lingatengerepo mwayi chifukwa lidziwa kuti munthu akamangidwa sakaonekera kubwalo la milandu.

“Izi zikutanthauza kuti ulamuliro wotsatira malamulo watha,” adatero Chunga.

Ndipo Osman Chimenya wa ku Kanjedza mumzinda wa Blantyre adavomerezana ndi Chunga ndipo adati boma likuyenera kukwaniritsa mgwirizano wake ndi ogwira ntchitowa.

Erick Gomani wa ku Malewule kwa T/A Kapeni m’boma la Blantyre adaikira mang’ombe, ndi kuti anthuwa adalonjezedwa kuti apatsidwa malipiro atsopano kotero boma likuyenera kukwaniritsa.

Mneneri wa gulu lomwe likunyanyalali yemwenso ndi kalaliki wamkulu ku High Court mumzinda wa Blantyre, Austin Kamanga wati sasintha ganizo lonyanyala ntchito pokhapokha boma litayamba kupereka ndalama zomwe zidavomerezedwa ndi Nyumba ya Malamulo m’chaka cha 2006.

Iye adati malipiro a anthu omwe amagwira ntchito zina kumabwalo amilandu amavomerezedwa ndi nduna ya zachuma zomwe akuti zidachitika mu 2006 koma boma silidafune kukwaniritsa.

“Kuyambira 1997, malamulo akagwiridwe ka ntchito a ogwira ntchito kumabwalo amilandu amaunikidwa pakatha zaka zitatu, ndipo akaonedwa amatumizidwa kunyumba ya malamulo kuti aphungu akaunikire ndikuvomereza,” adatero Kamanga.

Mu 2006, Nyumba ya Malamulo itavomereza komanso nduna ya zachuma itavomereza, anthuwa akuti sadalandire malipiro atsopanowo ndipo kukokanakokana kudayambika.

Kamanga adaonjeza kuti: “M’chaka cha 2009, boma lidangolengeza kuti litionjezera malipiro ndi K15 pa K100 iliyonse koma sitikumvetsa kuti ndalama imeneyi imachokera pati?

“Tikufuna tiyambe kulandira ndalama zathu, apo ayi sitibwerera kuntchito,” adalumbira Kamanga.

Nduna ya zachuma, Ken Lipenga, samayankha lamya yake ya m’manja pomwe Tamvani imafuna kulankhula naye.

Koma iye adauza atolankhani Lachiwiri m’sabatayi kuti unduna wake ukukambirana ndi okhudzidwa kuti ayankhe mavuto a anthuwa.

Iye adati alankhulapo pa nkhaniyo akangomaliza kukambirana ndi mbali zokhudzidwa pa nkhaniyo.

Previous Post

Kuchoka kwa Phoya kutisokoneza, atero ena

Next Post

Now we know why Bingu’s doesn’t care

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post

Now we know why Bingu’s doesn’t care

Opinions and Columns

Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022

Trending Stories

  • His case heard in UK court: Sattar

    Acb explains Sattar miss

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kwacha gets 25% weaker

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AmaZulu complete signing Gaba

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gone but still in our midst

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Conforzi to invest K8.2bn in PPP venture

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.