Thursday, March 4, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Akhumudwa ndi kusowa kwa mnyamata wachialubino

by Steven Pembamoyo
05/02/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Magulu omenyera ufulu wa anthu komanso bungwe la anthu achialubino la Association for People with Albinism in Malawi (Apam) ati ndi okhumudwa ndi kusowa kwa mnyamata wa chialubino mwezi wa January m’boma la Mangochi.

Mneneri wapolisi m’chigawo cha kummawa Inspector Joseph Sauka watsimikiza kuti Daiton Saidi wa zaka 18 adasowa pa 27 January 2021 ndipo apolisi adamanga anthu atatu omwe akuwaganizira kuti ndiwo adasowetsa mnyamatayo.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ian Simbota APAM Pic Mana 2 | The Nation Online
Simbota: Chitetezo Chikhalepo

“Tawafunsa ndipo akuvomera koma sitilankhula zambiri chifukwa tikadafufuza ndiye tingasokoneze kafukufuku,” adatero Sauka.

Izi zikuchitika patangotha miyezi 7 chilowereni boma la Tonse Alliance lomwe munsanamira za kampeni yake inkatsindika mfundo yokhwimitsa chitetezo cha anthu achialubino.

Lonjezoli lidalandiridwa ndi manja awiri chifukwa lidabwera pomwe pafupifupi sabata ziwiri zilizonse kumasowa kapena kuphedwa munthu wachialubino ndipo mabungwe komanso maiko ankadzudzula dziko la Malawi chifukwa cholephera kuteteza anthuwo.

Koma Pulezidenti wa Apam Ian Simbota wati bungwelo ndi lodabwa kuti chisadathe ndi chaka chomwe, mchitidwewo wayambiranso.

“Mitima yathu idayamba kukhazikika chifukwa timakhulupilira kuti boma likwaniritsa lonjezo lake la pakampeni koma momwe zachitikiramu mantha athu abwereranso ndipo tikufuna chitetezo chathu chikhwime monga momwe adatilonjezera,” watero Simbota.

Mabungwe a Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) ndi Centre for the Development of People (Cedep) ati potsatira nkhondo yomwe yamenyedwa mmbuyomu, zosowetsa ndi kupha anthu achialubino zimayenera kutha.

“Nzomvetsa chisoni kuti kufika lero, msika wa ziwalo za anthu achialubino ukadalipo. Apolisi akuyenera kuchitapo kanthu kuti mchitidwewu uthe msanga,” yatero kalata yomwe mabungwewo atulutsa.

Mabungwewo ati boma likuyenera kuyamba kugwiritsa ntchito ndondomeko yotetezera anthu achialubino yomwe idakonzedwa mchaka cha 2015.

Mchitidwe osowetsa ndi kupha anthu achialubino udafika pachimake kuyambira m’chaka cha 2014 ndipo boma lidalamula kuti milandu yokhudza nkhanzazi iziweruzidwa ndi khothi lalikulu lomwe lili ndi mphamvu zopereka chilango chachikulu.

Kufikira lero, milandu yokhudza kusowetsa ndi kupha anthu achialubino yomwe idalembetsedwa mukhothi ilipo 169 ndipo milandu 43 mwa iyo idagamulidwa kale.

Mirandu 17 idatsekedwa pomwe milandu 40 ikadali mukhothi, ina iwiri yapsa kale kuti ikhoza kupita kukhothi pomwe milandu 62 ikadafufuzidwabe.

Chodabwitsa nchakuti chiyambireni kafukufuku wa polisi komanso komiti yomwe Pelezidenti wakale Peter Mutharika adakhazikitsa ndipo imatsogoleredwa ndi Dr Hetherwick Ntaba, msika waziwalo za anthu achialubino sudziwikabe komwe ulili.

Malingana ndi Sauka, Saidi adasowa pa 27 January 2021 ndipo amachokera mmudzi mwa Kate Kadewere kwa T/A Chowe m’boma la Mangochi.

Previous Post

Letter to Vladimir Putin, Xi Xinping

Next Post

Cementgate moves to High Court

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
mukhito mbilizi court | The Nation Online

Cementgate moves to High Court

Discussion about this post

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Economist warns on teachers’ risk allowance

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.