Sunday, January 24, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Akudyerera obwela’

by Bobby Kabango
05/08/2016
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

A malawi akhala akuingidwa ngati nkhuku m’maiko ena akafuna thandizo la chipatala, koma nzika zakunja kumadzawamwera mazira zikafika m’dziko muno ponama kuti ndi nzika za dziko lino.

Izitu zakhala zikuchitika chifukwa chosowa chiphaso cha unzika, koma lero mpumulo wafika kwa Amalawi pamene akhale ndi mwayi wokhala ndi chiphaso chosonyeza unzika wa dziko lino.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Kuthithikana m’zipatala zina kumadza chifukwa cha anthu a kunja
Kuthithikana m’zipatala zina kumadza chifukwa cha anthu a kunja

Zili chonchi malinga ndi ntchito yomwe bungwe la National Registration Bureau (NRB) poyamba kalembera wa unzika amene adayamba ndi akuluakulu aboma komanso maboma 11.

Monga akufotokozera Senior Chief Kanduku wa m’boma la Mwanza, boma lake limalandira nzika zambiri kuchokera m’dziko la Mozambique.

“Anthu pafupifupi atatu mwa 10 alionse amene amafuna thandizo lachipatala kuno amakhala a ku Mozambique. Vuto ndiloti kuyambira pa Zobue mpaka ku Tete m’dziko la Mozambique palibe chipatala, posowa kolowera, anthu adera limeneli amathandizidwa m’zipatala za dziko la Malawi,” adatero Kanduku.

“Ngakhale tayandikana ndi dzikolo, satilola kupita m’dziko lawo kukalandira thandizo la chipatala. Amalawi angapo akhala akuthamangitsidwa, ndipo suthandizidwa chifukwa anzathuwo ali ndi zitupa za unzika,” adaonjeza motero.

Naye Senior Chief Kabunduli ya m’boma la Nkhata Bay, adati kumeneko nzika za maiko a Tanzania zimalowa pafupifupi tsiku lililonse ndi kumalandira thandizo lomwe Amalawi amayenera kulandira.

“Akafika kuno amakhala ndi maina a Chimalawi zomwe ndizovuta kuwakaikira kuti si nzika zathu. Mankhwala pachipatala amatha mwachangu ife ndi kumavutika pamene iwo kwawo ali ndi zipatala zomwe zingawathandize,” adatero Kabunduli.

“Kungofika pa Chintheche pali anthu ambiri amaiko a Burundi, sangapitenso kwawo ndipo akulandira chithandizo chilichonse chomwe chimayenera chipite kwa Amalawi. Kwawo sungayerekeze kupanga zimenezi koma ifeyo amationa kupusa,” adaonjeza Kabunduli.

Kuti munthu ulandire thandizo lachipatala cha boma m’maiko monga Zambia, Zimbabwe, Mozambique ndi Tanzania, umayenera kuonetsa chitupa chosonyeza kuti ndiwe nzika koma kuno kwathu izi sizichitika chifukwa kulibe ziphasozi.

Monga akufotokozera Norman Fulatira yemwe ndi mneneri wa NRB, iyi mwina nkukhala mbiri yakale chifukwa Mmalawi weniweni azidziwika ndi chiphaso chomwe adulitse.

“Mavuto amenewa akhala mbiri yakale posakhalitsapa pamene ntchito yodula ziphaso za unzika yayamba. Gawo loyamba tayamba kupanga ziphaso za aphungu a Nyumba ya Malamulo, akuluakulu m’boma, komanso midzi 27 m’maboma 11,” adatero Fulatila.

Mabomawa ndi Chitipa, Mzimba, Nkhotakota, Lilongwe, Salima, Dowa, Mchinji, Blantyre, Mangochi, Chikwawa ndi Thyolo. Zitupazo azidula m’midzi iwiri pa boma lililonse.

“Ili ndi gawo loyamba, gawoli likufuna lingotithandiza momwe ntchito ikhalire, ili ngati ntchito yoyeserera kaye koma anthu alandira ziphaso zawo. Mudzi ulionse takonza zoyamba ndi anthu 200 ndipo gawoli likamatha, anthu 5 000 akhala ndi ziphaso zawo,” adatero mneneriyu.

Iye adati gawo lachiwiri la ntchitoyi, anthu 95 000 ndiwo adzakhale ndi mwayi wokhala ndi ziphasozi ndipo gawoli likuyembekezereka kudzatha mu December chaka chino.

Chaka chamawa, bungweli likuyembekezera kuti ntchitoyi idzafalikira dziko lonse pomwe anthu 9 miliyoni akuyembekezeka kulandira zitupa zawo.

Fulatira adati aliyense amene wakwanitsa zaka 15 ndiye akuyenera kudulitsa ziphasozi. Iye watinso ngati uli nzika ya dziko lino, uyenera kudulitsa ziphasozi posatengera zikhulupiriro zako kapena mpingo.

Naye mkulu wa bungwe loona zaumoyo la Malawi Health Equity Network (Mhen) George Jobe wati ntchitoyi ipindulira Amalawi komanso boma.

“Apapa ndiye kuti thandizo la mabungwe ndi boma lizipitadi m’manja mwa Amalawi enieni kusiyana ndi poyamba pamene timaphangirana ndi obwera,” adatero.

Kwa amene ataye chiphasochi akuti ayenera kudzalipira K3 500 kuti amupangirenso chiphaso china. Koma malinga ndi Fulatira, mtengowu ukhala ukusinthasintha.

Chiphasochi chizisiya kugwira ntchito pakatha zaka 10, kuchokera apo ndiye kuti mwini chiphasoyo azayenera kupangitsaso chiphaso china. n

Previous Post

Lack of capital, expertise chocks coal industry

Next Post

‘Nutrition issues need to be urgently addressed’

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post

‘Nutrition issues need to be urgently addressed’

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • High-profile official angered Wirima to quit

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi vs Uganda.

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Legendary Patani Mwase remembered

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Bottom Up

Thanks Team Onjezani Kenani; our turn now

January 23, 2021
My Thought

Cloud hangs on Mtambo’s head

January 23, 2021
Off the Shelf

Goodbye Trump, you were a joke

January 23, 2021
Back Bencher

Chakwera’s ‘politics’ rant was in bad taste

January 23, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.