Monday, June 27, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Akupindula ndi chimanga chachiwisi

by ESMIE KOMWA
15/08/2020
in Chichewa
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pamene alimi ambiri akugulitsa chimanga chouma pa mtengo wotsika, mlimi wa chimanga chachiwisi ku Area 25 m’boma la Lilongwe Kandida Kalisito akupha makwacha ndi chimanga chachiwisi. Mlimiyu ali ndi malo amene amaotcherapo chimanga chake pa munda pomwepo ndipo akuti nthawi zambiri amagulitsa chootcha chifukwa ndi m’mene muli phindu lochuluka. ESMIE KOMWA adacheza naye motere:

Kodi kulima chimanga chachiwisi mudayamba liti?

Ndidayamba ulimiwu mu 2002.

Nanga chidakuchititsani n’chiyani kuti muyambe ulimiwu?

M’chaka cha 2001 kunali njala kotero a bungwe lina la Katolika mogwirizana ndi la European Union(EU) anabwera kudzaphunzitsa anthu ulimi wothirira ndipo pa nthawiyo pa malo pano panali anthu okwana 14.

Mabungwewa anauza anthu oyambirirawo kuti awonjezere anthu ena omwe akufuna kuyamba ulimiwu ndipo ine ndinali m’gulu la anthu owonjezeredwawo.

Chiyambireni ulimi wa chimanga chachiwisiwu mwapindula motani?

Ulimiwu wandipindulira kwambiri chifukwa ndaphunzitsa ana anga atatu onse pano ali pa ntchito ndipo akudzidalira, ndamanga nyumba za lendi ndipo panopa chilakolako changa n’chogula galimoto.

Nanga chinsinsi chanu kuti muzipindula motere chagona pati?

Chinsinsi changa ndikusamalira bwino mbewuyi kuti ituluke ikuluikulu bwino ndi yapamwamba komanso kugulitsa china chootcha.

N’chifukwa chiyani mumagulitsa chimanga chachiwitsi osati kudikira kuti chiume?

Chimanga chouma chimakhala chotsika mtengo kwambiri kusiyana ndi chachiwitsi kotero kugulitsa chotero n’kungotaya mphamvu zako pachabe.

Tangoganiza panopa makamaka kwa ine ndimagulitsa kwambiri chootcha, chimanga chimodzi ndikumagulitsa pa mtengo wa K200, K150 ndi K100 pamene chouma pa kilogalamu ndi K200.

Kodi pa chaka mumalima kokwana kangati?

Kamakwana katatu koma ndimaonetsetsa kuti malo anga ndiwaike m’magawo ndikubzalanso nthawi zosiyana n’cholinga choti m’chaka chonse ndizikhala ndikugulitsa.

Nanga mumagwiritsa ntchito njira yanji ya mthirira?

Ndimagwiritsa ntchito ya m’makhwawa. Ndili ndi khwawa lalikulu, komanso ma pump amene ndimagwiritsa ntchito petulo kuti ndilize injini. Ndimalumikiza mapiyipi ku pampu ndipo mbali ina ndimalumikiza ingini. Mapayipi ena amatenga madzi mu mtsinje pamene ena amakathira madzi mu khwawa muja ndipo likadzadza ndimapatutsira ku mbewu pokumba timakhwawa ting’onoting’ono.

Kodi si ntchito yolemetsa imeneyi?

Ndiyophweka kusiyana ndiyogwiritsa ntchito ma water cane kapena ma treadle pump n’chifukwa chake tinasiya kugwiritsa ntchito kalekale zinthu zoterezi.

Ndinu munthu wa mayi koma mukuoneka mukuchita zinthu zomwe amayi ambiri sangachite, mungawalangize zotani amayi anzanu?

Ndimakonda kuwauza amayi anzanga kuti sakuyenera kumakhala amanja lende podalira amuna awo okha ndipo pakutero adzachepetsa umphawi m’dziko muno ndipo m’maanja awo. Chinthu china munthu ukakhala wokangalika umakhala ndi masomphenya ndipo umayetsetsa kuwakwaniritsa  pakutero umakhala munthu osangalala pamene ukakhala wa manja lende umakhala otsirira mpaka kalekale.

Nanga ndimavuto anji omwe mumakumana nawo mu ulimiwu?

Vuto limene timakumana nalo ndi la mbozi. Nthawi zina zikachulukitsa timayenera kupopera sabata iliyonse kuti tipulumutse mbewu zathu choncho ndalama yochuluka imalowa ku mankhwala. Vuto lina limene timakumana nalo chaka chilichonse ndi kuphwa kwa madzi mu mtsinje umene timatengako madzi makamaka m’miyezi yotentha.  Aunduna wa zamalimidwe anayamba kutikumbira damu kuti tisamakumane ndi mavuto oterewa, koma sanamalidzitse kotero tinakakonda akanamalizitsa kuti mwina vutoli lichepe.

Previous Post

So, teachers are important?

Next Post

Govt worries experts on Covid-19

Related Posts

Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Nkhani

Woimba abedwa mumzinda wa mzuzu

May 28, 2022
Next Post

Govt worries experts on Covid-19

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Two years later and we are still singing same song

June 26, 2022
Big Man Wamkulu

Wife’s relatives have taken over my house

June 26, 2022
My Thought

Stop cyber harassment

June 26, 2022
Candid Talk

Baby gender preference and disappointments

June 26, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Changaya: It is a
huge trade deal

    K243bn Malawi trade deal on rocks

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Veep status under spotlight

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wife’s relatives have taken over my house

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • CSOs demand Chilima, others’ resignation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DRTSS backs off on Movesa, pays fine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.