Friday, March 5, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Akuti akukumana Ndi womwalira

by Steven Pembamoyo
21/04/2019
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Maloza! Mtembo wa mtsikana uli m’nyumba, manda atakumbidwa, anthu ena amakumana naye akungozungulirazungulira pamsika komanso m’munda mwa makolo ake.

Anthu a m’mudzi mwa Mponda m’dera la mfumu Mduwa ku Mchinji komwe kwachitika nkhaniyi akuganiza kuti mtsikanayo, Violet Lubani, wa zaka 19 adachita kuphedwa m’masenga.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

fire | The Nation Online
Katundu wambiri wa banjalo waotchedwa

Violet amadandaula kuti diso likumupweteka ndipo adapita naye ku Kamuzu Central Hospital ku Lilongwe komwe adamuchita opareshoni, koma adamwalirira patangopita masiku ochepa.

Nyakwawa ndi mafumu adauzidwa komanso anthu adafika mwaunyinji wawo kudzakhudza malirowo.

Gulupu Mponda ikuti maloza adayamba kuoneka mtembo wa mtsikanayo utayamba kutuluka thovu m’kamwa, m’makutu ndi m’phuno.

“Nkhope ndi nkhungu lake zimasintha. Nkhope yake imaoneka ngati ya mzimayi wachikulire kwambiri, pakapita nthawi  imaoneka ngati ya mwamuna.

“Nkhungu lake limayera pambuyo pake kuda kwambiri,” idafotokoza motero gulupuyo.

Anthu akudabwa ndi malozazo amayi omwe adapita kukathyola ndiwo zamasamba m’munda mwa makolo amtsikanayo adatulukamo chothawa.

“Adatifotokozera kuti akumana ndi malemuyo m’mundamo. Anthu adathamangira ku mundako, koma sadakampezemo.

“Tonse tinadabwa, komanso kugwidwa mantha. Mwambo wa maliro udapitirira ngakhale anthu ambiri sadakondwe ndi zomwe zimachitikazo,” adatero Mponda.

Chipwirikiti chidayamba anthu ena atabweranso ndi uthenga woti akumana ndi mtsikanayo kumsika.

“Titaona kuti adzukulu ndi anthu ena okwiya ndipo akukambirana zochitira mtopola makolowo powaganizira kuti akukhudzidwa ndi imfa ya mtsikanayo, tidazembetsa anamalirawo kuopa kuti anthu awachita chipongwe.

“Mafumu adaitanitsa apolisi kaamba koti zinthu zidafika poyipa,” adatero Mponda.

Anthu okwiya adagwetsa nyumba ndi kuotcha katundu wa banjalo moti mmene apolisi amafika zinthu zambiri zidali zitaonongeka kale.

Mneneri wapolisi wa m’boma la Mchinji, Rubrino Kaitano, adati adapeza ziwawa zili mkati moti sakadachoka mpaka kuonerera kuika mtembo wa Violet m’manda.

Violet adamwalira pa April 12 ndipo adaikidwa pa April 13.

Padakali pano apolisi atsekera m’chitokosi anthu oposa 13 kaamba kogumula nyumba zitatu ndi kuotcha katundu wa banjalo.

Mponda adati chiikireni malirowo m’manda “anthu ambiri akukumanabe ndi mtsikanayo m’malo osiyanasiyana”.

Msangulutso suudathe kulankhula ndi banjalo kaamba koti lachoka m’mudzimo, komanso komwe lalowera sikukudziwika. n

Previous Post

Zinthu zitatu mu nkhuku imodzi ya Mikolongwe

Next Post

‘Ndidamuona koyamba mu Shoprite’

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post
tidakumana 2 | The Nation Online

‘Ndidamuona koyamba mu Shoprite’

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.