Friday, January 22, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Akwapula mphunzitsi wochita ‘chisembwere’

by Martha Chirambo
12/09/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Maphunziro a ana a Sitandade 8, adasokonera Lolemba pasukulu ya pulaimale ya Kalira, yomwe ili m’mudzi mwa Kanyera ku Mtakataka m’boma la Dedza.

Izi zidachitika pomwe wachiwiri kwa mphunzitsi wamkulu pasukulupo Owen Kalolo adakwapulidwa pomuganizira kuti amachita chibwenzi ndi mkazi wa mwini.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

mob | The Nation Online

Zidatengera apolisi ndi aphunzitsi anzake kumuleletsa. Ndipo aphunzitsi anzake adanenetsa kuti saphunzitsanso malire ake chitetezo chawo chibwerere m’chimake chifukwa wokwapula mphunzitsiyo sadanjatidwe.

Mwini mkaziyo Sitivero John, akuti adapita pasukuluyi ndi kukwapula mphunzitsiyo ndi waya yemwe kwinaku akumunena kuti amagona ndi mkazi wake iye ali ku South Africa.

Malinga ndi omwe adatitsina khutu pankhaniyi wa m’mudzimo, mapokosowo adayambika m’mawa wa Lolemba, aphunzitsi ali pa kamsonkhano kawo.

“Tidangoona kwatulukira bambo wolusayo atanyamula waya wa mtundu wa y16 ndi kumukwapula mphunzitsiyo,” adalongosola iye.

Iye adati apa mpomwe aphunzitsi anzake adalowererapo kuopetsa kuti akadamuvulaza kwambiri.

“Kuchoka apa kudabweranso apolisi a ku Mtakataka komanso mkulu woyan’ganira maphunziro kudera la Mankhamba kudzaziziritsa zinthu,” iye adatero.

Polankhulapo, mkulu woona za maphunziro m’bomalo, George Ngaiyaye adatsimikiza za nkhaniyi koma adati pakadalipano ana adayamba kuphunzira zomwe zikusonyeza kuti chitetezo cha aphunzitsi chilli m’malo mwake.

“Nkhaniyi tsopano ili m’manja mwa apolisi ndipo ana akuphunzirano bwino,” adalongosola Ngaiyaye.

Wachiwiri kwa mneneri wa polisi m’bomalo Cassim Manda yemwe adakafikako kusukuluyi adatsimikizira Msangulutso kuti chitetezo cha aphunzitsitsiwo chili m’malo mwake ndipo adayambanso kuphunzitsa.

Manda adati Kalolo ndi John akhala ali pa chinansi kwa zaka 6 ndipo ubale wawo umapitirirabe ngakhale pomwe John adapita m’dziko la South Africa.

“Koma nkhani idakhota pomwe mkazi wa John adampatsa Kalolo munda kuti alimepo zomwe sizidasangalatse abale ndipo adayamba kulankhula zoti awiriwo adali pa ubwenzi wamseri,” adalongosola Manda.

Malinga ndi Manda, John atabwera chaka chino, adayamba kufufuza ndipo adadikira kuti sukulu zitsegulire kuti akamukhape Kalolo nthawi ya sukulu ngakhale adalibe umboni.

“Pakadalipano tikusakasaka komwe kuli John komanso kusukuluko kwapita apolisi chifukwa John-yu adalonjeza kuti sasiyira pomwepa zaupanduzi,” adatero Manda.

Ndipo adanenetsa kuti sukuluyo siyidatsekedwe.

Kalolo yemwe ali ndi zaka 29, amachokera m’mudzi mwa Maliwa, Mfumu Chilikumwendo pomwe John wa zaka 35, amachokera m’mudzi mwa Kanyera, Mfumu Kachindamoto, m’boma la Dedza.

Previous Post

Mlusu unveils first Tonse Alliance K2.2tn budget

Next Post

Chakwera, Nankhumwa akhambitsana

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Chakwera has dissolved 3098 child marriages

Chakwera, Nankhumwa akhambitsana

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.