Sunday, March 7, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Alimbikitsa chitetezo cha okhala m’malire Covid-19

by Nation Online
25/04/2020
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bungwe la Farmers Union of Malawi (FUM) lati pakufunika kulimbikitsa chitetezo cha anthu m’madera akumidzi omwe ali m’malire a dziko lino ndi maiko ena pofuna kupewa kufala kwa matenda a Covid-19.

Mlangizi wamkulu wa bungweli m’boma la Mwanza Caswel Kachingwe adanena izi sabata latha pamwambo wopereka mabeseni, ndowa ndi sopo kumidzi ya kwa mfumu Nthache ndi Govati m’bomalo polimbikitsa anthu kusamba m’manja ngati njira yopewera matendawa.

RelatedHeadlines

Akana ndalama za Covid-19

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

hands ashing | The Nation Online
Nthache (Kumanzere) ndi Kwachingwe (Kumanja)
kusamba m’manja pa mwambowo.

Maderawa, omwe ali m’malire a dziko ndi la Mozambique ndi komwe bungwelo likuchitako pulojekiti yolimbikitsa kadyedwe kabwino.

“Nthendayi yavuta m’maiko oyandikana nawo ngati Mozambique. Anthu a kwa Nthache ndi Govati ayandikana ndi dzikoli moti akhonza kugwidwa ndi mliliwu ngati satetezedwa ndi kulimbikitsidwa kutsata njira zopewera. Tathandiza ndi zinthuzi ndipo tionetsetsa kuti zigwire ntchito popeza kupewa kumaposa kuchiza,” adatero Kachingwe.

Iye adati zipangizozi zikaikidwa m’malo omwe anthu amadutsa kwambiri ndi mokumanirana.

Woona za umoyo m’bomalo Ireen Zuze adavomerezana ndi Kachingwe pa zolimbikitsa chitetezo cha anthu m’maderawo.

“Zipangizo zothandiza anthu kupewa makamaka kuti azisamba m’manja ndi sopo pafupifupi zikufunika. Tikuthokoza FUM pothangatira ntchito yathu yolimbikitsa umoyo wabwino m’boma lino,” adatero Zuze.

Mfumu Nthache idali yokondwa ndi kunena kuti ukhondo uyanja dera lake ndipo chitetezo ku Covid-19 chikula.

Previous Post

‘Pewani chukwu Ku mtedza’

Next Post

Top 5 cure stories presented at the CROI 2020

Related Posts

covid relief | The Nation Online
Nkhani

Akana ndalama za Covid-19

March 6, 2021
Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
Next Post

Top 5 cure stories presented at the CROI 2020

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Won’t libido-boosting pills kill him?

March 7, 2021
Political Uncensored

Pulling rank…

March 7, 2021
People’s Tribunal

Ombudsman has challenged us all

March 7, 2021
Emily Mkamanga

Unattended problems delay progress

March 7, 2021

Trending Stories

  • Lowe: We are trying to find potential markets

    Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SKC ‘intervenes’ on youths’ demos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt, TUM gloves off

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Let the teachers have their Covid-19 risk allowances

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.