Thursday, January 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Alimi alirira Admarc

by Steven Pembamoyo
05/09/2020
in Nkhani
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Lipoti la nthambi yochenjeza anthu za njala ya Famine and Early Warning Network (FewsNet) lati alimi a chimanga akupitirira kulira za mitengo yomwe akugulira chimanga chawo ndi mavenda chifukwa bungwe la Admarc lilibe ndalama.

Lipoti la FewsNet la August 2020 lati chifukwa cha vuto la ndalama ku Admarc komanso potengera kuti makampani opanga zinthu kuchoka ku chimanga achepetsa mlingo wa chimanga chomwe akufuna, alimi ena akugulitsa chimanga chawo  kunja kwa Malawi.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

admarc | The Nation Online
Kugula chimanga ku Admarc ndi ntchito yapadera

FewsNet yati mavenda ambiri omwe akugula chimanagacho akugula pamitengo yotsikitsitsa kuyerekeza ndi mtengo waboma wa K200 pa kilogalamu imodzi.

“Kupatula kuti alimi ambiri adakolola bwino, kwaoneka kuti makampani ambiri omwe amagula chimanga kuti azipangira zinthu achepetsa mlingo ndiye poti Admarc nayo ilibe ndalama, alimi akulowera  kulikonse komwe angamve msika,” latero lipoti la FewsNet.

Koma mkulu wa bungwe la alimi la Farmers Union of Malawi (FUM) Frighton Njolomole wati zomwe zikuchitikazi zikuika dziko la Malawi pachiopsezo chokhala losowa chakudya chifukwa mmalo moti chimangacho chisungidwe ku nkhokwe zake, chikupita kunja.

“Ndondomeko yathu, timadalira kuti Admarc ikagula chimanga kwa alimi, imadzatigulitsa pa mtengo wabwino nthawi ya njala koma ngati Admarc siyikugula chimanga ndipo alimi akugulitsa kunja, njala ikadzabwera mayiko amenewo adzatigulitsa mokwera,” adatero Njolomole.

Iye adati poti alimi ena akadali nacho chimanga, boma lichite changa popereka ndalama ku Admarc kuti igule chimanga chomwe chatsalacho n’kusunga kunkhokwe kuti dziko likhale mpodalira kumbali ya chakudya.

Nduna ya zamalimidwe Lobin Lowe atayendera ntchito zamalimidwe ku Salima adati boma likukonza ndondomeko yodzutsira Admarc kuti alimi azipeza potsamira akakolola mbewu zawo ndipo akufuna kugulitsa.

“Kale mlimi amatha kudziwa ndalama zomwe adzapeze akadzakolola nkugulitsa mbewu zake chifukwa Admarc idali yamoyo ndipo mitengo imatuluka nthawi yabwino choncho, mlimi amatha kudziwa kuti ndikakolola zochuluka mwakuti, ndidzapeza ndalama mwakuti,” adatero Lowe.

Iye adatsimikiza kuti magulu aalimi akhala akupita ku likulu la undunawu kumakadandaula nkhani ya mitengo ya mbewu ndipo adati kulira kwa mtundu umenewu kwatsala pang’ono kutha chifukwa boma lidzutsa Admarc.

Boma likamapanga mitengo ya mbewu, limawerengera zomwe mlimi adalowetsa kuti atulutse kilogalamu imodzi ndipo limawonjezerapo kangachepe kuti kakhale phindu la mlimi kutanthauza kuti mavenda akamagula pamtengo osafika pa mtengo wa boma amakhala kuti akupha mlimi.

Kadaulo pa zamalimidwe Tamani Nkhono-Mvula adaunikirapo kuti mchitidwe uwuwu utabwerezedwa kwa zaka zingapo zotsatana, alimi ambiri akhoza kusiya ulimi chifukwa chosowa mpamba.

“Ngati mlimi ali ndi K1 miliyoni yomwe walowetsa muulimi ndipo chaka choyamba mavenda amubera K200 000 ndiye kuti watsala ndi K800 000. Pakutha kwa zaka zinayi akuberedwa K200 000 chaka chilichonse, mlimi adzakhala opanda ngakhale 1 tambala.

Iye adati mpofunika kuti boma libwezeretse Admarc momwe idalili kale pomwe inkagula chimanga ndi mbewu zonse kuchoka kwa alimi nthawi yabwino chifukwa inkakhala ndi ndalama ndipo alimi ankakhala ndichikhulupiliro kuti akagulidwa mbeu zawo ku Admarc.

Kadaulo pa za ndale Henry Chingaipe yemwe adachita kafukufuku wa ntchito ndi mavuto a Admarc mmalo mwa bungwe la Civil Society Agriculture Network (CisaNet) adapeza kuti bungwe la Admarc likhoza kugwira ntchito bwino litachoka mkhwapa mwa ndale.

Iye adati bungwe ngati la Admarc ndi ndale siziyenderana ndipo zikangololedwa kulowererana, ntchito za kampaniyo zimalowa pansi chifukwa atsogoleri ake amauzidwa zochita ndi andale omwe siziwakhudza ngati kampaniyo ikuyenda kapena ayi.

Mkulu wa kampani ya Admarc Felix Jumbe adati potengera momwe nkhokwe za m’dziko muno zilili, n’kulakwa kwakukulu kugulitsa chimanga kunja ngakhale kuti msika ukupezeka kunjako.

Pofika pa 5 August 2020, Admarc idali itagula matani 35 000 a chimanga pa mtengo wa K200 pa kilogalamu ndi ndalama zokwana K7 biliyoni yomwe idapatsidwa ndi thumba la ndalama za Malawi komanso idagula matani 20 000 owonjezera ndi ndalama zomwe idakongola ku mabanki.

Previous Post

Zotsamwitsa pa kutseguliranso sukulu

Next Post

The poor shortchanged in human trafficking prevention efforts

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Vulnerable: Most women and girls are trafficked from rural areas “to work as prostitutes in urban centres

The poor shortchanged in human trafficking prevention efforts

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.