Sunday, February 28, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Alimi avale dzilimbe, kukubwera El Nino

by Bobby Kabango
25/09/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akatswiri a zanyengo alosera kuti chaka chino pali mantha kuti dziko lino lingakumane ndi nyengo yoipa ya El Nino.

Lipoti la BBC lomwe alitulutsa posachedwapa, zofufuza za ofesi yoona za nyengo ya United Kingdom Met Office zikuonetsa kuti zaka ziwiri zikubwerazi kukhala nyengo yotentha koopsa padziko lonse, zomwe zingapangitse kusintha kwakukulu pa mmene nyengo imakhalira.FARMER

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Nalo bungwe loona za mavuto a njala kummwera kwa kwa Africa la Famine Early Warning Systems (Fews-Net) lati mmene zikuonekera nyengo ya El Nino iyamba mosapeneka October mpaka December.

Tikati tione mmene zakhala zikuchitikira mmbuyo, kukakhala El Niño mvula simagwa mmene anthu amayembekezera ndipo ati chaka chino zigawo za kummwera kwa Mozambique, Malawi ndi Zimbabwe mvula itha kuvutiraponso monga zidachitikira mu 2014/15.

Nyengoyi ikudza pamene chaka chino alimi ambiri m’dziko lino akulira chifukwa cha kuchepa kwa mvula, pamene ena mvula idangogwa yochuluka kwa nthawi yochepa ndipo mbewu zawo zidakokoloka.

Kukakhala El Nino mwina mvula imagwa mosadukiza komanso ikadula mwina kumakhala ng’amba kwa nthawi yaitali, zomwe zimakhudza kwambiri alimi.

M’nyengo zovuta ngati zimenezi, ndi alimi okhawo otsata bwino ndondomeko zamalimidwe amene amapezabe phindu paulimi wawo kukakhala El Nino.

Prof. Moses Kwapata wa kusukulu ya zamalimidwe ya Luanar ku Lilongwe akuti zateremu alimi asagone koma ayambiretu kukonzekera ulimi wa chaka chino.

“Ngati sadamalize kusosa akuyenera apange changu ndipo agalauziretu minda yawo. Zikatere pamafunika kuti mvula yoyamba ikamagwa zonse zakumunda zikhale zatha kuti alimi athe kubzala ndi mvula yoyambirira,” adatero Kwapata pouza Uchikumbe.

“Feteleza aguliretu, ndipo adzaonetsetse kuti amuthira panthawi yake. Ngati m’munda mwamera tchire asachedwetse kupalira. Chilichonse chikhale m’chimake. Mlimi wotere ngakhale nyengo yavuta ndiye amene amakolola.”

Kwapata adati ngati mwayi ali nawo alimi akuyeneranso kulima mbewu zosiyanasiyana chifukwa zina zimafuna mvula yambiri pomwe zina sizikonda mvula yochuluka.

Previous Post

Boma litemera ziweto 10 000

Next Post

Asimba za kasamalidwe ka mpunga

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
Malawi is failing to match Asian countries in production of rice

Asimba za kasamalidwe ka mpunga

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Court has declared Escom a private firm

    Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K1.7bn Chisale assets seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What the hell is APM doing with BJ?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC alleges threats, intimidation from investor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.