Tuesday, January 26, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Alimi samalani pososa

by Bobby Kabango
13/08/2016
in Chichewa
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mlimi weniweni ndiye amasamalitsa kalendala yake ya ulimi. Kuyambira mwezi watha mpaka uno, alimi amalangizidwa kuti akuyenera kuyamba kusosa.

Mlangizi wamkulu m’boma la Chiradzulu, Sheila Kang’ombe wati alimiwa ayenera asamalitse pamene akusosa chifukwa chiyambi chosakolola zochuluka ndi nthawi yososa.

RelatedHeadlines

Amapita kukagula zomwera tiyi

Anatchezera

Odzipha akuchuluka

Kang’ombe adati alimi akuyenera kudziwa kuti mitengo ya thonje ndi fodya siyiyenera kukwiriridwa chifukwa nthawi zambiri imakhala ndi matenda.

Pofotokozapo njira zabwino za kasosedwe, Kang’ombe adati kukwirira mapesi ndi ndondomeko yabwino ya kasosedwe chifukwa kumasunga manyowa.

Alimi angathe kukwirira mapesi ngati awa
Alimi angathe kukwirira mapesi ngati awa

“Mapesi a chimanga mtedza ndi mbewu zina ayenera akwiriridwe, iyi ndi njira yabwino ya kasosedwe chifukwa zikaolerana zimapanga manyowa.

“Ena amakonda kuotcha mapesi, izi siziloledwa koma mitengo ya fodya ndi thonje ndi zomwe ziyenera kuotchedwa. Mapesi achimanga komanso mbewu zina amabweretsa manyowa ngati akwiriridwa,” adatero iye.

Madera ambiri alimi ayamba kale kukwirira koma ena sadayambe monga zilili ku Dedza komwe alimi ali otangwanika ndi kukumba kachewere ndi mbatata ya kholowa.

Sylvester Chitini wa m’mudzi mwa Salile kwa T/A Kasumbu m’boma la Dedza akuti kumeneko alimi sadayambe kusosa komabe mwezi ukudzawu ayambapo.

“Pano ndife otangwanika ndi kukumba mbatata ya kholowa komanso kachewere. Nthawi zonse timayamba mochedwa kusosa kuno. Kumapeto kwa September aliyense akhala wayambapo kusosa,” adatero iye.

M’boma la Blantyre ndi maboma ena alimi ena akumaliza kusosa pamene ena akuyamba kumene. Tomasi Kandodo wa ku Chilomoni akuti sabata ikubwerayi akhala atamaliza kusosa munda wake.

“Kwakukulu ndiye tasosa kale, panopa tangotsala ndi ndime yochepa yomwe sabata ziwiri zikubwerazi tikhala tamaliza,” adatero

Previous Post

Akhumudwa ndi kutsika kwa nandolo

Next Post

Agulitsa chimanga kudziko la tanzania

Related Posts

marriage | The Nation Online
Chichewa

Amapita kukagula zomwera tiyi

January 3, 2021
Chichewa

Anatchezera

January 3, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Odzipha akuchuluka

January 3, 2021
Next Post
Chikulamayembe: Kulankhula ndiye tikulankhula koma ena samamva

Agulitsa chimanga kudziko la tanzania

Trending Stories

  • covid 2 | The Nation Online

    SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Health workers not spared by Covid-19

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • court rebuffs apm on frozen account

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Cometh the hour,Cometh the man

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
My Thought

Spread hope not fear

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.