Tuesday, January 19, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Alipa nkhuku 70 atatayira chimbudzi pachitsime

by Bobby Kabango
30/07/2016
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Gulupu Chinyamula kwa T/A Kamenyagwaza m’boma la Dedza walipitsa amayi awiri nkhuku 35 aliyense chifukwa chotaira chimbudzi pachitsime.

Iye walamulanso kuti nyakwawa Chinyamula alipe nkhuku ziwiri chifukwa milanduyi idagwa m’mudzi mwake.Chicken_farming

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Gulupu Chinyamula adati sabata yatha, mjigo wa m’mudzi mwawo udaonongeka ndipo akulephera kukonza.

Malinga ndi gulupuyu, anthu 1 500 a m’midzi 10 imene ili pansi pake amamwa mjigo umodzi ngakhale akhala akudandaula kwa a mabungwe kuti awakumbire wina. Kaamba ka kuchuluka kwa anthu ogwiritsira ntchito mjigowu, sikuchedwa kuonongeka.

“Aka sikoyamba kuti mjigo uonongeke, wakhala ukuonongeka kuyambira chaka chatha. Pamene waonongeka, midzi yonse imakamwa pachitsime pamene achitira chipongwepo.

“Tsono ulendo uno, pamene anthu anapita kukatunga pachitsimecho, adadabwa kuti munthu wachitiramo chimbudzi. Koma amene adapita mmawa, ataona zofiira m’madzimo, amangoti ndi masamba ndipo adatunga ndi kukagwiritsira ntchito madziwo,” adatero gulupuyu.

Iye adati anthu amene adabwera pachitsimepo dzuwa litatuluka ndiwo adazindikira kuti pachitsimepo wina wachitira chimbudzi.

Nyakwawa Chinyamula adati anthuwo adamuitanitsa kuchitsimeko ndipo idadzionera yokha kuti idali ndowe ya munthu. Kodi adaidziwa bwanji?

“Ine ndisadziwe chimbudzi cha munthu? Amene adatungawo adandionetsa ndipo ndidatsimikiza chifukwa pa nthawiyo nkuti isadasungunuke,” idatero nyakwawayo.

Nkhaniyo itapita kwa gulupu Chinyamula, iye akuti adaopseza kuti ayenda ndi chimbudzicho kwa ng’anga kuti amene wachitayo aone mbonaona.

“Tsiku lomwelo padabwera amayi awiri amene adati ndiwo adachita zimenezo. Sadafotokoze bwino chifukwa chomwe achitira izi koma adavomera pamaso panga kuti adakataya chimbudzicho ndiwo,” adatero gulupuyu.

Gulupu Chinyamula wati amaiwo adauza bwalo lake kuti adachita chipongwecho ngati njira imodzi yoti akuluakuku akonze mjigowo mwachangu.

Nkhaniyi itapita kubwalo, gulupuyo adagamula kuti mayi aliyense alipe nkhuku 35. Mayi mmodzi wapereka kale nkhukuzo pamene wina wangopereka nkhuku 15.

“Ndalandira nkhuku 35 kwa mayi mmodzi komanso nkhuku 15 ndipo kwatsala nkhuku 20,” adatero gulupuyu.

Iye wati bwalo lake limaloledwa kulipitsa nkhuku. “Ndine gulupu, nkhani ikafika pabwalo langa, ndimalipitsa nkhuku basi. Bwalo la T/A limalipitsa mbuzi pamene kubwalo la paramount kumagwa ng’ombe,” adatero pamene olakwawo sadapatsidwe mwayi wolipira ndalama akalephera kulipa nkhuku.

“Nkhukuzi tigulitsa ndipo ndalama yake tikonzetsera mjigowu, mafumu anga ndawauza kale za nkhaniyi ndipo ntchito yokonza mjigowu iyamba sabata ikudzayi,” adatero.

Nyakwawa Chinyamula wati anthu asiya kugwiritsira chitsimecho ndipo akumba zitsime zina kumadimba komwe akulima mizimbe.

“Tidaitanitsa wa zaumoyo kuti adzathire mankhwala pachitsimepo koma mpaka pano sadabwere, chomwe tapanga ndikukumbanso zitsime zina kumadimba komwe tikumwa pano,” idatero nyakwawayi.

Amai awiriwo adakana kulankhula ndik mtolankhani wathu za nkhaniyi. n

Previous Post

‘Mmodzi adayenera kusiya ntchito’

Next Post

Our maids, the invaders

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post

Our maids, the invaders

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Laz Chakwera’s Covid-19 strategy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC takes govt to task over Covid-19 strategy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Sports Council board reshuffled

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
Political Uncensored

Maddening chaotic virus

January 17, 2021
Emily Mkamanga

Chakwera has to instill unity

January 17, 2021
People’s Tribunal

Perilous times and the need for accountability

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.