Monday, April 19, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Amalawi abwerera kumsewu

by Steven Pembamoyo
20/07/2019
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Amalawi ena amene akufuna kuti wapampando wa bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah atule pansi udindo, dzulo adachita zionetsero zina m’madera ena a dziko lino.

Polankhula ndi Tamvani kumayambiriro a zionetserozo mumzinda wa Lilongwe, wapampando wa mabungwe omwe akutsogolera zionetsero za dziko lonse la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) Timothy Mtambo adati adakhutira ndi momwe anthu adatulukira kukaonetsa mkwiyo wawo.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

demo mzuzu | The Nation Online

Iye adati: “Zomwe Amalawi achita lero n’zotamandika kwambiri ndipo wakumva akuyenera kumva n’kupanga zomwe eni dziko akufuna. Nkhani yathu yaikulu ndi yomwe ija, Jane Ansah atule pansi udindo chifukwa wasonyeza kulephera.”

Mtambo adati ngati Ansah satula pansi udindo potsatira chionetsero cha dzulo, zionetsero za Lachiwiri ndi Lachisanu sabata iliyonse zipitirira mpaka Amalawi adzayankhidwe.

“Sitigonja ndipo sitikuopa. Tizipanga zionetsero mpaka madandaulo athu amveke ndipo nkhawa zathu ziyankhidwe,” adatero Mtambo.

mzimba | The Nation Online

Zionetserozo zidachitika m’maboma ambiri kuphatikizapo ku Chitipa komwe chifukwa cha mkwiyo, Amalawi adalimbana ndi apolisi omwe amakhazikitsa bata ndipo mwa zina adaphwanya ofesi ya zankhalango m’bomalo.

Ndipo ku Blantyre, otsatira chipani cha DPP ena adamenyedwa ndi asirikali pomwe amafuna kusokoneza ofuna kuyendawo. Kumayambiriro, khonsolo ya mzinda wa Blantyre imaletsa zionetsero ati chifukwa khonsolo ya mzindawo imasankha mfumu ya mzindawo.

Pomwe timasindikiza nkhaniyi dzulo masana, n’kuti zionetsero zili mkati mumzinda wa Mzuzu ndipo tidalandira malipoti kuti ena adaphwanya sitolo ya Chipiku.

Ansah adanenapo mmbuyomo kuti anthu akungovutika kupanga zionetsero chifukwa iye sangatule pansi udindo wake pokhapokha yemwe adamuika pampandopo yemwe ndi Pulezidenti atamuchotsa.

Polankhula sabata yatha otsatira DPP atachita zionetso zosangalala kuti DPP idapambana chisankho, Mutharika adaopseza kuti athana ndi aliyense yemwe azipanga zionetsero.

Sitolo zina zinali zotsekedwa m’mizinda ya Blantyre ndi Lilongwe ndipo makolo ena sadatumize ana awo kusukulu poopa zochitika kumsewu.

M’kalata yomwe idaperekedwa dzulo, anthu ochita chionetserowo adadandaulamo za imfa za anthu 6 omwe amakhudzidwa ndi zachisankho omwe adafa mwadzidzidzi kuchokera pa 21 May tsiku lachisankho.

Kadaulo pa ndale George Phiri adati mfuwu wa Amalawi wamveka mokwanira kudzera m’zionetsero ndipo adati Mutharika ndi Ansah akuyenera kuchitapo kanthu zinthu zisadafike poipa.

Iye adadzudzula mchitidwe woopseza anthu ochita zionetsero ponena kuti kuteroko n’kuwaphwanyira ufulu omwe malamulo adziko lino amapereka kwa anthu.

Avatar
Steven Pembamoyo
Previous Post

Tractorgate: Apology welcome but prosecutions needed

Next Post

DPP’s Wild Ndipo re-elected as Blantyre Mayor

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Ndipo(R): I appeal to my fellow residents to jealously guard the facilities

DPP’s Wild Ndipo re-elected as Blantyre Mayor

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Lilongwe Road | The Nation Online

    OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Traders fall short of Maize export demand

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Caroline Kautsire: English Professor at Bay State College in Boston

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.