Thursday, February 25, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

‘Amayi oyembekezera akulipira k10 000’

by Martha Chirambo
14/04/2019
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kusamvana kwabuka pachipatala cha chaching’ono cha Chikangawa m’boma la Mzimba pamene amayi oyembekezera akulipiritsidwa K10 000 pokabereka.

Amayiwo omwe auza Msangulutso ati ndi odabwa kuti mwana akangobadwa, achipatala akumalamula kholo lake kuti lilipire K10 000.

RelatedHeadlines

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Aphungu akumana lolemba

Ndi ana omwe akudzipha

pregnant women | The Nation Online
Amayi oyembekezera akulipira K10 000 ku Chikangawa

“Kulibe komwe tingathawire, chipatala chathu ndi chimwechi, sitikudziwa ngati boma lakhazikitsa malamulo woti tiyambe kulipira m’zipatala tikakabereka. Kudabwitsa kwake sakumatipatsa malisiti tikabereka,” adatero mayi wina amene adakana kutchulidwa.

Koma mkulu woona za umoyo m’boma la Mzimba, Lumbani Munthali adavomera kuti amayi akumalipira koma izi zikuchitika kutsatira malamulo amene anthu ozungulira chipatalacho adagwirizana.

Iye adati anthuwo adagwirizana kuti mayi aliyense amene sapita kuchidikiriro (kukadikirira pamene masiku ake obereka ayandikira) azipereka K10 000.

“Cholinga chathu ndichoti amayi azipita msanga kuchipatala osati kudikira matenda ayambe chifukwa ena amapezeka kuti aberekera panjira kapena kunyumba. Ndalamayo imagwira ntchito zosiyanasiyana pachipatalapo,” adatero.

Munthali adatsimikizanso kuti anthuwo sapatsidwa malisiti potsimikiza kuti apereka ndalamayo zomwe zingabweretse mavuto polondoloza ngati ndalamazo zikugwiradi ntchito yoyenera.

“Ndalama iliyonse imafunika umboni monga lisiti kuti yalipilidwadi, apa tivomereze kuti zimalakwika ndipo ndawauza kuti athane ndi vutolo,” adalongosola Munthali.

Iye adati amayi amene amalipira ndalamayo ndi amene apita mochedwa kuchidikiriro, amene aberekera m’njira kapena amene aberekera kunyumba.

“Amene amakadikirira kuchipatala salipira kanthu akabereka,” adatero Munthali.

Komabe ngakhale mfumu yaikulu Kampingo Sibande ikuti malamulowo akuwadziwa, iyo idati sikudziwa kalikonse ngati anthuwo akuyenera kulipira.

“Ife chindapusa chomwe tidavomereza ndi chokhudza kukwatiwitsa mwana osati izizi,” adatero Sibande.

Iye adati malamulowo pamene amakhazikitsidwa amafuna alimbikitse kuti amayi azipita kuchipatala pamene masiku awo ayandikira.

Izi zikukhumudwitsa amayi oyembekezera. Malinga ndi mayi wina amene wangobereka kumene mwana wa mwamuna pachipatalapo, K10 000 ndi ndalama yambiri yomwe sangayipeze.

“Ngati adali malamulo, ndiye mwina bwezi atatidziwitsa kuti tiyambe kutsala ndondomeko yake. Apapa akutiranga koma osadziwa tchimo lathu. Komanso masiku anowa ndi munthu utiyo wa kumudzi angatulutse K10 000?” adafunsa mayiyo.

Mfumu James Lupeska ya m’deralo idati ngati mayi salipira ndiye kuti pena amabwenzedwa ndikulemberedwa kalata yopita ku chipatala cha boma pa Mzimba kapena chipatala chachikulu cha Mzuzu Central.

“Tidayamba kalekale kulipiraku ndipo amati ndi ndalama zopangira chitukuko pa chipatalapo monga kumanga zimbudzi,” adatero Lupeska. n

Previous Post

Pope offers South Sudan kiss of peace

Next Post

‘Ndidadabwa ndi dzina lake’

Related Posts

Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Parliament in session
Nkhani

Aphungu akumana lolemba

February 19, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Ndi ana omwe akudzipha

February 14, 2021
Next Post
tidakumana 1 | The Nation Online

‘Ndidadabwa ndi dzina lake’

Opinions and Columns

My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

February 21, 2021
Political Uncensored

No longer at ease..

February 21, 2021
Emily Mkamanga

Discipline paramount in government

February 21, 2021
People’s Tribunal

Let OPC be standard for everyone to follow

February 21, 2021

Trending Stories

  • Co-chaired the task force: Phuka (L) and Mwanamvekha

    K780M Dodma Covid-19 feast

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bushiri’s daughters blocked from flying out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Convention In July 2023—DPP

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mathanga, kunje Sue president, MEC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.