Saturday, May 28, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Anatchezera

by ANATCHEZERA
10/04/2016
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Ndimamukonda

Agogo,

Ndinali pachibwenzi ndi mkazi wina ndipo zaka ziwiri zatha pomwe tinasiyana. Pano ali ndi mwana yemwe wabereka mwezi watha ndiye akumabwera kwa ine n’kumati tibwererane. Kodi pamenepa ndithani, agogo? Mkaziyo kunena zoona ndimamukonda, koma pano ndinalimba mtima. Nditani?

Ine Amfumu,

Zingwangwa

Amfumu,

Nkhani yanu ndi yovuta kuitsata bwinobwino chifukwa simukumasula kuti vuto lanu ndi chiyani kwenikweni. Poyamba mwanena kuti mkaziyo munasiyana naye zaka ziwiri zapitazo, munasiyana chifukwa chiyani? Mwati pano mkaziyo akuti mubwererane ndipo inu nomwe mukuti ‘kunena zoona ndimamukonda’. Komanso inu nomwenso mukuti pano munalimba mtima, mukutanthauzanji? Mwatinso mkaziyo ali ndi mwana wa mwezi umodzi, n’chachidziwikire kuti mwanayo si wanu-poti mwanena nokha kuti chibwenzi chanu chidatha zaka ziwiri zapitazo. Apatu, kunena zoona, Amfumu, mayankho muli nawo ndinu. Ngati mkaziyo mukuti mumamukonda, chovuta n’chiyani kuti mubwererane? Koma mukuti mwalimba mtima, kulimba mtima kotani? N’chifukwa chake ndikuti zonse zili ndi inu kuti mubwererane kapena ayi poti zifukwa zake zomwe mudalekanirana mukuzidziwa ndinu. Mwakula mwatha, Amfumu.

 

Akungosereulana nane?

Anatchereza,

Ndili pachibwenzi ndi mtsikana wina amene ndikufuna kukwatira koma zochitika zake zikundidabwitsa. Chaka chatha adandijejemetsa pamene adati ali ndi mimba ndipo amati akufuna achotse chifukwa akuopa makolo ake. Ndidamuuza kuti asayerekeze kuchotsa pathupipo chifukwa ine ndidali wokonzeka kumukwatira, zivute zitani. Kenaka, patapita kanthawi adati amangocheza, alibe mimba. Mwezi wathawu adandiza kuti adakayezetsa magazi ndipo amupeza ndi kachilombo ka HIV ndipo n’kofunika kuti nane ndikayezetse. Kunena zoona, sindinapite kukayezetsa koma ndidangomunamiza kuti ndakayezetsa ndipo sanandipeze ndi kachilombo. Pano wandiuza kuti amangonama, sadakayezetse magazi. Kodi iyeyu ndi mtsikana wotani? Ndipitirize naye chibwenzi?

YB,

Lilongwe

 

Zikomo YB,

Pali zinthu ziwiri: Bwenzi lakolo mwina ndi wokonda kusereula komanso mwina ndi kamberembere. Koma zili ndi iwe kupeza choona chenicheni mwa iye. Koma tiyeni tione mbali zones ziwirizi. Poyamba, ngatidi amakonda kusereula, umuuze kuti pali zina zoti angathe kusereula nawe koma nkhani za mimba ndi HIV si nkhani zosereula nazo. Ngati akufuna aone ngati umamukondadi pali njira zina, osati kunamizira mimba kapena kuti amupeza ndi kachilombo. Kusereulana si kolakwika mukakhala pachibwenzi chifukwa ndi njira ina yokometsa chibwenzi chanucho, koma pali malire. Komanso mwina, monga ndanena, akhoza kukhalanso kamberembere ameneyo. N’kutheka mwina adachotsadi mimba ameneyo. Ngati adaterodi, cholinga chake chidali chotani? Wofuna banja amachotsanso pathupi mwadala? Ayi. Tsono pankhani yokayezetsa magazi, bwanji mutapita kuti mukayezetse limodzi kuti mudziwe momwe mulili nonse? Kwa anthu ofuna banja lansangala, losakaikirana, kuyezetsa magazi ndi njira imodzi yothandiza kuti mudziwe ngati muli ndi kachilombo pena ayi. Mukatere mumadziwa chochita pankhani ya kasamalidwe ka banja lanu.

Previous Post

Repercussions of discontentment

Next Post

Leo Mpulula: Alibe 2 koloko

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post
Mpulula: Ndazitaya

Leo Mpulula: Alibe 2 koloko

Opinions and Columns

Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022

Trending Stories

  • His case heard in UK court: Sattar

    Acb explains Sattar miss

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kwacha gets 25% weaker

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AmaZulu complete signing Gaba

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gone but still in our midst

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Conforzi to invest K8.2bn in PPP venture

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.