Chichewa

Anatchezera

Listen to this article

Akufuna mwana

Gogo,

Ndakhala m’banja ndi mwamuna wanga zaka zisanu, koma wopanda mwana.

Mwamuna wanga amalimbitsa mtima kuti ndisadandaule popeza mwana ndi mphatso yochokera kwa Mulungu, koma abale ake ndi anga sakuimva. Akundivutitsa akuti akufuna mwana.

Nthawi zina akwawo amabwera kudzandiuza kuti ndichoke pakhomopo chifukwa ndilibe phindu.

Nditani?

HGP

 HGP,

Ndiyamike mwamuna wanu kaamba koti ndi munthu wokoma mtima, komanso wachikondi.

Akadakhala amuna ena akadakuvutitsani.

Ndigwirizane ndi mwamuna wanu kuti mwana ndi mphatso ndipo Mulungu amapereka mu nthawi yake osati yathu. Choncho abale a mwamuna wanu ndi abale anu akulakwa kumavutitsani.

Nanga akudziwa bwanji kuti vuto ndinu?

Ndikufuna ndikupempheni kuchita zinthu zitatu. Choyamba, pitani ku chipatala mukawafotokozere vuto lanu.

Chachiwiri, limbani mtima. M’moyo wathu timakumana ndi mavuto osiyanasiyana, koma timayenera kulimba mtima.

Chachitatu, mufunseni Ambuye kuti alowerere pa vuto lanu.

Natchereza

 Akundikana

Gogo,

Ndakhala ndikumufunsira mtsikana wina kwa zaka zitatu tsopano, koma amangondiyankha pompopompo kuti sakundifuna.

Poyamba ndimaona ngati ndimomwe atsikana amachitira mnyamata akawafunsira, koma panopa ndayamba kuda nkhwawa.

Nditani?

BNM

 BNM,

Fupa lokakamiza silichedwa kuswa mphika.

Ngati mtsikanayo akukukanani kuti sakukufunani musamukakamize. Musiyeni.

Mwina mukadakhala ndi chiyembekezo akadakuuzani kuti mumudikire aganize kale, koma kukuyankhani pompopompo kuti sakufuna sikukupereka chiyembekezo chilichonse.

Musadandaule, mudzapeza mtsikana wina wokukondani.

Natchereza

Akuchita nsanje

Gogo,

Mtsikana wina ndinamufunsira ndipo anandikana, koma nditapeza mnzake adandilembera kalata yokhumudwa.

Adandiuza kuti ndimusiye mtsikana winayo ndipange chibwenzi ndi iyeyo.

Ndithandizeni.

DPK

 DPK,

Musalole. Adakukanani ndipo inu mudalimba mtima ndi kupeza mnzake. Nanga akufunanso chiyani?

Musalole kulakwira mtsikana winayo poonetsa kukhulupirika kwa mtsikana amene adakukanani kale ubwenzi.

Natchereza

 Ndikufuna mkazi

Gogo,

Ndine mnyamata wa zaka 26 ndipo ndikufuna mkazi woti ndimange naye banja.

Mkaziyu akhale woti sanaberekepo, komanso wa zaka zosaposa 25.

Ine ndikukhala ku Area 25 mu mzinda wa Lilongwe ndipo amene ali wokonzeka kulowa m’banja ayimbe 0990 920 810.

PPK,

Lilongwe

Related Articles

Back to top button