Wednesday, May 25, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Aniva alingalira zosumira boma

by Nation Online
15/11/2020
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Eric Aniva yemwe adaseweza chifukwa chokhala fisi ku Nsanje wati akulingalira zosumira boma pomugwiritsa jere chonsecho amangotsatira chikhalidwe.

Aniva, yemwe adatuluka kundende pa 3 April 2018 atakhala kundende zaka ziwiri atamupeza wolakwa pamlandu wotsata zikhalidwe zoipa. Iye adakhala akuchita za ufisi ndi amayi m’maboma a Nsanje ndi Chikwawa kuyambira mu 1985, ndipo adavomereza kuti adagona ndi amayi oposa 100 ndipo amalandira K5 000 kapena K10 000.

“Atangondigamula kuti ndipite kundende, loya wanga adati achita apilo koma mpaka pano palibe chidachitika. Ndikupempha akufuna kwabwino andithandize kuti chilungamo chioneke chifukwa ndinkangotsatira chikhalidwe chathu basi,” adatero iye.

Padakalipano, Aniva adachoka m’mudzi mwa Chiphwembwe kwa Senior Chief Malemia m’boma la Nsanje ndipo akukhala kwa Mbenje, T/A Ngabu m’nomalo. Iye adakhazikitsa gulu lothandiza kufalitsa mauthenga opewera matenda a Edzi.

Kaliati: Tikakumana kukhoti

“Ndikusowa chithandizo kuti ntchitoyi ndipite nayo patali komanso ndikukhala mwa umphawi,” adatero mkulu wa zaka 54.

Nduna yoona kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo pantchito Patricia Kaliati adati boma ndi lokonzeka kukakumana ndi Aniva kukhoti.

“Amayi ali ndi ufulu wogona ndi aliyense amene iwo angakonde, koma zobisalira ku chikhalidwe n’zachikale ndipo n’zosaloledwa pomwe tili mu ulamuliro wa demokalase,” adatero Kaliati.

Kaliati adati unduna wake uli ndi maloya oimira amayi amene achitiridwa nkhanza. Amayiwo azithandizidwa mwaulele pofuna kuthana ndi nkhanza.

Koma mmodzi mwa anthu a m’deralo, Michael Dansa adati Aniva adangoperekedwa ngati nkhosa.

“Chigamulo chija chidakomera mbali imodzi. Bwanji mafumu ngakhalenso amayi ndi asungwana amene amatsata chikhalidwecho sadatengedwe? Nthawi zinanso ngati fisi angagwira ntchitoyo abale a mkazi atavomereza, onsewo adawasiya bwanji?” adadabwa Dansa.

Iye adati anthuwo amachita kukamupeza pakhomo pawo.

Koma gogo Malemia adanenetsa kuti izo adachita Aniva zidanyazitsa dera lake.

“Ndi ufulu wa aliyense kupita kukhoti kukafuna chilungamo. Komatu Aniva amatsata chikhalidwe cholakwika, n’chifukwa chake bwalo lidamupeza wolakwa litaunikira umboni komanso kupalamula kwake. Inu, munthu n’kumatchedwa bwanji kuti ndi fisi?” idadabwa mfumuyo.

Malemia adati anthu asamabisalire ku chikhalidwe akufuna kuchita zolakwika zimene zingaike ena pachiopsezo chotenga kachilombo ka HIV.”Mafumu timasunga chikhalidwe koma timalimbikitsa chikhalidwe chabwino monga mavalidwe, zakudya, zilankhulo ngakhalenso magule. Koma izi ayi,” adatero iye.

Aniva adapezeka wolakwa pa 22 November ndipo woweruza Innocent NeBi adagamula kuti akasewenze kwa zaka ziwiri, ngakhale iye adaukana mlanduwo.

Woimira boma panthawiyo Chiyembekezo Banda adati Aniva akasewenze chifukwa amatsata khalidwe limene likadaika ena pa chiopsezo chotenga matenda a Edzi.

Michael Goba Chipeta, yemwe adaimira Aniva adapempha bwalo kuti limukhululukire chifukwa chitonzo chomwe adapeza panthawiyo chidali chokwanira.

Previous Post

Men deserve treats, too

Next Post

Politics of nonsense

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post

Politics of nonsense

Opinions and Columns

People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022
Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022

Trending Stories

  • Kalindo: I am hearing it from you

    Kalindo earmarked for diplomatic post

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musicians, fans mourn Martse

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Cooking oil project impresses Chilima

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • APM under pressure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.