Monday, January 25, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Anthu 500 000 sadalembetse

by Steven Pembamoyo
24/08/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zotsatira za kalembera wachisankho m’gawo loyamba ndi lachiwiri zasonyeza kuti anthu 468 860 omwe amayenera kulembetsa sadalembetse nawo m’kaundulayo.

Malingana ndi zotsatira zochokera ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), m’gawo loyamba, anthu 1 094 269 amayenera kulembetsa koma anthu 798 351 ndiwo adalembetsa kuimirira anthu 73 pa anthu 100 aliwonse.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

VOTER REGISTRATION 1 | The Nation Online

M’gawo Lachiwiri, anthu 1 048 080 ndiwo amayenera kulembetsa koma anthu 875 138 okha ndiwo adalembetsa kuimirira anthu 83 pa anthu 100 aliwonse ofunika kulembetsa.

Apa zikutanthauza kuti m’magawo onse awiri, anthu 2142 349 ndiwo amayenera kulembetsa koma mmalo mwake, anthu 1 673 489 ndiwo adalembetsa kutanthauza kuti anthu otsala osalembetsa mmagawowa ndi 468 860.

Mwa anthu omwe adalembetsawa, 901 060 ndi amayi pomwe 771 922 ndi abambo ndipo chiwerengerochi sichidasangalatse chipani chachikulu chotsutsa cha Malawi Congress (MCP) komanso bungwe lowona za ufulu wa anthu la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR).

MCP ndi CHRR adapempha bungwe la MEC kuti liganizire kudzabwereza kalembera mmaboma omwe mudachitika kalemberayu mmagawo awiriwa kuti anthu omwe adatsalirawa adzapeze mpata wolembetsa.

Mneneri wa MCP Rev Maurice Munthali adati kalemberayo ngoyenera kuchitikanso m’maboma omwe adakhudzidwa chifukwa anthu omwe sadalembetse ndi wochuluka kwambiri.

“Sitingasiye anthu onsewa osalembetsa ayi ndiye kuti sitikudziwa chomwe tikupanga. MEC ikuyenera kudzabwerera mmaboma omwe akukhudzidwa mmagawo amenewa,” adatero Munthali.

Mkulu wa bungwe la CHRR Timothy Mtambo adati potengera kulemekeza ufulu wa anthu, mpoyenera kuti kalembera adzabwerezedwe mmaboma okhudzidwawa.

“Anthu ali ndi maufulu osiyanasiyana ndipo umodzi mwa maufuluwo ndi otenga nawo mbali posankha atsogoleri ngati momwe tikuyembekezera chaka cha mawachi. Apapa, zikuonetseratu kuti anthu ambiri sadalembetse kotero ufulu wawo odzasankha atsogoleri waphwanyidwa,” adatero Mtambo.

Mkulu wa MEC Jane Ansah adati kalembera m’magawo oyambirirawa adavuta chifukwa anthu adali asadamve mauthenga bwinobwino komanso padali mavuto okhudzana ndi zipangizo zomwe zimafaifa koma adati mavutowa adatha.

Iye adapempha mabungwe ndi zipani zandale kuti zichilimike kumema anthu kukalembetsa mkaundula kuti akavote nawo chaka cha mawa pachisankho cha patatu.

Mkulu wa bungwe loona kuti zisankho zikuyenda bwino la Malawi Electoral Support Network (Mesn) Steve Duwa adagwirizana ndi Ansah kuti mabungwe ndi zipani zandale athandizirepo kwambiri kumema anthu kukalembetsa kuti chisankho cha chaka chamawa chidzakhale chatanthauzo.

Previous Post

Adzudzula Admarc

Next Post

Abida Mia to contest as MP

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Mia: I understand their problems

Abida Mia to contest as MP

Trending Stories

  • covid 2 | The Nation Online

    SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • court rebuffs apm on frozen account

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Citizens power brings change

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
My Thought

Spread hope not fear

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.