Saturday, July 2, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Anthu 500 000 sadalembetse

by Steven Pembamoyo
24/08/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zotsatira za kalembera wachisankho m’gawo loyamba ndi lachiwiri zasonyeza kuti anthu 468 860 omwe amayenera kulembetsa sadalembetse nawo m’kaundulayo.

Malingana ndi zotsatira zochokera ku bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), m’gawo loyamba, anthu 1 094 269 amayenera kulembetsa koma anthu 798 351 ndiwo adalembetsa kuimirira anthu 73 pa anthu 100 aliwonse.

M’gawo Lachiwiri, anthu 1 048 080 ndiwo amayenera kulembetsa koma anthu 875 138 okha ndiwo adalembetsa kuimirira anthu 83 pa anthu 100 aliwonse ofunika kulembetsa.

Apa zikutanthauza kuti m’magawo onse awiri, anthu 2142 349 ndiwo amayenera kulembetsa koma mmalo mwake, anthu 1 673 489 ndiwo adalembetsa kutanthauza kuti anthu otsala osalembetsa mmagawowa ndi 468 860.

Mwa anthu omwe adalembetsawa, 901 060 ndi amayi pomwe 771 922 ndi abambo ndipo chiwerengerochi sichidasangalatse chipani chachikulu chotsutsa cha Malawi Congress (MCP) komanso bungwe lowona za ufulu wa anthu la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR).

MCP ndi CHRR adapempha bungwe la MEC kuti liganizire kudzabwereza kalembera mmaboma omwe mudachitika kalemberayu mmagawo awiriwa kuti anthu omwe adatsalirawa adzapeze mpata wolembetsa.

Mneneri wa MCP Rev Maurice Munthali adati kalemberayo ngoyenera kuchitikanso m’maboma omwe adakhudzidwa chifukwa anthu omwe sadalembetse ndi wochuluka kwambiri.

“Sitingasiye anthu onsewa osalembetsa ayi ndiye kuti sitikudziwa chomwe tikupanga. MEC ikuyenera kudzabwerera mmaboma omwe akukhudzidwa mmagawo amenewa,” adatero Munthali.

Mkulu wa bungwe la CHRR Timothy Mtambo adati potengera kulemekeza ufulu wa anthu, mpoyenera kuti kalembera adzabwerezedwe mmaboma okhudzidwawa.

“Anthu ali ndi maufulu osiyanasiyana ndipo umodzi mwa maufuluwo ndi otenga nawo mbali posankha atsogoleri ngati momwe tikuyembekezera chaka cha mawachi. Apapa, zikuonetseratu kuti anthu ambiri sadalembetse kotero ufulu wawo odzasankha atsogoleri waphwanyidwa,” adatero Mtambo.

Mkulu wa MEC Jane Ansah adati kalembera m’magawo oyambirirawa adavuta chifukwa anthu adali asadamve mauthenga bwinobwino komanso padali mavuto okhudzana ndi zipangizo zomwe zimafaifa koma adati mavutowa adatha.

Iye adapempha mabungwe ndi zipani zandale kuti zichilimike kumema anthu kukalembetsa mkaundula kuti akavote nawo chaka cha mawa pachisankho cha patatu.

Mkulu wa bungwe loona kuti zisankho zikuyenda bwino la Malawi Electoral Support Network (Mesn) Steve Duwa adagwirizana ndi Ansah kuti mabungwe ndi zipani zandale athandizirepo kwambiri kumema anthu kukalembetsa kuti chisankho cha chaka chamawa chidzakhale chatanthauzo.

Previous Post

Adzudzula Admarc

Next Post

Abida Mia to contest as MP

Related Posts

Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Next Post
Mia: I understand their problems

Abida Mia to contest as MP

Opinions and Columns

My Turn

Following spouse is no crime

July 1, 2022
Rise and Shine

Create your personal brand

June 30, 2022
Business Unpacked

We can do without some levies in fuel price

June 29, 2022
My Turn

US court threatens women’s rights

June 29, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Entrance to one of the VP’s official residences in Blantyre: Mudi House

    New VP houses draw criticism

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Malawi credit Status at risk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Britain squeezes Zuneth Sattar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • 4 DPP MPs disown Nankhumwa injunction

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ex-MPC boss sues for unfair dismissal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.