Wednesday, January 27, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Anthu 6.9 miliyoni alembetsa mavoti

by Steven Pembamoyo
16/11/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zotsatira za kalembera wa mavoti zomwe bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) latulutsa zasonyeza kuti anthu 6 856 295 ndiwo alembetsa m’dziko lonse kuti adzaponye nawo voti chaka cha mawa.

Bungwe la MEC limayembekezera kulemba anthu 8 510 625 m’maboma onse m’magawo onse 8 koma chifukwa cha zovuta zina zomwe bungweli limakumana nazo mkati mwa ndime, anthu 1 654 330 sadalembetse.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

registration 1 | The Nation Online

Pachisankho cha 2014, anthu 7 520 816 ndiwo adalembetsa mkaundula kutanthauza kuti odzavota pachisankho cha ulendo uno akuchepera ndi anthu 664 521 kwa omwe adalembetsa kuti akavote mu 2014.

Koma mneneri wa MEC Sangwani Mwafulirwa wanenetsa kuti chiwerengerochi chikhoza kusintha bungwe la MEC likayamba ntchito ya kalondolondo wa kalembera mmalo onse omwe anthu amalembetserako.

“Izi n’zotsatira zomwe zili m’kaundula potengera mapeto a kalembera koma tiyamba ntchito ya kauni. M’kauni, ena amapezeka kuti adalembetsa kawiri pa zolinga zawo ndiye mayina otero timachotsa kumodzi n’kusiya kumodzi choncho anthu asadzadabwe kudzamva kuti ma figala asintha,” watero Mwafulirwa.

Mwa anthu omwe alembetsawa, 3 045 766 ndi abambo pomwe 3 810 625 ndi amayi ndipo Lilongwe ndiyo yalembetsa anthu ambiri 1 013 414 pomwe Likoma ndilo chimtseka khomo ndi anthu 6 946.

Zina mwa zovuta zomwe bungwe la MEC lidakumana nazo mkati mwa kalembera ndi kuonongeka kwa makina opangira kalembera, kuvuta kwa mphamvu ya

magetsi yoyatsira makina ndikunyanyala ntchito kwa ochita kalembera pofuna malipiro makamaka kumayambiriro.

Mabungwe komanso zipani zotsutsa boma zidapereka nkhawa zawo ku bungwe la MEC zokhudza kutsika kwa chiwerengero cha anthu olembetsa ndipo adapempha kuti ngati nkotheka, kalembera akuyenera kudzabwerezedwa m’madera ena omwe zidanyanya.

“Zotsatira za kalembera sizikukhala zabwino koma si vuto la anthu chifukwa akupita mmalo molembetsera koma akubwerera. Bungwe la MEC likuyenera kuchitapo kanthu kuti kalembera adzabwerezedwe,” adatero mneneri wa Malawi Congress Party (MCP) Reverend Maurice Munthali.

Mkulu wa bungwe loona za ufulu wa anthu la Centyre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) Timothy Mtambo adati kupanda kupereka mpata wina wa kalembera n’kuphwanya ufulu wa anthu.

Mawu a Mtambo akutanthauza kuti ufulu wodzaponya voti wa anthu 1 654 330 omwe sadalembetse waphwanyidwa ndipo akuyenera kupatsidwa mpata

wolembetsa kuti nawo adzakhale ndi danga loponya voti.

Kalembera wa m’kaundulayu ndi gawo limodzi la zokonzekera chisankho cha 2019 koma bungwe la MEC silidabwere poyera nkunena ngati liganizire pempho lobwereza kalembera kapena ayi potsatira pempho la mabungwe ndi zipani.

Previous Post

Escom explores alternative power supply sources

Next Post

‘Kasanthuleni za chisankho’

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
PARLIAMENT | The Nation Online

‘Kasanthuleni za chisankho’

Trending Stories

  • Mlusu presents the budget in this file photo

    Budget off rails

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • New mashup draws mixed reactions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Donors up game in Covid-19 fight

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Spread hope not fear

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

When schools become inaccessible, a glimmer of hope in a coding boot-camp

January 27, 2021
My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.