Thursday, March 4, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Aphungu akana makondomu aulere

by Steven Pembamoyo
04/10/2020
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Aphungu a Nyumba ya Malamulo Lachitatu adabweza mphatso ya makondomu 206 000 yomwe bungwe la Aids Health Foundation (AHF) lidapereka kunyumbayo.

Aphunguwo adakhumudwa ndi zomwe adanena wapampando wa komiti ya zaumoyo Maggie Chinsinga kuti aphungu, ogwira ntchito kunyumbayo komanso alendo amagwiritsa ntchito makondomu 10 000 pa mwezi.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Parliament 2 | The Nation Online

Koma Lachitatu, aphungu a mbali zonse ziwiri ya boma ndi yotsutsa adanyangala ndi lipotilo lomwe adati ndi lochotsa ulemu komanso lonyazitsa ndipo adagwirizana zobweza mphatso yamakondomuyo.

Wachiwiri woyamba kwa sipikala wa nyumbayo Madalitso Kazombo sadapereke chigamulo chake pamtsutsowo, aphungu osiyanasiyana adapereka maganizo awo osonyeza kunyansidwa.

Pomaliza pa nkhaniyo, Kazombo adavomerezana ndi aphunguwo kuti mawu omwe adanenedwawo adachepsa ulemu wa aphungu ndipo adati mphato yamakondomuyo ibwezedwe komanso Chinsinga apepese.

Mkulu wa bungwe la AHF Triza Hara adati adapereka mphatso ya makondomuyo pofuna kuteteza aphungu, ogwira ntchito ku nyumbayo komanso alendo.

“Aliyense mwa iwo ayenera akhale ndi mpata umenewu odziteteza ku matenda,” adatero Hara.

Malingana ndi Chinsinga, mmbuyomo, nyumbayo imalandira makondomu kuchokera kuofesi ya zaumoyo m’boma la Lilongwe koma kenako idapanga ubale ndi bungwe la Partners in Hope.

Previous Post

Dorothy Sulani: Abandoned because of three children with disabilities

Next Post

Akumba manda m’khonde la nyumba

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
manda | The Nation Online

Akumba manda m’khonde la nyumba

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Macra to introduce fees for phone numbers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.