Tuesday, May 17, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Aphungu akumana lolemba

by Steven Pembamoyo
19/02/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Aphungu a Nyumba ya Malamulo ayamba kuunika momwe bajeti ya 2020 mpaka chaka chino yayendera m’miyezi 6 yoyamba Lolemba likudzali kuti aunikire moyenera kusintha ndi kuwongola.

Akadaulo pa nkhani zosiyanasiyana ati aphunguwo aonetsetse kuti mkumanowo waika mtima poongola dziko pa zinthu zingapo zomwe zidaima kapena kubwerera mmbuyo.

Aphungu ayamba mkumano Lolemba

Nyumbayo yalemba patsamba lake la Facebook kuti mkumanowo uyamba Lolemba pa 22 February 2021 ndipo udzatha pa 26 March 2021.

“Mkumanowo udzayenda m’njira ziwiri nthawi imodzi popewa kufalitsa Covid. Aphungu ena azidzakhala m’nyumbamo pomwe ena azidzatsatira pa Intaneti koma onse akuyenera kudzakhala mumzinda wa Lilongwe nthawi yonse,” yatero komiti yokonza ndondomeko ya zokambirana m’nyumbayo.

Matenda a Covid adayambanso kuvuta kumapeto kwa mwezi wa December 2020 bajeti ya 2020/2021 yomwe inkapangidwa matendawa atapola moto itadutsa kale ndipo akadaulo adati asakhale chifukwa cholepheretsa mkumanowo.

Akadaulowo amayankha Tamvani potsatira malipoti awiri otsutsana oti nyumbayo siyitsegulidwa chifukwa cha Covid pomwe lina limati aphungu akumana pogwiritsa ntchito njira zosafalitsa Covid.

Kadaulo pazaumoyo George Jobe adati nyumbayo ilibe chisankho koma kukumana chifukwa ino ndiye nthawi yofunika aphunguwo kukambirana zamavuto omwe ali m’dziko muno.

“Akati kutumikira anthu n’kumeneku. Panopa dziko lili m’mavuto ambiri ofunika bajeti iunikidwenso kuti ikhale ndi njira zothanirana ndi mavutowo,” adatero Jobe.

M’dziko muno muli mavuto monga matenda a Covid, maphunziro adaima, bizinesi sizikuyenda komanso pali mphekesera zoti ndalama zina zothsna ndi Covid sizidayende m’chilungamo.

Mkulu wa bungwe la Center for Democracy and Economic Development Initiative (Cdedi) Silvestre Namiwa adati ngati komiti yoona za kasankhidwe ka adindo m’boma idakwanitsa kukumana pa nkhani ya makomishona awiri a MEC ndiye kuti pali kuthekera koti nyumbayo ikhoza kutsegulidwa.

“Akumane chifukwa pali mafunso ambiri omwe mayankho ake angachokere muzokambirana za aphungu. Pali nkhani zambiri zoti kuyamba kutambasula pano mpakana dzuwa kulowa. Apeze njira yokumanirana kaya pamaso mpamaso kaya pamakina koma akambirane,” watero Namiwa.

Cholinga cha mkumanowu chimakhala kuunika momwe bajeti yayendera pa theka lachaka ndi kusintha moyenera kusinthidwa malingana ndi momwe nyengo ikuonekera.

Kadaulo pa zamaphunziro Limbani Nsapato wati nzachidziwikile kuti bajeti ikuyenera kusintha kuti unduna wa za maphunziro ulandire ndalama zokwanira zolimbana ndi Covid uku sukulu zikuyenda.

“Ophunzira akuyenera kuganiziridwa, n’zachidziwikite kuti apapa bajeti ya za maphinziro ikuyenera kukwera kuti sukulu zitsegulidwe ndiye aphungu akungoyenera kukumana,” watero Nsapato.

Nkhani ina yomwe anthu akuyidandaula pankhondo yolimbana ndi matendawa ndi mchitidwe wa apolisi ena omwe akuti akumenya anthu mwa nkhanza ndipo ena akutengera mphamvu katundu makamaka mmalo ogulitsira mowa akadutsa nthawi yotseka.

Mkulu wa gulu lomenyera anthu ufulu la HRDC Gift Trapence wati aphungu asalephere kukumana ndipo nkhani ya chitetezo makamaka polimbikitsa anthu kutsatira njira zopewera Covid ikakambidwe.

“Apapa akumane ndipo akambirane za malamulo omwe adakhazikitsidwa polimbana ndi Covid ndi kuunikira momwe apolisi ikuyenera angagwilire ntchito yawo,” adatero Trapence.

Nyumbayo inkayenera kutsegulidwa pa 8 February 2021 mpaka pa 15 March 2021 koma zidakanika chifukwa nyengoyo idali yomwe matenda a Covid amafala kwambiri mpaka kupha aphungu ena.

Komitiyo yati pambali pounika momwe bajeti yayendera pa theka la chaka, adzakambirananso bilu yakayendetsedwe ka chuma, bilu yakuima pa yokha kwa Nyumba ya Malamulo ndi malipoti a makomiti.

Previous Post

Tapping shared benefits of Songwe

Next Post

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • A fleet of UTM vehicles: The movement says it is funded by well-wishers

    UTM party vehicle issue goes to MRA

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Firm discovers copper deposits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Embassy assets sold, money untraceable

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DCs face chop

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.