Thursday, March 4, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Aphunzitsi akhala ndi khonsolo

by Steve Chilundu
09/10/2020
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Unduna wa za maphunziro wati ukufuna kukhazikitsa khonsolo ya aphunzitsi yoti izikhazikitsa mwambo komanso kutukula ntchito yauphunzitsi.

Nduna ya za maphunziro Agnes NyaLonje adalengeza izi Lachitatu atatsegulira msonkhano waukulu wokumbukira aphunzitsi komanso sabata yolimbikitsa kuwerenga.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

nyalonje 2 | The Nation Online
NyaLonje: Aphunzitsi atakasuke

Iye adati iyi ndi imodzi mwa njira zomwe boma la Tonse Alliance likufuna kugwiritsa ntchito potukula ntchito za uphunzitsi.

“Boma la Tonse Alliance likufuna kuti aphunzitsi azitakasuka pantchito yawo chifukwa amagwira ntchito yaikulu. Mwaichi, tikukonza zokhazikitsa khonsolo ya aphunzitsi yoti izikhazikitsa mwambo,” adatero NyaLonje.

Koma bungwe la aphunzitsi la Teachers Union of Malawi (TUM) lati silinganenepo kaye kanthu paganizo la bomalo mpaka litamvetsetsa zomwe boma likutanthauza.

Mlembi wamkulu wa bungwe la TUM Charles Kumchenga wati mpofunika kumvetsetsa pomwe zizisiyana mphamvu ndi ntchito za khonsoloyo ndi za TUM.

“Kodi khonsoloyo udindo wake ndi wotani? Zikhonza kusokoneza kuti udindo wake ulowererane ndi wa TUM,” adatero Kumchenga.

Bungwe la TUM limayang’anira aphunzitsi powayimirira makamaka pa nkhani zokhudza madandaulo awo monga kuchedwa kapena kuduphadupha kwa malipiro, kuchedwa kukwezedwa pantchito ndi mavuto ena.

Padakalipano bungwe la TUM likuyimirira aphunzitsi pa nkhani ya ndalama za ukadziotche zomwe aphunzitsi akuti akuyenera kumalandira kaamba kophunzitsa m’nyengo ya Covid-19.

Nthambi zina monga za zachitetezo ndi umoyo, ogwira ntchito amalandira ndalama zaukadziotche zomwe ena zimafika K50 000 pa mwezi.

Pofotokoza bwinobwino za lingaliro la bomalo, NyaLonje adati ntchito yaikulu ya khonsolo ya aphunzitsi idzakhala yokhazikitsa mwambo pa ntchito yophunzitsa.

NyaLonje adatinso boma likukonza ndondomeko yokwezera aphunzitsi m’maudindo polingalira kuti chikwezereni aphunzitsi 25 000 chaka chatha, mipata yambiri ikadali yosatseka.

“Kukweza aphunzitsi tikweza koma zitengapo nthawi chifukwa tikufuna ndondomeko yabwino osati zongoti chulukechuluke ngwa njuchi ayi chifukwa zimapweteketsa ena,” adatero NyaLonje.

Iye adati boma likufuna kuti aphunzitsi azikwera potengera mbiri yawo yauphunzitsi pofuna kuchepetsa mchitidwe oti ena omwe agwira ntchito zaka zochepa azipezeka kuti akwera pomwe ena omwe agwira zaka zambiri ali pamodzimodzi.

Previous Post

UK minister tips Malawi on climate change

Next Post

‘Amalawi dekhani’

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Chakwera has dissolved 3098 child marriages

‘Amalawi dekhani’

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Macra to introduce fees for phone numbers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.