Wednesday, April 14, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

APM alola ansah achoke

by Steven Pembamoyo
22/05/2020
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika dzulo wavomereza kuti wapampando wa bungwe la zisankho la Electoral Commission (MEC) Jane Ansah atule pansi udindo wake.

Ansah Lachinayi adalengeza kuti adalembera Mutharika kuti akufuna kutula pansi udindowo potsata malamulo, osati kuopa zionetsero. Koma iye adaonjeza kuti Mutharikayo adali asanayankhe.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Ansah | The Nation Online
Ansah: Sindikuchoka poopa zionetsero

Koma dzulo, mneneri wa Mutharika Mgeme Kalilani adati adalola Ansah kuti atule pansi udindo wake.

“Mutharika walola kuti Ansah atule pansi udindo. Iye wayamikira Ansah pokhala mmodzi mwa Amalawi okonda kwambiri dziko lawo. Ndikuwafunira zabwino zonse konse angapite,” adatero Kalilani.

Malinga ndi malamulo a dziko lino majaji 6 mu nthambi yolemba ogwira ntchito za malamulo ya Judicial Service Commission ndiwo amasankha munthu amene akhale wapampando wa MEC ndipo mtsogoleri wa dziko lino ndiye amavomereza dzinalo. Mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika adavomereza dzina la Ansah pa 14 October mu 2016 ndipo kontilakiti yake imayenera kudzatha mwezi wa October chaka chino.

Mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa  anthu la Human Rights Defenders Coalition (HRDC) Gift Trapence adati ngakhale Ansah wachoka, zionetsero zimene anakonza kuti makomishona a MEC nawo achoke zipilirabe.

“Tikufuna makomishona onse achoke. Tikufunanso kuti tsiku la chisankho liikidwe posachedwa. Komanso boma lipeze ndalama zimene zikusoweka kuti chisankho chichitike. Ngati Reserve Bank of Malawi idapereka K6 biliyoni kuthumba lothana ndi matenda a Covid-19, zachisankho zingavute pati?” adatero Trapence.

M’sabatayi, mtsogoleri wa chipani cha UTM Party Saulos Chilima adakamang’ala kubwalo la milandu kuti Ansah achotsedwe limodzi ndi makomishona ake. Mmbuyomu, komiti ya Nyumba ya Malamulo yoona zolemba anthu m’maudindo ena a boma adalembera Mutharika kuti achotse makomishonawo koma Mutharika adakana kutero.

Padakalipano, oimira Chilima adapempha mkulu wa majaji Andrew Nyirenda kuti alole mlanduwo umvedwe m’bwalo lounikira malamulo aakulu a dziko lino la Constitutional Court.

Polankhula ndi mtolankhani wathu dzulo, woimira Chilima, Chikosa Silungwe adati kaya Ansah atula pansi udindo kaya satula, mlandu wawo ukupitirira.

“Mumvetsetse. Ifetu tikufuna bwalo lilingalire zochotsa makomishona osati Ansah yekha. Mlandu ukadalipo,” adatero Silungwe.

Mneneri wa UTM Party Joseph Chidanti Malunga adati adagwirizana ndi ganizo la Ansah. “Koma wachita izi mochedwa zinthu zitathina kale,” adatero Malunga.

Avatar
Steven Pembamoyo
Previous Post

Businesses advance digital technologies

Next Post

Mkokemkoke patsiku la chisankho

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Msukwa: There have been changes

Mkokemkoke patsiku la chisankho

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Namadingo | The Nation Online

    Made See needs help—Namadingo

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera wants Malawi Airlines woes resolved

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • NAO concludes K6.2bn audit report

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Billions spent,No safe water

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 measures relaxed, bars open till late

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.