Thursday, May 26, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Apolisi anjatidwa pokhudzidwa ndi ophedwa pa zionetsero

by Staff Writer
11/05/2013
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Apolisi asanu ndi anayi adatengedwa m’sabatayi powaganizira kuti akudziwapo kanthu pa za ena amene adaphedwa pazionetsero za pa 20 Julaye 2012.

Anthu 20 adaphedwa pazionetserozo zomwe Amalawi adachita m’mizinda ya Blantyre, lilongwe, Mzuzu ndi Zomba pokwiya ndi ulamuliro wa yemwe anali mtsogoleri wa dziko lino Bingu wa Mutharika. Pofuna kuletsa zionetserozo apolisi adaombera ena mwa iwo.

Wachiwiri kwa mneneri wa kulikulu la polisi Kelvin Maigwa adati apolisi Lachitatu adamanga Sub Inspector Kamwala wa kupolisi ya Lumbadzi, Sergeant Makokezi wa PMF ku Lilongwe, Sergeant Kanyama wa ku Mchinji ndi Constable Lobo wa kupolisi ya Kawale omwe amasungidwa kupolisi ya Lilongwe.

Ndipo malinga ndi mneneri wa polisi m’chigawo cha kumwera Nicholas Gondwa, ku Blantyre Paul Mussa, Kelvin Nyirenda, Benedicto Dzombe, Mahomed Kulusinje komanso Lemekezo Mikuti, omwe ndi apolisi ya Ndirande, adatsekeredwa powaganizira kuti akukhudzidwa ndi imfa ya anthu awiri ku Ndirande pa zionetserozo.

Apolisiwo amayembekezeka kukaonekera kukhoti dzulo.

Anthu 20 atafa pazionetserozo, Mutharika adakhazikitsa bungwe lofufuza chomwe chidachitika patsikulo ndipo zotsatira zake zidatuluka muulamuliro wa Joyce Banda, pomwe zidaoneka kuti apolisi adalakwa kuombera anthuwo.

Mabungwe oposa 80 adakonza zionetserozo. Zofuna za Amalawi zidayalidwa m’masamba 15 a chikalata chimene chidatulutsidwa.

Zina mwa zolira za Amalawiwo pazionetserozo zidali kusowa kwa mafuta, ndalama zakunja, kubwera kwa bajeti yosadalira ndalama zakunja, kusowa kwa ufulu wa aphunzitsi m’sukulu za ukachenjede komanso kuthamangitsa kazembe wa ku Mangalande kuno ku Malawi.

Previous Post

Distance learning in Third World countries

Next Post

Mawanga sings for the voiceless

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post

Mawanga sings for the voiceless

Opinions and Columns

Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022

Trending Stories

  • Mutharika on the campaign trail in 2019

    APM under pressure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kalindo earmarked for diplomatic post

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nyasa Mobile Limited partners Vodafone

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Blantyre-based artists see off Martse

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.