Friday, January 22, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Asing’anga akuti akonza zionetsero

by Bobby Kabango
10/06/2016
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Asing’anga m’dziko muno akonza zionetsero zokhumudwa ndi chigamulo cha bwalo lalikulu la Mzuzu chopereka chiletso kuti asiye kugwira ntchito yawo powaganizira kuti ndiwo akukolezera mchitidwe wosowetsa ndi kupha anthu achialubino.

Mkulu wa bungwe la asing’anga mu Afrika la Traditional Medicine Council of Africa (TMCA), Steve Chester Katsonga, watsimikiza kuti zionetserozi zichitika sabata ikudzayi mumzinda wa Lilongwe.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Katsonga: Sitibwerera mmbuyo
Katsonga: Sitibwerera mmbuyo

Polankhula ndi Tamvani Lachitatu, Katsonga adati akonza zionetserozi pofuna  kukapereka madandaulo awo kwa mtsogoleri wa dziko lino, Peter Mutharika, kuti apitirize kugwira ntchito yawo mopanda mantha.

Iye wati akonza kuti boma lililonse litumize asing’anga 15 ndipo onse akakumana ku Lilongwe komwe akapereke madandaulo awo kuofesi ya Pulezidenti ndi Kabineti.

Bwalo lalikulu la milandu sabata yatha lidapereka chiletso choletsa asing’anga m’dziko muno koma lidati anthu amene adatenga chiletsocho akuyenera kulengezetsa uthenga woletsa asing’angawo kwa masiku 7 m’nyuzipepala ziwiri zodziwika ndi nyumba ziwirinso zoulutsa mawu zomwe zili ndi omvera ochuluka.

Mpaka pano uthengawo sudayambebe kulengezedwa monga bwalo lidanenera ndipo loya wa anthu amene adatenga chiletsocho, George Kadzipatike, wati ndalama ndi zomwe zawavuta.

“Anthu amene ndikuwaimirira alibe ndalama. Pakufunika pafupifupi K10 miliyoni kuti tilengezere uthengawo, koma tili ndi chikhulupiriro kuti ndalamazi zipezeka ndipo tilengeza momwe khoti lagamulira mpaka asing’angawa ataletsedwa ntchito yawo,” adatero Kadzipatike.

Komabe Katsonga wati pamene akuluakuluwa akuyang’anga ndalama, iwo agwirizana kuti achite zionetsero zamtendere pofuna kuti asaletsedwe kugwira ntchito yawo.

“Mutaonetsetsa, ndondomeko yonseyi sidayende mwadongosolo lake. Angotiganizira kuti tikukhudzidwa ndi kuphedwa kwa maalubino koma palibe umboni kuti zili choncho.

“Komanso mutha kuona kuti, pakakhala madandaulo pa zomwe mwana wachita, umayenera upeze kholo kuti likambirane ndi mwanayo. Asing’anga m’dziko muno ali ndi mabungwe, koma tikudabwa kuti ife sanatidandaulire koma adangopita kukhoti kukatenga chiletso,” adatero Katsonga.

Adapitiriza kunena kuti: “Anthu akupezeka ndi ziwalo, kodi amenewo ndi asing’anga? Komanso kodi anthuwo adawafunsa amene wawatuma? Ngati aulula munthu amene wawatuma, bwanji osamumanga munthuyo?

“Pali zambiri zoyenera kutsatidwa ngati dziko tisanabwere ndi ganizo loletsa asing’anga. Nafenso tikufuna kuthandiza dziko kuti mchitidwe wopha maalubino utheretu.”

Pokambapo nkhani za zionetsero, Katsonga adati akukhulupirira kuti Mutharika ndiye angathandize pa madandaulo awo chifukwa zikalata zomwe ali nazo kuti azigwira ntchito m’dziko muno, zidasaniyidwa ndi mtsogoleri wakale wa dziko lino.

Adati iye: “Bungwe lathu kuti likhazikitsidwe udali mgwirizano wa dziko ndi ifeyo asing’anga. Kamuzu Banda ndiye adasayinira. Izi zikutanthauza kuti mtsogoleri wa dziko lino ndiye angatithandize.

“Ngati mtsogoleri wa dziko angavomereze asing’anga, ndiye muganiza kuti n’zolondola wina kukangotenga chiletso kuwaletsa? Nanga mabungwe ovomerezeka a asingawa azitani?”

Kuphedwa mwachisawawa kwa malubino m’dziko muno, kwachititsa kuti anthu ayambe kuperekera maganizo kuti opha anthuwa nawonso aziphedwa.

Mwa iwo ndi phungu wa Nyumba ya Malamulo ku Mulanje South, Bon Kalindo, amene wati ngati izi sizichitika, iye ayenda chibadwire kusonyeza kukwiya kwake.

Winanso ndi mtsogoleri wa chipani cha Petra Kamuzu Chibambo, yemwe Lachitatu adauza wayilesi ya Zodiak kuti lamulo loti opha anzawo nawo aziphedwa lilipobe m’dziko muno ndipo n’kofunika kuti ligwire ntchito pofuna kuteteza miyoyo ya maalubino.

Koma lipoti lomwe latulutsa bungwe loteteza maufulu a anthu padziko lapansi la Amnesty International (AI) lati silingakhale yankho kuti wopha alubino aziphedwanso.

“Monga Amnesty International, tikutsutsa kwathunthu ganizo lomapha anthu amene akhudzidwa ndi kuphedwa kapena kuzembetsedwa kwa maalubino. Izi ndi nkhanza chifukwa palibe umboni weniweni kuti chilangochi chingathetse nkhanazi,” adatero Deprose Muchena, mkulu wa bungweli kudera la kummwera kwa Afrika (Southern Africa) atabwera kudzacheza m’dziko muno masiku apitawa.

Previous Post

Should education be expensive?

Next Post

Boma libweza moto pa zolipiritsa m’zipatala

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Patients queue in hospital as they await treatment

Boma libweza moto pa zolipiritsa m’zipatala

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

These Freedoms

Where is God in the Malawi Vision 2063?

January 22, 2021
Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.