Friday, January 15, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Ati boma lisabweze ndalama ku FDH

by Bobby Kabango
24/06/2016
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Anthu ena otsata mmene zinthu zikuyendera m’dziko muno aopseza kuti akonza zionetsero ngati boma limvere zonena za banki ya FDH kuti libwezeko K1.1 biliyoni mwa ndalama K9.5 biliyoni zomwe adagulitsira banki ya Malawi Savings Bank (MSB).

Sabata yatha zidadziwika kuti banki ya FDH yalembera boma kuti libweze ndalamazi ponena kuti padali zingapo zomwe sadaunikire bwino panthawi yogulitsanayo.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

CFTC has just approved the merger of MSB and FDH Financial Holdings

Koma boma lakana kale kuti silibweza ndalamazo, zomwenso zasangalatsa othirira ndemanga kuti ndalamazi zisaperekedwe.

Mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa ogula la Consumers Association of Malawi (CAMA) John Kapito wati boma lichite zomwe likulankhula.

“Zimatere kuti lero akutiuza kuti sabweza ndalamazo pamene kuseri apanga kale, tazionapo zotere zikuchitika. Pogulitsa bankiyi ife timati sagulitsa atatitsimikizira kuti satero koma mapeto ake tidamva kuti agulitsa.

“Lero boma litha kutilimbitsa mtima kuti sabweza ndalamazo koma mawa mumva kuti abweza kale. Ife tikupempha kuti chonde boma lisatero,” adatero Kapito.

Iye adati boma liganizire kuti zinthu sizili bwino m’dziko muno kumbali ya chuma ndipo ndi kulakwa kuti ndalama zipite m’njira zotere.

“Panopa tili pantchito yopeza ma triliyoni a bajeti ya dziko lino. Ndiye ngati tingapereke ndalamazi anthu akhala pamavuto chifukwa iyi ndi misonkho yathu,” adaonjeza Kapito.

Mu July 2015, boma lidagulitsa MSB ngakhale Amalawi ambiri adachenjeza kuti lisagulitse bankiyi. Koma mathero ake, boma lidagulitsabe bankiyi pamtengo wa K9.5 biliyoni.

Winanso womenyera ufulu wachibadwidwe, Martha Kwataine, wati zomwe zikuchitikazi ndi kubera Amalawi ndipo boma lisayerekeze.

“Banki idagulitsidwa pamtengo wotsika ndi kale, lero akuti tibwezenso ndalama zina, zoona? Ichitu n’chibwana ndipo Amalawi tisalole zimenezi. Ngati boma libweze ndalamazi kumbali ife osadziwa, ndiye timema Amalawi kuti tichite zionetsero chifukwa uku n’kutitengera pamgong’o,” adatero Kwataine.

Dr. Ephraim Chirwa, kadaulo pa zachuma kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, yomwe ndi nthambi imodzi ya Yunivesite ya Malawi, wati apa palibe nkhani chifukwa boma silidaswe pangano lililonse. n

Previous Post

Okwiya aimitsa kumanga njanje

Next Post

Kutambasula nthenda ya kadzamkodzo

Related Posts

Malango: Covid-19 ikadalipo
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Kumpalume: It is a
sad situation

Kutambasula nthenda ya kadzamkodzo

Trending Stories

  • Kamuzu Central Hospital

    Hospitals in crisis

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Treasury pays Chilima, Chakwera lawyers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Locked with hubby’s brother

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt warned on Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bank charges under spotlight

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

In pursuit of development

The workshop mentality

January 13, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 13, 2021
Business Unpacked

Be safe, embrace digital amid Covid-19 surge

January 13, 2021
My Turn

Framework for engaging retired experts

January 11, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

WhatsApp us

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.