Saturday, March 6, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

by Steven Pembamoyo
19/02/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Komiti yotsogolera kulimbana ndi matenda a Covid yalengeza kuti sukulu zonse zitsegulidwe Lolemba likudzali pa 22 February.

Nduna ya zaumoyo Khumbize Kandodo yemwe ndi mmodzi mwa a pampando a komitiyo wati kauniuni wasonyeza kuti mphepo zili bwino kuti sukulu zikhoza kutsegulidwa.

RelatedHeadlines

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Khumbize Chiponda 1 | The Nation Online
Adalengeza kutsegulira kwa sukulu: Chiponda

Akadaulo ayamikira ganizoli koma ati unduna wa za maphunziro ugwiritse bwino ntchito K5 biliyoni yomwe walandira kuchoka pa K17 biliyoni yomwe boma lapeeeka ku nkhondo yolimbana ndi matendawa.

Kadaulo pazamaphunziro Benedicto Kondowe wati kugwiritsa bwino K5 biliyoni polimbana ndi matrndawa, chitetezo chikhoza kukhwima m’sukulu.

Iye wati sipakufunikaso kuti zidzafikenso poti mpakana kutseka sukulu ndi phunziro lomwe dziko laphunzirapo paulendo woyamba ndi wachiwiri womwe.

school covid | The Nation Online

“Zidzakhala zochititsa manyazi kuti sukulu zidzafikenso potseka, apapa ana asokonezeka kale kokwana kwinako ambiri adzangosiya sukulu. K5 biliyoni ikhoza kuthandiza kupewa zimenezo itagwira ntchito bwino,” adatero Kondowe.

Pulezidenti wa eni sukulu zoyima pazokha Joseph Patel adati sukulu zoima pa zokha zidakonzeka kalekale koma zimangodikira lamulo la boma kuti sukulu zitsegulidwe.

“Apapa zakhala bwino chifukwa ife a sukulu zoima pa zokha tidakonzeka kalekale potsatira zomwe boma lidati n’zofunika pasukulu m’nyengoyi,” adatero Patel.

Iye adati chifukwa china choyenera kutsegulira sukulu n’choti ana ndi aphunzitsi omwe adapezeka ndi Covid adachira ndiye chitetezo m’sukulu chidakwera.

Katswiri wina pa maphunziro Limbani Nsapato adati boma likhale ndi chidwi chachikulu pa chitetezo m’sukulu chifukwa matendawa akadzabukanso m’sukulu zidzaonetsa kulephera.

“Boma likhoza kukwanitsa kuteteza ana asukulu ndi aphunzitsi awo ku Covid ndiye sitikuyembekezera kuti tidzamvenso zoti matendawa abuka m’sukulu,” adatero Nsapato.

Pulezidenti Lazarus Chakwera adalamula kuti sukulu zitsekedwe kwa sabata zitatu pa 17 January 2021 m’sukulu zina monga Lilongwe Girls mutabuka matendawa.

Sukuluzo zimayenera kutsegulidwa pa 8 February 2021 koma Chakwera adaonjezera sabata zina ziwiri kuti aonererebe chifukwa n’kuti nthawiyo matendawo atafika pa indeinde.

Aka kadali kachiwiri kutseka sukulu chifukwa cha Covid. Chaka chatha, sukulu zidatsekedwanso kwa miyezi 5 ndipo pomalizira pake asungwana ambiri adapezeka ndi pathupi ndipo ena adakalowa kumabanja.

Previous Post

Aphungu akumana lolemba

Next Post

In favour or not of proportional representation

Related Posts

Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
Next Post
Padambo: Current system downplays 
nationwide support

In favour or not of proportional representation

Discussion about this post

Opinions and Columns

My Diary

Musowa voice missing yet needed

March 6, 2021
Off the Shelf

Off the Shelf 5 years on

March 6, 2021
Back Bencher

Let the teachers have their Covid-19 risk allowances

March 6, 2021
Guest Spot

Ensuring quality education for Malawian girls

March 6, 2021

Trending Stories

  • Chilima reported to have engaged the anti-nepotism group

    Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 vaccine in today

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SKC ‘intervenes’ on youths’ demos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.