Tuesday, May 17, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

by Steven Pembamoyo
19/02/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Komiti yotsogolera kulimbana ndi matenda a Covid yalengeza kuti sukulu zonse zitsegulidwe Lolemba likudzali pa 22 February.

Nduna ya zaumoyo Khumbize Kandodo yemwe ndi mmodzi mwa a pampando a komitiyo wati kauniuni wasonyeza kuti mphepo zili bwino kuti sukulu zikhoza kutsegulidwa.

Adalengeza kutsegulira kwa sukulu: Chiponda

Akadaulo ayamikira ganizoli koma ati unduna wa za maphunziro ugwiritse bwino ntchito K5 biliyoni yomwe walandira kuchoka pa K17 biliyoni yomwe boma lapeeeka ku nkhondo yolimbana ndi matendawa.

Kadaulo pazamaphunziro Benedicto Kondowe wati kugwiritsa bwino K5 biliyoni polimbana ndi matrndawa, chitetezo chikhoza kukhwima m’sukulu.

Iye wati sipakufunikaso kuti zidzafikenso poti mpakana kutseka sukulu ndi phunziro lomwe dziko laphunzirapo paulendo woyamba ndi wachiwiri womwe.

“Zidzakhala zochititsa manyazi kuti sukulu zidzafikenso potseka, apapa ana asokonezeka kale kokwana kwinako ambiri adzangosiya sukulu. K5 biliyoni ikhoza kuthandiza kupewa zimenezo itagwira ntchito bwino,” adatero Kondowe.

Pulezidenti wa eni sukulu zoyima pazokha Joseph Patel adati sukulu zoima pa zokha zidakonzeka kalekale koma zimangodikira lamulo la boma kuti sukulu zitsegulidwe.

“Apapa zakhala bwino chifukwa ife a sukulu zoima pa zokha tidakonzeka kalekale potsatira zomwe boma lidati n’zofunika pasukulu m’nyengoyi,” adatero Patel.

Iye adati chifukwa china choyenera kutsegulira sukulu n’choti ana ndi aphunzitsi omwe adapezeka ndi Covid adachira ndiye chitetezo m’sukulu chidakwera.

Katswiri wina pa maphunziro Limbani Nsapato adati boma likhale ndi chidwi chachikulu pa chitetezo m’sukulu chifukwa matendawa akadzabukanso m’sukulu zidzaonetsa kulephera.

“Boma likhoza kukwanitsa kuteteza ana asukulu ndi aphunzitsi awo ku Covid ndiye sitikuyembekezera kuti tidzamvenso zoti matendawa abuka m’sukulu,” adatero Nsapato.

Pulezidenti Lazarus Chakwera adalamula kuti sukulu zitsekedwe kwa sabata zitatu pa 17 January 2021 m’sukulu zina monga Lilongwe Girls mutabuka matendawa.

Sukuluzo zimayenera kutsegulidwa pa 8 February 2021 koma Chakwera adaonjezera sabata zina ziwiri kuti aonererebe chifukwa n’kuti nthawiyo matendawo atafika pa indeinde.

Aka kadali kachiwiri kutseka sukulu chifukwa cha Covid. Chaka chatha, sukulu zidatsekedwanso kwa miyezi 5 ndipo pomalizira pake asungwana ambiri adapezeka ndi pathupi ndipo ena adakalowa kumabanja.

Previous Post

Aphungu akumana lolemba

Next Post

In favour or not of proportional representation

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Padambo: We have not been advised

In favour or not of proportional representation

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • Cleared of any
wrongdoing: Suleman

    PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UTM party vehicle issue goes to MRA

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Firm discovers copper deposits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Embassy assets sold, money untraceable

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DCs face chop

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.