Tuesday, March 2, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Bajeti yadutsa, koma m’zikhomo

by Steven Pembamoyo
16/10/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Nyumba ya Malamulo Lachitatu idavomereza bajeti ya K2.2 triliyoni ya chaka cha 2020 mpaka 2021 aphunguwo atayikambirana kuyambira Lolemba.

Bajetiyo yakwera kuchoka pa K1.7 triliyoni mu 2019 mpaka 2020 ndipo ndi bajeti yoyamba ya boma latsopano la Tonse Alliance lomwe akutsogolera Lazarus Chakwera ndi wachiwiri wake Saulos Chilima.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Mlusu 2 | The Nation Online
Adayembekezera zokhoma: Mlusu

Nduna ya zachuma Felix Mlusu adalengeza bajetiyo sabata 5 zapitazo ndipo aphungu adali ndi sabata ziwiri zounika bajetiyo m’makomiti asadayambe kupereka maganizo awo.

Popereka maganizo awo, aphungu osiyanasiyana adaunikira magawo omwe bajetiyo sitidaganizire mokwanira ndipo adapempha Mlusu kuti alingalile magawowo.

Ambiri mwa aphunguwo omwe adali makamaka a mbali yotsutsa adaunikira Mlusu kuti aonjezere ndalama ku maunduna ndi nthambi zina za boma.

Zina mwa nthambizo ndi Nyumba ya Boma, ofesi ya Pulezidenti ndi nduna zake, ofesi yolondoloza momwe ndalama za boma zikugwirira ntchito, unduna woona zoti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo komanso chitukuko ndi maunduna komanso nthambi zina.

Phungu wa kummwera m’boma la Chitipa Werani Chilenga adadabwa kuti Mlusu samaonetsa chidwi chofuna kuonjezera zomwe aphunguwo amanena m’bajeti.

Chilenga adati: “Kodi nduna ya zachuma ikufuna tizingovomera zonse zomwe zili m’bajeti? Nanga bwanji sakusintha kalikonse? Ngati akufuna kuti tingovomera bajeti popanda kuunikira atiuze tikhoza kupanga zimenezo lero lomwe.”

Mlusu adavomeleza kuti aphunguwo adamufinya kwambiri pa nkhani ya ndalama zopita m’maunduna ndi nthambi zosiyanasiyana za boma.

“Ndimayembekezera kufinyidwa koma ndidalimba nazo kuwakumbutsa aphungu za komwe tikuchoka ndi momwe thumba lathu lilili. Ndawatsimikizira kuti tiziunika zinthu pang’onopang’ono malingana ndi mmene tizipezera,” adatero Mlusu.

Polankhula mmalo mwa chipani chachikulu chotsutsa cha Democratic Progressive (DPP) Joseph Mwanamvekha yemwe adali nduna ya zachuma m’boma la chipanicho adasambwadza bajetiyo kuti ndi ya njenjete yongodya yosalabadira chitukuko.

“Mukaunika bajetiyo mofatsa, muona kuti siikukhudza kwambiri zotukula ntchito za malonda ngakhale kuti timayenera kuika mtima ku malondako potengera momwe ntchitozo zalowera pansi ndi Covid,” adatero Mwanamvekha.

Mu bajetiyo, boma lakonza zoti K1.679 triliyoni igwire ntchito za malipiro a ogwira ntchito m’boma, kuthandizira nthambi za boma zomwe zimalandira thandizo kuchoka kuboma, kulipira chiongola dzanja cha ngongole za boma ndi ntchito zina zotumikira anthu.

Malingana ndi bajetiyo, K511.2 biliyoni ndiyo yaikidwa kuti igwire ntchito zachitukuko ndipo mwa ndalamazo, K410.3 biliyoni ndi yazitukuko zodalira ndalama zakunja pomwe zitukuko zodalira ndalama za misonkho zalandira K100.9 biliyoni.

Mwa zinthu zikuluzikulu zomwe Amalawi ena anyadira m’bajetiyo ndi kukwera kwa ndalama yoyambira kudula msonkho kufika pa K100 000, kukwera kwa ndalama yoyambira malipiro kufika pa K50 000 komanso pulogalamu ya zipangizo zotsika mtengo yomwe mabanja 4.3 miliyoni azigula feteleza pamtengo wa K4 495.

Previous Post

‘Chidodo pamilandu’

Next Post

Hand to mouth

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Maize prices have relatively remained stable in recent months

Hand to mouth

Opinions and Columns

My Turn

Tackling global slowdowns

March 1, 2021
People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021

Trending Stories

  • Olela: We are excited

    K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • We won’t give Up—Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Lhomwe chiefs divided on paramount chief

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.