Tuesday, July 5, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Bingu apepese posathetsa mtima pa sitalaka

by Staff Writer
31/03/2012
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pulezidenti Bingu wa Mutharika akuyenera kupepesa Amalawi pa zokhoma zomwe aziona pomwe ogwira ntchito kumabwalo a milandu amanyanyala ntchito.

Mkulu wa bungwe loona ufulu wachibadwidwe la Malawi Watch, Billy Banda komanso mphunzitsi wa zandale kusukulu ya ukachenjede ya Chancellor College, Joseph Chunga, anena izi m’sabatayi.

Izi zadza pamene ogwira ntchito kumabwalo a milandu adayambanso ntchito zawo m’sabatayi patatha miyezi iwiri ndi theka akunyanyala ntchitozo pokwiya kuti boma limalephera kuwakwezera malipiro chonsecho Nyumba ya Malamulo inavomereza mu 2006.

Koma mneneri wa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Hetherwick Ntaba, wati maganizo a akuluakuluwa ndiopotoka komanso osowa nzeru.

Iye wati nkhani yomwe idalipo kudali kusamvana maganizo pakati pa mbali ziwirizi, kotero mbalizo zidakambirana ndikupeza mayankho ndipo boma silolakwa.

Koma Banda ndi Chunga ati Mutharika amangoonerera monse mmene anthu amaphwanyiridwa ufulu.

Iwo atinso ndibwino kuti ena apite kubwalo kukasumira boma kaamba kophwanyiridwa ufulu wawo wofuna chilungamo kumabwalo.

Mwa zovuta panthawiyi, iwo ati ena afera m’ndende kapena kukhala mopanikizika ndipo ichi n’chifukwa chokwanira kuti mtsogoleri wa dziko lino apepese mtundu wa Amalawi.

“Boma livomereze kuti zinthu sizidali bwino. Anthu akhoza kusumira boma pazimenezi. Kwachitika zambiri monga ziphuphu za belo komanso ena adwala ndikufa m’ndende,” adatero Banda.

Iye adati ndibwino amabungwe omwe siaboma akhalirane pansi ndikupeza thandizo kuti atolere zomwe zimachitika pomwe mabwalo adali otseka.

Chunga akuti monga atsogoleri ena anzeru amachitira m’maiko akunja, kukadakhala kwanzerunso Mutharika akadapepesa koma chachidziwikireni n’kuti sangayerekeze.

Iye wati anthu alisumire boma kaamba kowaphwanyira ufulu.

“Zingakhale bwino ena atasuma. Ngakhale kuli sitalaka kapena ayi komabe pakutha pa maola 48 munthu amayenera adziwe mlandu wake ndipo ngati n’koyenera apatsidwe belo.

“Ena atasuma zingapereke chenjezo kuboma pazomwe zidachitikazo ndipo ena sangadzazichitenso,” watero Chunga.

Koma Ntaba wati akuluakuluwa asayambe zosokoneza chifukwa nkhani ya mbali ziwirizi yatha ndipo amvana chimodzi.

Iye wati sakuona choti Mutharika apepesere pomwe sadalakwitse.

Limbani Kawombe wa m’mudzi mwa Kachepa T/A Likoswe m’boma la Chiradzulu wati n’chanzeru kuti Mutharika apepese chifukwa omwe adamuvotera amazunzika kundende asadapezeke ndi mlandu.

“Adakayenera kulankhulapo pomwe sitalaka imachitika koma sadalankhule zomwe zazunzitsa Amalawi,” adatero Kawombe.

Mneneri wa omwe amachita sitalakayi, Austin Kamanga wati iwo alibe zonena zambiri chifukwa agwirizana ndi boma kuti awapatsa K40 pa K100 iliyonse ya malipiro awo kuyambira 2006.

Kamanga adati boma lawatsimikizira kuti ndalamazi ayamba kulandira m’mwezi wa Epulo.

Iye adati ena adzalandira zonse pomwe ena azilandira pang’onopang’ono.

Kamanga adati sitalakayi yachulutsa mulu wantchito chifukwa pali milandu yambiri yomwe ikuyenera kukambidwa.

Malinga ndi iye, pangano lawo ndi boma n’kuti agwira ntchito mokhetsa thukuta.

Mabwalo a milandu adasiya kugwira ntchito pa 9 Febuluwale pofuna kukakamiza boma kuti likwaniritse zomwe Nyumba ya Malamulo idavomereza mu 2006 kuti malipirowo akwezedwe.

Zingapo zakhala zikuchitika pomwe anthu amalephera kutenga chiletso cha bwalo, ena amakanika kutulutsidwa pabelo, malipoti akhalanso akumveka kuti angapo amwalira m’chitolokosi akudikira milandu ndipo milandu yambiri yangokhala njiiii!

Ndende za dziko lino zimayenera kusunga oganiziridwa milandu 1 000 koma chiwerengerochi chakwera kufika pa 2 425.

Mneneri wa ndende m’dziko muno, Evance Phiri, wati chiwerengerochi chidakula makamaka m’ndende za Zomba, Chichiri, Mzuzu ndi Lilongwe.

Iye adati padali chiopsezo kuti chakudya chiyamba kusowa m’ndende kaamba ka kuchulukana.

Phiri adaonjeza kuti chiwerengero cha anthu m’ndende chakwana 13 425.

Phiri adati ndende za dziko lino mumayenera kukhala anthu a pakati pa 5 000 ndi 6 000.

Previous Post

Ministry of Health breaches drug procurement rules

Next Post

15 parties to field 1 candidate in 2014

Related Posts

Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Next Post

15 parties to field 1 candidate in 2014

Opinions and Columns

My Turn

Child neglect and street robbery

July 4, 2022
Editor's Note

MPs’ houses to cost taxpayers K60bn

July 3, 2022
My Thought

Women underutilise digital platforms

July 3, 2022
Big Man Wamkulu

Her body count is too high, should I dump her?

July 3, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • APM, Ntaba risk Criminal charges

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Artists revel in presidential awards

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Dubai firm cries foul

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bank questions import substitution rhetoric

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Her body count is too high, should I dump her?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.