Friday, May 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

by Steven Pembamoyo
06/03/2021
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kadaulo pazamalimidwe Tamani Nkhono-Mvula wati boma likhale ndi ndondomeko yokhwima yogulitsira chimanga pa mtengo wa sabuside ngati momwe lakonzera poopa akamberembere.

Mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera adalengeza Lamulungu lapitali kuti boma lake lakonza zogulitsa chimanga kumsika wa Admarc pa mtengo wotsikirako kuti lipulumutse anthu omwe alibe chakudya komanso ndalama zogulira chakudyacho.

Anthu akugula chimanga ku Admarc mmbuyomu

“Ndidakambirana ndi nduna ya zamalimidwe komanso ya zachuma ndipo tidagwirizana kuti panopa chimanga tigulitse pa mtengo wotsikirako kuti anthu asamve kupweteka kwambiri ndi nyengo ya matendayi chifukwa asokoneza ntchito zambiri,” adatero Chakwera.

Koma Nkhono-Mvula wati nthawi zambiri kukakhala chikonzero chotere, mavenda amalowererapo nkugula chimanga chambiri chomwe amadzagulitsanso ku Admarc chikatha kapena kwa anthu pamtengo obowola mthumba.

“Mfundo yanga ndi yoti pakhale ndondomeko yeniyeni ya momwe chikonzerochi chidzayendere apo ayi ganizo labwino ngati ili silidzaoneka phindu lake,” watero Nkhono Mvula.

Iye wati chikonzerochi n’chabwino kwambiri koma zikhoza kukhalanso bwino boma litapeza njira yokhazikika yoti anthu asamakhalenso ndi njala mmalo momadalira njira ya sabuside.

“Chimodzi mwa zifukwa zomwe Admarc idakhazikitsidwira n’kuonetsetsa kuti anthu azipeza chakudya motsika mtengo pakakhala mavuto ngati amenewa a Covid 19 koma sitingamati sabuside pa zipangizo zaulimi kenakonso sabuside pa chakudya ayi. Tikufunika njira yothetseratu njalayo,” watero Nkhono-Mvula.

Mkulu wa bungwe loona za anthu ogula, kudya ndikugwiritsa ntchito katundu la Consumers Association of Malawi (Cama) John Kapito wati chikonzerochi chabwera nthawi yabwino pomwe anthu ambiri ali mmavuto azachuma chifukwa cha corona.

“Zafika nthawi yoyenera chifukwa anthu ambiri akuoneka kuti asowa chakudya ndipo alibe ndalama zogulira chifukwa mwina adachotsedwa ntchito kaamba ka mayendawa kapena bizinesi zawo sizikuyenda,” watero Kapito.

Dziko la Malawi limadalira chimanga ngati chakudya chenicheni chodalirika ndipo alimi ambiri amalima chimanga chakudya komanso chogulitsa.

Zaka zapitazi ntchito ya Admarc idalowa pansi moti anthu amadalira misika ya mavenda akafuna chimanga zomwe zimapangitsa kuti mitengo ya chimanga izikwera kwambiri m’madera ena.

Boma lidapanganso dongosolo yoti bajeti yaboma iziyamba pa 1 April chaka chilichonse kuti mabungwe ngati Admarc azilandira msanga ndalama zogulira chimanga ndi mbewu zina mavenda asadasese nkhokwe za alimi.

Previous Post

Girls suffer as lawmakers await abortion Bill

Next Post

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Opinions and Columns

Business Unpacked

Fixing economy needs action, not rhetoric

May 19, 2022
Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022

Trending Stories

  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCTU pushes for 75% minimum wage hikeof

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Road traffic spot fines on way out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mayors may face ballots

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.