Monday, April 12, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Boma likonzekera Ebola

by Steven Pembamoyo
21/05/2017
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Unduna wa zaumoyo wasonjola komiti yoyang’anira za kapewedwe ndi kuthana ndi matenda a ebola kuti ikhale chile zitamveka kuti matendawa abuka

m’dziko la Democratic Republic of Congo (DRC).

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Ebola screaning at the airport | The Nation Online
Scanning for Ebola

Malingana ndi undunawu, kuyambira mwezi wa April, 2017, anthu 11 apezeka ndi matendawa m’dzikolo ndipo mwa  anthuwa, atatu adamwalira nawo zomwe zikupereka nkhawa kuti akhoza kusefukira m’maiko oyandikana nawo.

Dziko la DRC ndi dziko lomwe maiko osiyanasiyana kuphatikizapo Malawi amatumizako asilikali ankhondo kukathandiza kukhazikitsa bata malingana nkuti mdzikoli muli nkhondo yamgonagona.

Mkulu oyang’anira ntchito zaumoyo mu unduna wa zaumoyo m’dziko muno Charles Mwansambo wati komitiyi yayamba kale kugwira ntchito yake ndipo wapempha anthu kuti agwirane manja ndi komitiyi kuti matendawa asafike m’dziko muno.

“Komiti imeneyo yayamba kale kukumana ndi kukonza ndondomeko zoyenera. Padakalipano tayamba kale kuunika anthu olowa m’dziko muno kuti ngati ali ndi matendawa abwezedwe ndipo mauthenga akumwazidwa moyenera,” watero Mwansambo.

Chikalata chomwe undunawu watulutsa, chikukumbutsa anthu kuti nthendayi ndiyopatsirana ndipo imafala kudzera mu kukhudzana ndi madzi a m’thupi mwa munthu amane ali ndi matendawa kapena zinyama zina zomwenso zimapezeka ndi matendawa.

Icho chati matendawa akagwira munthu, amamva zizindikiro monga kutentha thupi, kufooka, kuwawa kwa minofu, kuwawa kwa mutu ndi zilonda za pakhosi zomwe zimatsatana ndi kutsegula, kusanza, zidzolo ndi kulephera kugwira ntchito bwino kwa chiwindi ndi kapamba ndipo nthawi zina magazi amatsanyukira mkati kapena kunja kwa thupi.

Undunawu wati anthu akuyenera kusamala podwazika matenda omwe akuonetsa zizindikiro za matendawa komanso akuyenera kusamala poika maliro a munthu yemwe wamwalira ndi matenda a Ebola kuti asatengere.

Matenda a Ebola ndi amodzi mwa matenda omwe mankhwala ake sadapezeke mpaka pano ndipo unduna wa zaumoyo wati mankhwala ake aakulu n’kupewa kutenga potsata malangizo a za kapewedwe.

Matendawa adabukanso m’chaka cha 2014 ndipo adasautsa m’maiko ambiri ndi kupha anthu ochuluka koma chifukwa cha kugwirizana kwa maiko kudzera mu thambi ya zaumoyo ya World Health Organisation (WHO), matendawa adagonja. 

Avatar
Steven Pembamoyo
Previous Post

Chilima faces funding squeeze ahead of 2019

Next Post

Akukambirana zolola ana a chi Rasta m’sukulu

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Mwanamanga: Tinkakambirana ndi Bingu

Akukambirana zolola ana a chi Rasta m’sukulu

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Malawi Airlines is yet to post a profit since it took to the skies

    Malawi Airlines faces liquidation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MHC houses risk demolition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Shareholders, Airtel tussle in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MLS wants APM, Muhara property seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Industrial disputes choke IRC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.