Monday, May 16, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Boma lipereka katemera winanso wa polio

by Steven Pembamoyo
11/03/2022
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Womenyera ufulu pa nkhani zaumoyo, a George Jobe akumema makolo ndi onse omwe akusunga ana kuti aonetsetse kuti ana awo alandira katemera woonjezera wa polio yemwe boma liyambe kupereka pa 21 mwezi uno.

Katemera woonjezerayu aperekedwa kwa ana pafupifupi 2.9 miliyoni osachepera zaka 5 m’dziko lino ngati njira imodzi yochepetsera kufala kwa matendawa. Polio adapezeka kotsiriza m’chaka cha 2005 m’Malawi lino.

Izi zikuchitika potsatira kupezeka kwa polio pa mwana wa zaka zitatu ku Lilongwe mu mwezi wa February, zomwe zachititsa kuti boma lilamule kuti ana onse a misinkhu imeneyi, ngakhale omwe adalandira kale katemerayu alandirenso katemera wa polio akayambiranso kulandiritsa.

Ana omwe ali pachiopsezo kwambiri ndi omwe sadalandirepo katemera wa polio komanso omwe adalumphitsapo katemerayu.

A Jobe adati china chimene chikufunika ndi kuuza anthu ngati boma ndi mabungwe za kufunikira koti mwana akalandire katemerayu ndi cholinga choti anawo atetezedwe ku polio, zomwe ndi zotheka kudzera m’katemerayu.

Katemera wa polio-yu amapezeka ku sikelo komwe makolo amapititsa ana awo, ndipo a Jobe adati ana omwe sadalandire katemerayu ndi chifukwa cha kunyalanyaza kwa makolo awo.

“Boma lalengeza kuti pakhala katemera wina wa polio chifukwa choti mwana wina wapezeka ndi polio ku Malawi kuno, ndipo pozindikira kuti pali makolo ena omwe akhala akulumphalumpha kupititsa ana awo ku katemera wa polio, ndi chifukwa chake pabwera kulengeza kumeneku.

“Katemerayu alipo wambiri. M’zipatala zathu katemera wa polio amaperekedwa kanayi. Mwana akangobadwa kumene amalandira polio zero, kenaka polio 1 mpaka 3. Palinso katemera wa chifuwa chachikulu, wa penta, wa chikuku ndi ena,” adatero a Jobe.

Katemera wa polio wakhala akuperekedwa m’dziko lino, ndipo akatswiri pnkhani za umoyo adati Malawi ikuchita bwino ndithu ku mbali yolandira katemera wa polio yu.

Mkulu woona nkhani za katemera mu unduna wa zaumoyo, Dr Mike Chisema ali ndi chikhulupiliro kuti matenda a polio sapitirira kufala potengera kuti ana oposa makumi 8 mwa 100 ali onse m’dziko lino adalandira katemera wa polio kudzera m’ntchito zopereka katemera zomwe undunawu ukugwira.

Iwo adakambanso kuti mwa ana 200 ali wonse ogwidwa ndi polio, mmodzi amalumala nayo ndipo pakati pa ana 5 ndi 10 mwa 100 ali onse ogwidwa ndi nthendayi amatha kutaya miyoyo yawo chifukwa cha kusagwira ntchito bwino kwa njira zopumira.

Posachedwapa, wachiwiri kwa nduna ya za umoyo, a Enock Phale adati boma lichita izi mogwirizana ndi othandiza boma osiyanasiyana. Padakalipano ali pa kalikiliki kudziwitsa mtundu wa Malawi za kubwera kwa katemera owonjezerayu.

Previous Post

Mabishopu akunena zoona—akadaulo

Next Post

Group moves to protect public purse

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Chisale displays a Bible during a previous court appearance

Group moves to protect public purse

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • Chakaka-Nyirenda: The DPP will look into it

    Embassy assets sold, money untraceable

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse cracks suspicions grow

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Two years of nothing but development rallies

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • My wife is a WhatsApp addict

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.