Thursday, March 4, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Boma litemera ziweto 10 000

by Bobby Kabango
25/09/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pofuna kuthana ndi mliri wa matenda a zilonda za m’ mapazi ndi m’mkamwa a ng’ombe omwe agwa m’boma la Chikwawa, boma lakonza zopereka katemera ku ziweto zoposa 10 000 m’chigwa cha Shire posachedwapa.

Mlembi wa unduna wa zamalimidwe, ulimi wamthirira ndi chitukuko cha madzi, Erica Maganga, watsimikizira Uchikumbe kuti boma laitanitsa kale mankhwala a katemerayu kuchoka kudziko la Botswana.cow

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

“Pakalipano mankhwala ali m’njira ndipo akhala akufika tsiku lina lililonse kuti ntchito yopereka katemera iyambike,” adatero Maganga Lolemba.

Iye adati boma lachita machawi poitanitsa katemerayu pofuna kuti matendawa asafalikire m’madera ena komanso pofuna kuteteza ntchito zina za ulimi monga ulimi wa mkaka.

Boma lidakhazikitsa chiletso cha malonda a nyama ndi kutulutsa kapena kulowetsa ziweto m’boma la Chikwawa zitatsimikizika kuti m’bomali mudagwa mliri wa matendawa omwe pachizungu amati Foot and Mouth Disease.

Unduna wa zamalimidwe, ulimi wamthirira ndi chitukuko cha madzi udatsimikiza za mliriwu womwe akuti udasautsa pamalo ena osambitsirapo n’gombe a Mthumba omwe ali m’gawo loyang’anira za ulimi la Mitole EPA.

M’chikalata chomwe Maganga adasayinira sabata yatha, undunawu udati chigodola cha ng’ombe ndi nthenda yovuta kwambiri ndipo imagwira ziweto monga ng’ombe, mbuzi, nkhosa ndi nkhumba komanso nyama zakutchire monga njati.

Potsirapo ndemanga pamliriwu, wachiwiri kwa mkulu woyendetsa ntchito za zaumoyo wa ziweto ndi ulimi wa ziweto, Dr Patrick Chikungwa, adati nthendayi ndi yowopsa kwambiri ndipo ngati yalekereredwa imafala msanga.

Nthendayi imafala kudzera mumpweya, kukhudzana kapena kudya msipu womwe uli ndi tizilombo (virus) toyambitsa matendawa, adatero Chikungwa. Adaonjezera kunena kuti anthunso atha kufalitsa tizilombo ta nthendayi kudzera m’zovala kapena nsapato, koma adati alimi asade nkhawa chifukwa boma likuchita zothekera kuti nthendayi isafalikire madera ena.

Iye adati zizindikiro za nthendayi ndi kuchucha malovu, matuza mkamwa komanso pakati pa zikanamba za miyendo zomwe zimapangitsa kuti ng’ombe izivutika poyenda.

“Ngati mlimi aona zizindikirozi, chomwe ayenerea kuchita n’kupatula ziweto zodwalazi kuti zisakhudzane ndi zimene sizinakhudziwe ndi nthendayi,” Chikungwa adalangiza.

Mkuluyu adati zilondazi zikaphulika zitha kupola pogwiritsa ntchito mankhwala monga ma antibayotiki a ziweto. n

Previous Post

Have you been cured?

Next Post

Alimi avale dzilimbe, kukubwera El Nino

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
FARMER | The Nation Online

Alimi avale dzilimbe, kukubwera El Nino

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Economist warns on teachers’ risk allowance

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.