Sunday, February 28, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Bungwe lilimbikitsa ulimi wa akalulu

by Steve Chirombo
10/10/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Akalulu ndi mtundu wa ziweto zing’onozing’ono zomwe alimi ambiri amanyalanyaza kuweta koma katswiri paulimi wa ziweto zosiyanasiyana, Sute Mwakasungula, wati ulimiwu ndi wopindulitsa.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Mwakasungula, yemwe ndi mkulu wa bungwe lomwe limagwira ntchito ndi alimi a ziweto aang’ono la Small Scale Livestock and Livelihoods Programme (SSLLP) akuti ulimi wa akalulu suboola m’thumba ndipo uli ndi ubwino wochuluka.

Muli chuma: Akalulu savuta kudyetsa
Muli chuma: Akalulu savuta kudyetsa

Kupatula kuchita ndiwo pakhomo, mkuluyu adati akalulu amabweretsa ndalama komanso mlimi amapindula ndi manyowa ochokera m’khola la akalulu ngakhale kuti iye amalowetsa ndalama zochepa.

“Choyamba, akalulu savuta kudyetsa chifukwa amadya zopezeka mosavuta.

Kusamala kwakenso, monga kumanga khola ngakhalenso kunyamula n’kosavuta chifukwa cha msinkhu wake,” adatero Mwakasungula.

Iye adati chisamaliro chakathithi ndiye chinsinsi cha phindu paulimi wa akalulu chifukwa kulephera kutero, akalulu amagwidwa matenda kapena kujiwa ndi zinyama zolusa.

“Khola la akalulu limafunika kukhala labwino. Akalulu amafuna chitetezo chachikulu kunyengo monga dzuwa, mvula ndi kuzizira.

“Amafunikanso chitetezo kunyama zolusa monga njoka, agalu, afisi ngakhalenso makoswe. Komanso safuna kusokonezedwa ndi phokoso,” adatero Mwakasungula.

Iye adati mbewu ya akalulu imapezeka mosavuta m’malo a zaulimi monga kusukulu ya ukachenjede ya Bunda, nthambi za boma zokhudzidwa ndi ulangizi wa zaulimi ngakhalenso alimi ena a akalulu.

Mwakasungula adati nkhani ina yaikulu pa ulimiwu yagona pa katetezedwe kumatenda, makamaka pokhala tcheru nthawi yosankha akalulu oweta.

“Nthawi zonse mlimi ayenera kuonetsetsa kuti akalulu sakuchucha m’mphuno, alibe zilonda m’makutu, kumapazi ndi malo obisika. Mwachidule, pogula akalulu oweta, gulani komwe muli nako chikhulupiriro kuti kulibe matenda,” adatero Mwakasungula.

Mkuluyu adati madzi ndi ofunika kwambiri pankhani yodyetsera akalulu mwakuti m’khola mumayenera kukhala madzi nthawi zonse chifukwa kalulu mmodzi ndi ana ake amamwa malita awiri patsiku.

Iye adaonjeza kuti pali zakudya zina zosayenera kudyetsa akalulu monga zakudya zomwe zaunga ndere, masamba a mbatatesi, masamba a mabilinganya ndi masamba a chinangwa.

Mwakasungula adati pofuna kusintha chakudya cha akalulu, pamafunika kusintha pang’onopang’ono osangoti kamodzin’kamodzi modzidzimutsa chifukwa kuteroko kumasokoneza m’mimba mwa akalulu ndipo akhoza kudwala n’kufa.

Previous Post

Mental maths and good spending choices

Next Post

Who manned the gates?

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post
Migrator: Chande(R) now faces his former team

Who manned the gates?

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021
People’s Tribunal

When blood of citizens is on head of leaders

February 28, 2021

Trending Stories

  • chisale1 | The Nation Online

    Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What the hell is APM doing with BJ?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K780M Dodma Covid-19 feast

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.