Wednesday, January 27, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chakwera, Nankhumwa akhambitsana

by Martha Chirambo
12/09/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Chilinganizo chomwe chidaikidwa pofuna kuti mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera akayankhe mafunso m’Nyumba ya Malamulo chidasanduka mtsutso pakati pa iye ndi mtsogoleri wa mbali yotsutsa boma m’Nyumbayo Kondwani Nankhumwa.

Mtsogoleri wa dziko linoyu adayembekezeka kuti akayankhe mafunso omwe aphungu adali nawo pa zomwe adalankhula Lachisanu sabata latha pa za pamene dziko lino likuyendera.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

chakwera parliament 1 | The Nation Online
Chakwera: Adziwa liti?

Koma atayamba kulankhula m’nyumbayo, Chakwera adaoneka kuti akutsamira kwambiri pa zomwe adalankhula Nankhumwa poyankhapo pa uthengawo.

Mwa zina zomwe adakhudzapo mu uthenga wake m’Nyumbayo, Nankhumwa adafunsa boma kuti lipereke ndalama zapadera kwa aphunzitsi pamene sukulu zatsegulidwansomu ati ponena kuti iwo akuika miyoyo yawo pa chiswe ku nthenda ya Coronavirus (Covid-19) yomwe yavutitsa pa dziko lonse lapansi.

Koma Chakwera adati pa anthu onse, a Nankhumwa sadali woyenera kuti apereke uphungu wa mtunduwu ku boma lake.

“A Nankhumwa adali nduna ya boma m’miyezi itatu yapitayo. Funso n’kumati n’chifukwa chiyani boma lawo silidaike ndondomekoyo m’dongosolo lawo la za chuma?” adatero Chakwera.

Mtsogoleriyo adanyogodolanso Nankhumwa posagwirizana ndi ganizo la boma lofuna kumangira aphungu onse nyumba zokhalamo m’madera omwe iwo amaimira, ati ponena kuti mkulu wosutsa bomayo samalabadira za mavuto omwe anthu a m’dziko muno amakumana nawo.

Koma Nankhumwa—pofuna kuphupha pa mtsutsowo—adayambitsa nkhani ina ya ndale yomwe idaoneka kuti ikhoza kugwedeza mtsogoleri wa dziko linoyo.

Iye adapempha Chakwera kuti auze nyumbayo mwachimvemvemve ngati mgwirizano wa Tonse Alliance—momwe chipani cha Malawi Congress Party (MCP) udagwirizana ndi zipani zina 8 kuphatikizapo cha UTM Party—uli ndi tsogolo.

“Mutiuzenso lero kuti kodi boma mukuyendetsali ndi la MCP kapena Tonse Alliance. Chifukwa tikudabwa kuti anthu ena omwe munkayenda nawo m’nyengo ya misonkhano yokopa anthu lero sakuonekanso. Kodi anthu ngati a Michael Usi, a Khumbo Kachale, ali kuti lero? Mwawataya kapena?” Adafunsa a Nankhumwa.

Koma poyankhapo, Chakwera adati palibe angaphwasule chimvano chomwe chili mu mgwirizano wa zipani za mu Tonse Alliance.

“Ndikumvetsetsa kuti ambiri akuyesa kusonkhezera kugawanika pakati pa ine ndi wachiwiri wanga komanso zipani zonse zomwe zili mumgwirizanowu. Koma sizitheka. Mgwirizanowu adachita kukonza yekha Yehova ndipo palibe angauthetse.

“Komanso ndinene kuti ambiri mwa omwe akutero—monga mkulu wotsutsa bomayu—sadavomereze kuti zinthu zidasintha ndipo Amalawi adawakana n’kusankha utsogoleri wodzipereka omwe wayambikawu. Zimenezi zangoonetseratu poyera kuti Malawi wa lero sangakhulupilirenso atsogoleri omwe sangadalirike pa utsogoleri wotumikira ngati wathuwu,” adatero Chakwera.

Mauwa adadzanso patangopita tsiku limodzi zipani za MCP ndi UTM Party zitatulutsa chikalata chotsimikiza anthu kuti mgwirizano wawo ulibe nthenya.

Chikalatacho chidalembedwa ndi Maurice Munthali komanso Joseph Chidanti Malunga, omwe ndi aneneri ku zipanizo.

Koma polankhulapo pa zochitika kadaulo pa zandale Mustafa Hussein adayamikira Chakwera poonetsa chidwi cholemekeza malamulo a dziko lino.

“Zayamba bwino komabe sizilephera, mpofunikabe kukonza pena ndi pena,” adatero katswiriyo.

Previous Post

Akwapula mphunzitsi wochita ‘chisembwere’

Next Post

Mwawi helps Vixens clinch minor premiership

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Mwawi in action for Vixens

Mwawi helps Vixens clinch minor premiership

Trending Stories

  • Mlusu presents the budget in this file photo

    Budget off rails

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • New mashup draws mixed reactions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Donors up game in Covid-19 fight

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Spread hope not fear

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

When schools become inaccessible, a glimmer of hope in a coding boot-camp

January 27, 2021
My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.