Thursday, January 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chakwera wakwera paphiri

by Steve Chilundu
11/09/2020
in Nkhani
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akadaulo osiyanasiyana ati Pulezidenti Lazarus Chakwera waonetsa chamuna popita ku Nyumba ya Malamulo kukayankha mafunso a aphungu pankhani zokhudza dziko la Malawi.

Lachinayi, Chakwera limodzi ndi wachiwiri wake Saulos Chilima komanso nduna zina za boma adali ku Nyumba ya Malamulo komwe adayankha mafunso omwe aphungu makamaka a mbali yotsutsa adali nawo pa zomwe adalankhula potsegulira mkumano wa aphunguwo wokambirana za bajeti ya 2020 mpaka 2021.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

chakwera parliament2 1 | The Nation Online

Kadaulo pa zamalamulo Ernest Thindwa wati kupatula mayankho a nzeru omwe Chakwera adapereka m’nyumbayo, mtsogoleriyu wasonyeza kuti ndiwokonzekadi kutsata ndi kulemekeza malamulo aakulu a dziko lino.

“Lamulo limati Pulezidenti amayenera kukayankha mafunso pa Sitetimenti iliyonse yotsegulira mkumano wa bajeti ndiye kupita kokhako, waonetsa kuti ndi mtsogoleri otsata malamulo. Komanso tikasanthula momwe adayankhira mafunsowo, adayankha mwa nzeru kwabasi,” adatero Thindwa.

Koma iye adati n’zomvetsa chisoni kuti aphungu ena adataya mpata osowawo pofunsa mafunso opanda pake mmalo mofusa mafunso othandiza kukhuthalitsa Sona.

Naye kadaulo pa kayendetsedwe ka zinthu m’dziko Vincent Kondowe adati kukumana ndi aphungu maso ndi maso n’kuyankha mafunso awo kumasonyeza kuti mtsogoleri ndi wozindikira komanso ali pamwamba pa chilichonse chomwe akuchita.

“Kuyankha mafunso a aphungu maso ndi maso ndi njira yokhayo yomwe aphungu angaonetsetse kuti zinthu zikuchitika pambalanganda kuti aliyense azitha kutsatira. Chakwera waonetsa chitsanzo chenicheni cha demokalase,” adatero Kondowe.

Aka n’kachiwiri kuti Pulezidenti apite ku Nyumba ya Malamulo kukayankha mafunso a aphungu chiyambireni ulamuliro wa zipani zambiri. Bakili Muluzi adapitako kamodzi n’kuleka pomwe Bingu wa Mutharika, Joyce Banda ndi Peter Mutharika onse sadapiteko ku Nyumba ya Malamulo kukayankha mafunso.

Chakwera adayankha mafunso okhudza mbali zosiyanasiyana kuchokera mu Sona ndipo mfundo yake yaikulu adauza Nyumba ya Malamulo kuti aliyense akaika mtima pa malamulo ndi chilungamo, dziko la Malawi litukuka mosavuta.

Chakwera adayamba ndi kuyankha nkhawa za mtsogoleri wa mbali yotsutsa boma m’Nyumba ya Malamulo Kondwani Nankhumwa kenako nkhawa za aphungu payekhapayekha n’kumalizira mafunso ofunsidwa pompopompo.

Zina mwa nkhawa za Nankhumwa zidali ndalama za ukadziotche za aphunzitsi, zodya katatu patsiku, feteleza wa K4 495 pa thumba la makilogalamu 50, nyumba za aphungu, kusunthidwa kwa adindo ena ndi kumanga anthu pazifukwa za ndale.

Koma poyankha Chakwera adati Amalawi ali ndi chikhulupiliro m’boma la Tonse Alliance chifukwa akudziwa kuti likwanitsa zomwe lidalonjeza.

Iye adatinso kumanga nyumba za aphungu kuthandiza kupulumutsa ndalama za boma zomwe zimaonongeka polipira nyumba zobwereka zokhalamo aphunguwo.

“Boma la DPP lidaononga K2.7 biliyoni kulipira nyumba za aphungu muulamuliro wake. Ndalama zimenezi zikadapulumuka pakadakhala nyumba zokhalamo aphungu za boma,” adatero Chakwera.

Pa ndalama za ukadziotche, Chakwera adati Nankhumwa adali nduna miyezi itatu yapitayo ndipo sadaonetse chidwi choika ndalama za ukadziotche za aphunzitsi.

Aphungu osiyanasiyana adafunsa mafunso akukhosi kwawo koma funso lina lalikulu lidachokera kwa phungu wa ku Machinga Likwenu Bright Msaka yemwe adafunsa Chakwera kuti ngati akulemekeza malamulo abwezeretsa alembi omwe adawasuntha?

Chakwera adati palibe chifukwa chowabwezeretsera chifukwa sadalakwiridwe malingana ndi momwe zimakhalira m’boma lililonse kuti ogwira ntchito za boma amatha kusunthidwa bola ngati sadatsike udindo komanso malipiro ndi zolowa zina zili chimodzimodzi.

Mtsogoleriyu adadzudzula maganizo oti akusuntha alembi otsatira chipani cha DPP ponena kuti ngati alembiwo alidi a DPP, sakuyenera kugwira ntchitoyo chifukwa akupanga ndale mosemphana ndi malamulo.

Adatinso anthu asiye kukhulupirira kuti boma likumanga otsatira chipani cha DPP chifukwa akumanga ndi apolisi komanso apolisiwo akumanga anthu omwe amagwira ntchito m’boma ndipo adasokoneza osati a DPP.

Thindwa adati momwe wayambiramu, Chakwera asabwerere mmbuyo koma apitirize kutsatira zomwe lamulo limanena ndipo azipita ku Nyumba ya Malamulo kukayankha mafunso pakakhala kufunika kotero.

Previous Post

Govt gazettes Access to Information Act

Next Post

Okalamba 46 aphedwa zaufiti

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Kadadzera: Policewere investigating

Okalamba 46 aphedwa zaufiti

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Fake injury claims soar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.