Monday, March 8, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Chikondi chidayambira kutchalichi

by Steven Pembamoyo
31/03/2019
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mipingo ina ponyadira chipembedzo chawo imati ‘kupemphera ndi kwabwino kwatidziwitsa awa, awo ndi awo.’ Kukumana kwa mtundu womwewu kudasintha moyo ndi tsogolo la Elisha Mtambo ndi Menala Msiska womwe lero ndi banja.

Elisha yemwe amachokera m’dera kwa mfumu Mwenelupembe m’boma la Chitipa akuti adakumana ndi Menala wochokera m’dera la mfumu Kachulu m’boma la Rumphi m’chaka cha 2015 kutchalitchi ya CCAP ya Sinodi ya Livingstonia ku Area 24 mu mzinda Lilongwe.

RelatedHeadlines

Akana ndalama za Covid-19

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

tidakumana 1 | The Nation Online
Elisha ndi Menela paukwati wawo

Iye adati kupatula kukumana koyamba kutchalitchi, amakhulupilira kuti Mulungu ndiye adawalumikizitsa chifukwa atangowonana mitima yawo idadumpha mwachilendo pambuyo pake, adalonjerana n’kupatsana nambala za lamya pompo.

“Ambiri amadziwa kuti sichophweka kukumana ndi msungwana kapena  mnyamata koyamba n’kulankhulana naye pomwepo mpaka kupatsana nambala za lamya koma ndimo zidakhalira ndiye sindichotsera kuti dzanja la Atate lidayendapo,” adatero Elisha.

Naye Menala wati tsiku lomwe adakumana ndi Elisha kutchalitchi, adamva kugunda kwachilendo mumtima mwake koma pokhala msungwana adayesetsa kugwira thupi lake kuti asawonekere kuti adali kumva mwachilendo m’thupi.

“Munthu aliyense amazidziwa momwe amakhalira kapena kumvera nthawi zonse m’thupi mwake koma patsikuli, ndithu ndidamva mwachilendo makamaka momwe mtima wanga umagundira,” watero Menala.

Elisha wati kuchoka tsiku lokumanalo, awiriwa adakhala miyezi itatu akungocheza palamya kudikira tsiku lomwe onse adakhutira wina ndi mnzake.

“Tsiku lomwe ndidamufunsira, adaseka n’kundifunsa kuti ndidaganiza bwanji potenga nthawi yonseyo. Chilungamo chidali chakuti ndinkafufuza kaye za khalidwe lake,” adatero Elisha.

Iye wati atapereka yankho lakelo, adadzidzimuka Menala naye atamuuza kuti adagwa m’chikondi kalekale tsiku la kukumana kwawo koma sadafune kuonetsera ndipo pamiyezi itatu yomwe amangochezayo, nayenso amafufuza mbiri ya Elisha.

Ngakhale onse adali atamasukirana, Menala sadavomere kutomera kwa Elisha ndipo adamuuza kuti adzamuyankhabe akamaliza kulingalira za mawuwo.

“Ndidavomera maganizo akewo koma eeeeh! adandiyika mundende ya malingaliro usiku ndi usana. Adandilora pakutha pa mwezi wachiwiri, pemene ine ndinkati zanga zada,” Elisha adafotokoza.

Chibwenzi chitayamba mu 2015, akuti awiriwa adagwirizana zoti adzamanga ukwati m’chaka cha 2018 ndipo chibwenzicho chidayenda bwino kwa zaka zitatu zomwe amakonzekera ukwati wawo omwe adamanga pa 7 July 2018 patchalitchi yomwe adakumanirayo.

Menala wati Elisha ndi mwamuna wachikondi, wodziwa kusamala banja lake, woopa Mulungu komanso wopereka chilimbikitso pa nthawi yakufooka muuzimu ndi muthupi kotero kuti amayamika Mulunguyo pomupatsa mwamuna wotero.

Elisha naye adatsindika kuti banjalo adakonza yekha Mulungu, ndipo awiriwo sangasiyane.n

Previous Post

Masalamusi asokoneza maphunziro ku Lunzu

Next Post

Anatchezera

Related Posts

covid relief | The Nation Online
Nkhani

Akana ndalama za Covid-19

March 6, 2021
Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
Next Post

Anatchezera

Opinions and Columns

Search Within

Cut out the religious dogma from Covid-19 vaccines

March 7, 2021
Big Man Wamkulu

Won’t libido-boosting pills kill him?

March 7, 2021
Political Uncensored

Pulling rank…

March 7, 2021
People’s Tribunal

Ombudsman has challenged us all

March 7, 2021

Trending Stories

  • Protesting pay cut: Mathanga

    Court blocks RBM deputy governor salary cut

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • RBM sues Mulli, 4 others

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Police, DPP, ‘ignore’ court order

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.