Sunday, January 24, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Chilango cha kunyonga chiutsa mapiri pachigwa

by Steven Pembamoyo
26/06/2016
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Ndawala yofuna kubwezeretsa chilango choti wopha mnzake naye aphedwe yavumbulutsa maganizo osiyanasiyana pakati pa mafumu, anthu ndi boma.

RelatedHeadlines

Amapita kukagula zomwera tiyi

Anatchezera

Odzipha akuchuluka

Ndawalayi idachitika Lachinayi lapitali mumzinda wa Lilongwe pomwe phungu wa kummwera kwa boma la Mulanje Bon Kalindo adatsogolera khamu la anthu kukapereka chikalata ku Nyumba ya Malamulo chopempha kuti chilangochi chibwerere.

Kumayambiriro a sabata yathayi, ndawalayi isadachitike, nduna ya zofalitsa nkhani Patricia Kaliati idanenetsa kuti boma lilibe maganizo obwezeretsa chilangochi potengera pangano la maiko onse.

Kaumba akaseweza moyo wake  wonse kundende
Kaumba akaseweza moyo wake
wonse kundende

“Dziko la Malawi lidasayina nawo mapangano ambirimbiri okhudza za ufulu wa anthu ndiye sitingabwerere mmbuyo n’kuyamba kuphwanya pangano lomwe tidasayina tokha,” adatero Kaliati polankhula ndi atolankhani ku Nyumba ya Malamulo.

Koma mafumu ena akuluakulu monga Chindi wa ku Mzimba m’chigawo cha kumpoto ndi Kabudula wa chigawo cha pakati adati iwo akuona kuti munthu wopha mnzake akuyenera nayenso aphedwe, osanyengerera.

Chindi adati koma mpofunika kulingalira mofatsa pogamula milandu yotereyi kuti chilungamo chioneke kuti kodi adapha mwangozi kapena dala kuti zilangozo ziperekedwe.

“Kupha kuli pawiri-mwadala ndi mwangozi. Apapa tikhazikike pa wopha mwadala monga momwe opha maalubino amachitira. Amenewa akuyenera kuphedwa basi, osawanyengerera, ayi, chifukwa nawonso sadanyengerere mnzawoyo,” adatero Chindi.

Naye Kabudula adati palibe njira ina yoposa kupha anthu otere chifukwa moyo wawo uli ngati zilombo zolusa zomwe zingaononge mtundu.

Onsewa adasemphana ndi mfumu Chapananga ya ku Chikwawa m’chigawo cha kummwera yomwe idati chilango chakupha si chilango chabwino, bola ndende moyo onse.

“Kwa ine zakuphazo ayi, bola atati opha mnzake azikakhala kundende moyo wake wonse basi,” adatero Chapananga.

Anthu osiyanasiyana omwe adacheza ndi Msangulutso adaperekaso maganizo osiyanasiyana pa nkhani ya chilangochi.

Bernadette Kaonga, wa ku Area 49 mumzinda wa Lilongwe, adati iye sangavomereze kuti anthu aziphedwa. Iye adati njira yabwino n’kupeza njira yoti zophanazo zitheretu kapena, apo ayi, kundende moyo wonse.

Mnzake yemwe adali naye limodzi panthawiyo, Mary Molosi, adati iye akuganiza kuti njira yomwe ingathetse zophanazo ndi chilango chophedwa, basi.

Pa 14 June, 2016, Samson Kaumba wa zaka 33, adakhala munthu oyambirira kupatsidwa chilango chokakhala kundende moyo wake wonse pamlandu wokhudzana ndi nkhanza kwa alubino kubwalo lalikulu la milandu la Mzuzu. n

Previous Post

I need a husband

Next Post

On rabies, stray and minimum household dogs

Related Posts

marriage | The Nation Online
Chichewa

Amapita kukagula zomwera tiyi

January 3, 2021
Chichewa

Anatchezera

January 3, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Odzipha akuchuluka

January 3, 2021
Next Post

On rabies, stray and minimum household dogs

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AG disowns K750m compensation signature

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera has to instill unity

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
My Thought

Spread hope not fear

January 24, 2021
Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.