Sunday, April 11, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chipalamba ku Malawi

by Bobby Kabango
13/10/2017
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Dziko la Malawi likusanduka chipalamba. Kafukufuku wathu wapeza kuti mafumu ndi apolisi ena ndiwo akuthandizira kusambula dzikoli pamene akuthandizira kudula mitengo mosasamala ndi kuotcha makala.

Lidali dziko la nkhalango zowirira. Koma lero, madera ambiri ali mbee! Ukaona mitengo, ndiye kuti ndi pamanda.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Charcoal | The Nation Online
Makala kudikira kuti awatengere kumalonda

Malinga ndi unduna woona zachilengedwe, dziko lino lili pamwamba pa maiko a mu Sadc posakaza mitengo ndipo padziko lonse lapansi, lili pa nambala 4.

Mtolankhani wathu sabata yatha adalowa geni ya makala m’boma la Ntcheu. Uku ndi kumalire a Neno ndi Mwanza.

Iye adapeza anthu ochuluka akuchita bizinesi yootcha ndi kugula makala. Mitengo yambiri yatsala kuderali ndipo amene amapanga makala m’maboma a Mwanza ndi Neno asamukira kumeneko.

Mtunda woposa makilomita 90 umene udali ndi mitengo yambiri yachilengedwe lero ndi mpala. Mitengo yatha ndipo mitengoyi ikugwetsedwa m’malire a Malawi ndi Mozambique.

Mtolankhaniyu atafika, adauzidwa kuti akakumane ndi nyakwawa Kabwayibwayi ya m’boma la Ntcheu yomwe imupatse malo woti agwetse mitengo. Mfumuyo idatsimikiza kuti mitengo ilipo ndipo kuti mtolankhaniyu aotche makala, akuti amayenera kulipira ‘cha nkhalango’.

“Cha nkhalango ndi K2 000,” idatero mfumuyo.

Mtolankhani adauza mfumuyi kuti akufuna apange uvuni zisanu zotalika mamita 20. “Koditu kuli golide [mitengo], ndi zotheka,” idatero mfumuyo.

“Mita imodzi ndi K2 000, ngati mulibe ndalama ndiye mukaphula makalawo mudzapereka matumba atatu [olemera makilogalamu 50 lililonse],” adaonjeza.

Poona kuti zitenga masiku ambiri, mtolankhaniyu adaganiza zogula makala kwa ogulitsa ena kumeneko. Thumba lililonse limagulidwa K2 000.

Kuti thumba lifike ku Blantyre kokagulitsira, umayenera ulipe K2 500 kwa mwini galimoto. Kupatula izi, adatinso ndipereke K300 pa thumba lililonse yomwe imakhala ya apolisi.

“Masiku ambiri timakumana ndi apolisi amene amatilipiritsa. Ndiye timakonzeratu kunoko kuti tisavutike mayendedwe,” amene amathandiza mtolankhaniyo kupanga makalawa, Happy adatero.

Mtolankhaniyo atafunsa Happy kuti pa ‘roadblock’ ya polisi ya Zalewa akalipira chiyani, iye adayankha kuti malowo ngosavuta. Harry adaoda matumba 70.

“Mungomupatsa dalaivala K2 500 ndi K300, ndalamayi imathandiza zonsezi ndipo matumba anu akakupezani ku Blantyre,” adatero.

Anthu onse amene adali ndi makala adapereka ndalama zawo kwa woyang’anira kampuyo pamene iwo adanyamuka ulendo ku Blantyre.

Lachisanu onse amene adakwezetsa makala awo adachoka kumaloko. “Sitiyenda limodzi ndi galimotoyi, adzangotiuza kuti makala afika, tiyeni tibakadikirira ku Blantyre,” adatero Happy.

Sipadatenge nthawi, Loweruka m’ma 3 koloko mmawa, mtolankhaniyu adalandira foni kuti galimotoyo yomwe idanyamula matumba 250 yafika msika wa Khama ku Machinjiri. Onse amene adakweza makalawo adali pamalopo kugulitsa makalawo.

Patsikulo bizinesi simayenda bwino chifukwa thumba lomwe poyamba limagulidwa K9 000, limapita pa K5 000 mpakanso kumafika pa K3 500.

Malinga ndi unduna woona zachilengedwe, pafupifupi mahekitala 3.4 miliyoni aonongeka pootcha makala. Mu June chaka chino, komiti yoona zachilengedwe ku Nyumba ya Malamulo idapempha undunawu kuti uletse kuotcha komanso kugulitsa makala m’dziko muno.

Wachiwiri kwa mkulu wa za nkhalango Ted Kamoto akuti dera la Neno, Ntcheu ndi Mwanza ndi lomwe likutulutsa makala ambiri pakadalipano. “Kumeneko mitengo ikugwetsedwa kwambiri pamene akupanga makala,” adatero.

Malinga ndi Kamoto vuto la kuotcha makala lakulanso kwambiri chifukwa cha kuzimazima kwa magetsi komanso kuchepa kwa chiwerengero cha Amalawi amene amagwiritsa ntchito magetsi pophika.

“Amalawi 85 mwa 100 alionse amagwiritsa ntchito makala ndi nkhuni pophika. Izi zili choncho, 15 mwa 100 ndiwo amagwiritsa ntchito magetsi. Izi zafika pena chifukwa cha kuzimazima kwa magetsi,” adatero iye.

Koma mneneri wa polisi James Kadadzera akuti anthu akuyenera akanene kupolisi ngati wapolisi wina akufuna ziphuphu kuti adutsitse makala.

“Ngatinso akuti akumapereka ndalama ku 997, atiuze nambala ya galimotoyo. Komanso atiuze wapolisi amene walandirayo,” adatero iye.

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

This one is for you mothers

Next Post

Amangidwa popha ‘anamapopa’

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
An illustration of an arrest

Amangidwa popha ‘anamapopa’

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Malawi Airlines is yet to post a profit since it took to the skies

    Malawi Airlines faces liquidation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MHC houses risk demolition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Shareholders, Airtel tussle in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MLS wants APM, Muhara property seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • IMF cancels K9bn debt

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.