Wednesday, April 14, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chipwirikiti pachisankho

by Nation Online
16/05/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pali chipwirikiti pachisankho cha mtsogoleri wa dziko lino, pomwe wapampando wa bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah wapempha Nyumba ya Malamulo kuti isankhe tsiku lochitira chisankhocho.

Izi zikudza pomwe mmbuyomu Nyumba ya Malamuloyo idapempha mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika kuti avomereze chisankhocho chidzachitike pa 19 May. Koma Mutharika adakana kusainira bilo ya nyumbayo, pomwe MEC idaika 2 July ngati tsiku lochitira chisankhocho potengera ndi chigamulo cha bwalo la milandu la Constitutional Court lomwe lidati chisankho chichitike pasanathe masiku 150.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

voting 1 | The Nation Online
Pali mkokemkoke pa za tsiku limene Amalawi angadzaponyenso voti

Popereka lipoti ku mbali zonse zokhudzidwa ndi chisankho la National Electoral Consultative Forum (Necof) ku Mangochi Lachitatu, Ansah adati chigamulo cha bwalo lalikulu la Supreme Court chiyenera kuganizira za miyoyo ya anthu omwe akufuna kuti adzawavotere kuti adzawatsogolere zaka zikudzazi.

“Mtsogoleri sangakhale waphindu ngati anthu omwe akutsogolera akudwala, tsono apa tikukamba za matenda owopsa a Covid-19. Tikamba nawo kuti tione momwe tingathandizirane nawo,” adatero Matemba.

Pomwe katswiri pa ndale Musatafa Hussein adati chomvetsa chisoni n’choti anthu omwe amayenera kutsogolera kupewa matendawa, ndiwo akutsogolera kuphwanya ndondomeko zowapewera.

“Nkhani ili apa ndi ya moyo kapena imfa tsono timayenera kukhala osamala kwambiri. Boma silopusa kuyika ndondomeko koma atsogoleri ndiwo akuyambitsanso kuphwanya,” adatero Hussein.

Nduna ya zaumoyo Jappie Mhango yemwenso akutsogolera komiti yapadera yoyendetsa za kapewedwe ka matendawa adati sakukondwa ndi zomwe zipani za ndale zikupanga.

“Akuganizira zawo zokha ndi cholinga chodzapambana mavoti koma akuyika miyoyo ya anthu pachiswe. Kunena zoona,” adatero Mhango.

Amalawi ena omwe alankhula ndi tamvani ati nawo sakukondwa ndi misonkhanoyo polingalira kuti iwo akulephera kupanga zitukuko chifukwa boma lidaletsa ntchito zina monga mabizinesi.

Matenda a Covid-19 adapezeka koyamba m’dziko la China kumapeto kwa chaka chatha ndipo bungwe la zaumoyo pa dziko lonse la WHO lidalengeza kuti matendawo ndi m’lili wadziko lapansi.

Anthu zikwizikwi amwalira m’mayiko ambiri padziko lonse ndipo M’malawi muno anthu 56 adapezeka ndi matendawo pomwe atatu ndiwo adamwalira.

Dziko la Malawi lidakhazikitsa ndondomeko zopewera matendawo kuphatikizapo kuletsa misonkhano ya anthu oposa 100, kusamba m’manja mwakathithi, kusintha makhalidwe a m’magalimoto, kutseka sukulu ndi kupeleka tchuthi kwa ogwira ntchito zina m’boma.

Padakalipano MEC ikufuna kugula zipangizo zodzitetezera pamene akukonzekera chisankhocho.

Avatar
Nation Online
Previous Post

Andale agundika misonkhano, osapewa Covid-19

Next Post

Covid 19 cases hit 65

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Mhango: The 15 arrived on May 24

Covid 19 cases hit 65

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Namadingo | The Nation Online

    Made See needs help—Namadingo

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera wants Malawi Airlines woes resolved

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • NAO concludes K6.2bn audit report

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Billions spent,No safe water

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 measures relaxed, bars open till late

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.